Eksodo 12 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 12:1-51

Kukhazikitsidwa kwa Paska

1Yehova anayankhula kwa Mose ndi Aaroni mʼdziko la Igupto kuti, 2“Mwezi uno uzikhala mwezi wanu woyamba wa chaka. 3Muliwuze khamu lonse la Israeli kuti pa tsiku la khumi la mwezi uno, munthu aliyense asankhire banja lake mwana wankhosa mmodzi. Banja lililonse litenge mwana wankhosa mmodzi. 4Ngati banja lili lochepa moti silingathe kudya nyama yonse ya nkhosa, ligawane ndi banja lomwe layandikana nalo nyumba. Mabanja adziwiretu chiwerengero cha anthu amene alipo pokonzekera zimenezi. Muwerengere kuchuluka kwa nyama imene anthu adzadye potengera mmene munthu mmodzi angadyere. 5Ziweto zimene musankhe ziyenera kukhala zazimuna za chaka chimodzi, zopanda chilema, ndipo zikhale nkhosa kapena mbuzi. 6Muzisunge mpaka tsiku la khumi ndi chinayi la mwezi, pamene gulu lonse la Aisraeli lidzaphe nyamazo madzulo. 7Ndipo adzatengeko magazi anyamazo ndi kuwaza pa mphuthu ziwiri za chitseko ndiponso pamwamba pa chitseko cha nyumba mmene adzadyeremo ana ankhosawo. 8Adzawotche nyamayo ndi kudya usiku womwewo, ndipo adzayidye ndi buledi wophikidwa popanda yisiti pamodzi ndi masamba wowawa. 9Musadzadye yayiwisi kapena yophika, koma mudzawotche yonse, mutu, miyendo ndi zamʼmimba. 10Musadzasiye nyama ina mpaka mmawa, ngati ina idzatsala mpaka mmawa, mudzayitenthe. 11Muzidzadya nyamayo mutavala chotere, pokonzekera ulendo: mudzazimangirire lamba mʼchiwuno, nsapato zanu kuphazi ndi ndodo yanu kumanja. Mudzadye mofulumira. Imeneyi ndi Paska ya Yehova.

12“Usiku umenewo Ine ndidzadutsa mʼdziko la Igupto ndipo ndidzapha chilichonse choyamba kubadwa kuyambira mwana wa munthu aliyense mpaka ana aziweto. Ndidzalanganso milungu yonse ya Igupto. Ine ndine Yehova. 13Magazi amene mudzawaze pa mphuthu za zitseko ndi pamwamba pa zitseko aja adzakhala ngati chizindikiro. Ine ndikadzaona magaziwo ndidzakudutsani, ndipo ndikadzamakantha anthu a Igupto, mliri wosakazawu sudzakukhudzani.

14“Ili ndi tsiku la chikumbutso. Tsiku limeneli muzidzachita chikondwerero, kupembedza Yehova. Mibado yonse imene ikubwera izidzakumbukira tsiku limeneli ngati lamulo lamuyaya ndi kuti pa tsikuli azidzachita chikondwerero cholemekeza Yehova. 15Kwa masiku asanu ndi awiri muzidya buledi wopanda yisiti. Tsiku loyamba muzichotsa yisiti mʼnyumba zanu, ngati aliyense adzadya kanthu kalikonse kali ndi yisiti kuyambira tsiku loyamba mpaka tsiku lachisanu ndi chiwiri, munthu ameneyo adzayenera kuchotsedwa mʼgulu la Israeli. 16Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika, ndipo winanso uzikhala pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Musamagwire ntchito masiku onsewa, koma ntchito yokonza chakudya yokha kuti aliyense adye. Izi ndi zimene muzichita.

17“Muzichita chikondwerero cha buledi wopanda yisiti, chifukwa ndi pa tsiku limeneli ndinatulutsa magulu anu mʼdziko la Igupto. Muzikondwerera tsiku limeneli pa mibado yonse ngati lamulo lamuyaya. 18Mwezi woyamba muzidzadya buledi wopanda yisiti kuyambira madzulo tsiku la 14 la mweziwo mpaka tsiku la 21 mwezi womwewo. 19Yisiti asamapezeka mʼnyumba zanu kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo aliyense amene adya chakudya chimene muli yisiti, munthu ameneyo ayenera kuchotsedwa mʼgulu la Aisraeli, kaya iyeyo ndi mlendo kapena mbadwa. 20Musadye chilichonse chokhala ndi yisiti. Kulikonse kumene mukukhala, muyenera kudya buledi wopanda yisiti.”

21Ndipo Mose anasonkhanitsa akuluakulu onse a Israeli nati, “Pitani msanga kukasankha nkhosa zokwanira pa mabanja anu, ndipo muziphe ngati Paska. 22Mutengenso nthambi ya chitsamba cha hisope, muchiviyike mʼmagazi amene mwawayika mʼbeseni ndipo muwaze ena mwa magaziwo pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko. Palibe aliyense wa inu amene adzatuluke mʼnyumba yake mpaka mmawa. 23Pamene Yehova adzadutsa mʼdziko kudzakantha Aigupto, nʼkuona magazi pamwamba ndi mʼmbali mwa mphuthu za chitseko, Iye adzadutsa khomo limenelo ndipo sadzalola woonongayo kuti alowe mʼnyumba zanu kuti akukantheni.

24“Muzimvera malamulo amenewa kwa muyaya, inu ndi zidzukulu zanu. 25Mukakalowa mʼdziko limene Yehova adzakupatseni monga analonjeza, mukasunge mwambo umenewu. 26Ndipo ana anu akakakufunsani kuti, ‘Mwambo umenewu ukutanthauza chiyani?’ 27Inu mukawawuze kuti, ‘Ndi nsembe ya Paska ya Yehova, popeza pamene ankakantha nyumba za Aigupto anasiya nyumba zathu.’ ” Kenaka anthu anawerama napembedza. 28Aisraeli anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni.

29Pakati pa usiku Yehova anakantha ana onse oyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira woyamba kubadwa wa Farao, amene amakhala pa mpando waufumu wa Faraoyo, mpaka mwana woyamba kubadwa wa munthu amene anali mʼdzenje, pamodzinso ndi ana oyamba kubadwa a ziweto zawo. 30Farao ndi nduna zake zonse ndiponso Aigupto onse anadzuka pakati pa usiku, ndipo kunali kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, pakuti panalibe nyumba imene munalibe munthu wakufa.

Kutuluka kwa Aisraeli

31Pakati pa usiku Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Nyamukani! Asiyeni anthu anga, inu ndi Aisraeli! Pitani, kapembedzeni Yehova monga munapempha. 32Tengani ziweto ndi ngʼombe zanu ndipo pitani kapembedzeni Mulungu wanu monga munanenera kuti ine ndidalitsike.”

33Aigupto anawawumiriza anthuwo kuti atuluke mofulumira ndi kusiya dziko lawo. Iwo anati, “Ngati sitiwalola kutero, tonse tidzafa.” 34Motero anthuwo ananyamula ufa wawo wopangira buledi asanathiremo yisiti ndipo anasenza pa mapewa awo pamodzi ndi zokandiramo buledi atazikulunga mu nsalu. 35Aisraeli anachita monga anawawuzira Mose kuti apemphe kwa Aigupto zozikongoletsera zasiliva ndi zagolide ndi zovala. 36Yehova anafewetsa mtima Aigupto kuti akomere mtima Aisraeliwo ndipo anawapatsa zimene anawapempha. Motero Aisraeli anawalanda zinthu Aigupto.

37Aisraeli anayenda ulendo kuchokera ku Ramesesi mpaka kukafika ku Sukoti. Anthu aamuna oyenda pansi analipo 600,000 osawerengera akazi ndi ana. 38Anthu enanso ambiri anapita nawo, kuphatikizanso gulu lalikulu la ziweto, mbuzi, nkhosa pamodzi ndi ngʼombe. 39Iwo anapanga buledi wopanda yisiti ndi ufa umene anachoka nawo ku Igupto. Ufawo unalibe yisiti chifukwa anachita kuthamangitsidwa ku Igupto ndipo analibe nthawi yokonzera chakudya chawo.

40Ndipo Aisraeli anakhala ku Igupto kwa zaka 430. 41Pa tsiku lomwelo limene anakwanitsa zaka 430, magulu onse a Yehova anatuluka mʼdziko la Igupto. 42Usiku wonse Yehova anachezera kutulutsa ana a Israeli mʼdziko la Igupto. Nʼchifukwa chake pa tsiku limeneli Aisraeli onse azichezera usiku wonse kulemekeza Mulungu kamba ka mibado yonse ya mʼtsogolo.

Lamulo la Paska

43Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Malamulo a Paska ndi awa:

“Mlendo asadye Paska. 44Kapolo aliyense amene munagula angadye ngati atayamba wachita mdulidwe. 45Koma amene mukukhala naye kwa kanthawi kapena waganyu asadye Paska.

46“Muzidyera Paska mʼnyumba imodzi. Musatulutse nyama iliyonse kunja kwa nyumba. Musaswe mafupa aliwonse. 47Gulu lonse la Israeli lizichita mwambo wachikondwererochi.

48“Ngati mlendo wokhala pakati panu angafune kuchita nawo mwambo wa chikondwerero cha Paska, cha Yehovachi, amuna onse a mʼnyumba mwake ayenera kuchita mdulidwe. Akatero muzimutenga ngati mbadwa pakati panu. Koma aliyense wosachita mdulidwe asadye Paska. 49Lamulo limeneli likhudza mbadwa ngakhalenso alendo wochita mdulidwe wokhala pakati panu.

50“Aisraeli onse anachita monga momwe Yehova analamulira Mose ndi Aaroni. 51Ndipo tsiku lomwelo Yehova anatulutsa gulu lonse la ana a Israeli mʼdziko la Igupto.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

出埃及記 12:1-51

逾越節

1耶和華在埃及摩西亞倫說: 2「從現在開始,你們要以這個月為一月,為一年之首。 3你要向以色列全體會眾宣佈,本月的第十日,每家都要預備一隻羊羔,一家一隻。 4倘若家人太少,吃不了一隻,可以跟最近的鄰居共享一隻,你們要按人數和各人的食量預備羊羔。 5羊羔必須是毫無殘疾、一歲的公綿羊或公山羊。 6全體會眾要把羊留到本月十四日,在黃昏時分宰殺, 7然後取點血塗在房子的門框和門楣上,全家要在房子裡吃羊肉。 8當晚,你們要用火把羊肉烤熟,與無酵餅和苦菜一起吃。 9不可吃生羊肉,也不可煮著吃,要把整隻羊,連頭帶腿和內臟一併烤著吃。 10不可把肉留到早晨,留到早晨的肉要燒掉。 11你們吃的時候,要束腰、穿鞋、手中拿杖,要趕快吃,這是耶和華的逾越節。

12「因為那一夜我要巡遍埃及,把境內所有長子和頭生的牲畜全都殺掉,也要嚴懲埃及所有的神明。我是耶和華。 13塗在你們房屋上的血是一個記號,我見到這血就會越過你們。我擊打埃及的時候,那災禍不會落到你們身上。 14你們要記住這一天,守為耶和華的節期,作為世世代代永遠的定例。

除酵節

15「七天之內你們都要吃無酵餅。第一天,要清除家中所有的酵。任何人若在這七天當中吃有酵的餅,要將他從以色列人中剷除。 16在節期的第一天和第七天,你們都要招聚百姓舉行聖會。這兩天所有人都不得工作,除了預備各人要吃的以外,不可做任何工。 17你們要守這無酵節,因為我在這天把你們大隊人馬從埃及領了出來。你們要守這節期,作為世世代代永遠的定例。 18從一月十四日晚上開始,直到二十一日晚上,你們都要吃無酵餅。 19在這七天內,你們屋裡不能有酵。任何人若吃了有酵的東西,不論他是寄居者還是本地人,要將他從以色列會眾中剷除。 20無論你們住在哪裡都要吃無酵餅,不能吃有酵的食物。」

21於是,摩西召集以色列的眾長老,對他們說:「你們家家戶戶都要挑選羊羔,把這逾越節的羊羔宰了。 22拿一把牛膝草蘸盆裡的血,把血塗在門框和門楣上。天亮前,你們不可踏出門外。 23因為耶和華要巡行各地,擊殺埃及人,祂看見你們的門框和門楣上有血,就必越過你們的家門,不讓滅命者進你們家殺人。 24這是你們世世代代都要遵守的定例。 25你們進入耶和華應許給你們的地方以後,要守這逾越節。 26你們的兒女問你們守這節期的意義時, 27你們就說,『這是獻給耶和華逾越節的祭,因為我們從前在埃及時,祂擊殺埃及人,卻越過以色列人所住的房子,救了我們各家。』」百姓聽了摩西這番話,都低頭下拜。 28耶和華怎麼吩咐摩西亞倫以色列人就照樣遵行。

29到了半夜,耶和華把所有埃及人的長子都殺了,包括坐王位的法老的長子、牢中囚犯的長子和一切頭生的牲畜。 30晚上,法老及其臣僕和所有埃及人都驚醒了,到處都是哭號聲,因為沒有一家不死人的。 31法老連夜召見摩西亞倫,對他們說:「你們和以色列人走吧,離開我的人民。就照你們的要求,去事奉耶和華吧! 32照你們的要求,把所有的牛羊都帶走吧!也要為我祝福。」 33埃及人催促以色列人趕快離開埃及,因為他們說:「我們都要死了。」 34於是,以色列百姓就把沒有酵的麵團放在揉麵盆裡,用衣服包起來扛在肩上, 35又遵照摩西的吩咐向埃及人索取金器、銀器和衣服。 36耶和華使埃及人恩待以色列人,他們要什麼,埃及人就給什麼。這樣,以色列人奪取了埃及人的財富。

37以色列百姓從埃及蘭塞啟行,前往疏割,婦女孩童不算在內,單是步行的男子就有六十萬, 38同行的還有許多外族人和大群的牛羊。 39他們用從埃及帶出來的麵團烤成無酵餅,麵團沒有酵,因為他們被催促離開埃及,沒有時間準備食物。 40以色列人在埃及共住了四百三十年, 41正好滿了四百三十年的那一天,耶和華帶領以色列大隊人馬離開了埃及42那天晚上是耶和華把祂的子民帶出埃及之夜,因此以後世世代代的以色列人都要在那日守夜,以尊崇耶和華。

43耶和華對摩西亞倫說:「以下是逾越節的條例。

「所有外族人都不可吃逾越節的羊羔, 44但那些買來的奴隸若接受了割禮,就可以吃。 45寄居的外族人和雇用的工人不可吃。 46你們吃的時候,應當在房子裡吃,不得把肉帶到外面去,也不可折斷羊羔的一根骨頭。 47以色列全體會眾都要守這節期。 48跟你們住在一起的外族人如果想為耶和華守逾越節,他全家的男子都必須接受割禮,這樣才可以像以色列人一樣守逾越節,但沒有接受割禮的人絕不可吃逾越節的羊羔。 49本地人和在你們中間寄居的外族人都要遵守這規矩。」

50耶和華怎樣吩咐摩西亞倫以色列百姓都遵命而行。 51就在那一天,耶和華帶領以色列大隊人馬離開了埃及