Eksodo 10 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Eksodo 10:1-29

Mliri wa Dzombe

1Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Pita kwa Farao, pakuti Ine ndawumitsa mtima wake ndi mitima ya nduna zake kuti ndichite zizindikiro zozizwitsa pakati pawo 2kuti inu mudzawuze ana ndi zidzukulu zanu za mmene ndinawakhawulitsira Aigupto ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinachita pakati pawo ndiponso kuti inu mudziwe kuti ine ndine Yehova.”

3Ndipo Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndi kukanena kuti, “Yehova Mulungu wa Ahebri, akuti: ‘Kodi udzakanabe kudzichepetsa pamaso panga mpaka liti? Alole anthu anga apite kuti akandipembedze. 4Ngati ukana kuwalola, ndigwetsa dzombe mʼdziko lako lino mawa. 5Dzombeli lidzakuta nthaka yonse moti sidzaoneka konse. Lidzadya kalikonse kakangʼono kamene sikanawonongedwe ndi matalala aja, kuphatikizapo mitengo yonse imene ikumera mʼminda yanu. 6Dzombeli lidzadzaza nyumba zako ndi za nduna zako ndiponso za Aigupto onse, chinthu chimene ngakhale makolo anu kapena makolo awo sanachionepo kuyambira tsiku limene anakhala mʼdzikoli mpaka lero.’ ” Ndipo Mose ndi Aaroni anatembenuka ndi kumusiya Farao.

7Nduna za Farao zinamufunsa kuti, “Kodi munthu uyu adzativutitsa mpaka liti? Aloleni anthuwa apite, kuti akapembedze Yehova Mulungu wawo. Kodi simukuona kuti dziko la Igupto lawonongeka?”

8Choncho Mose ndi Aaroni anayitanidwanso kwa Farao ndipo anati, “Pitani kapembedzeni Yehova Mulungu wanu. Koma ndani amene adzapite?”

9Mose anayankha kuti, “Ife tidzapita tonse pamodzi; angʼonoangʼono ndi akuluakulu, ana athu aamuna ndi aakazi, ndiponso ziweto zathu ndi ngʼombe chifukwa tikakhala ndi chikondwerero cha kwa Yehova.”

10Farao anati, “Yehova akhale ndi inu ngati ndingakuloleni kupita pamodzi ndi akazi ndi ana anu! Zikuoneka kuti mwakonzeka kuchita choyipa. 11Ndakana! Amuna okha ndiwo apite ndi kukapembedza Yehova pakuti izi ndi zimene mwakhala mukupempha.” Kenaka Mose ndi Aaroni anathamangitsidwa pamaso pa Farao.

12Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Tambalitsa dzanja lako pa dziko la Igupto kuti dzombe lidze pa dziko la Igupto ndi kuwononga chilichonse chimene chikumera mʼminda ndi chilichonse chimene chinatsala pa nthawi ya matalala.”

13Kotero Mose anakweza ndodo yake pa dziko la Igupto, ndipo Yehova anawutsa mphepo ya kummawa imene inawomba pa dziko usana ndi usiku wonse. Mmene kumacha nʼkuti mphepoyo itabweretsa dzombe. 14Dzombelo linafika pa dziko lonse la Igupto ndi kukhala dera lililonse la dzikolo. Dzombe lambiri ngati limenelo silinakhaleponso nʼkale lonse ndipo silidzakhalapo ngakhale mʼtsogolo. 15Dzombelo linaphimba nthaka yonse mpaka kuoneka kuti bii. Linadya zonse zimene zinatsala nthawi ya matalala, zomera za mʼmunda ndi zipatso. Panalibe chobiriwira chilichonse chimene chinatsala pa mtengo kapena pa chomera chilichonse mʼdziko lonse la Igupto.

16Mwamsangamsanga, Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni ndipo anati, “Ine ndachimwira Yehova Mulungu wanu ndiponso inu. 17Tsopano ndikhululukirenso tchimo langa kano konkha ndipo pempherani kwa Yehova Mulungu wanu kuti andichotsere mliri wosakazawu.”

18Mose anachoka kwa Farao nakapemphera kwa Yehova. 19Ndipo Yehova anasintha mphepo ija kuti ikhale ya mphamvu yochokera ku madzulo, ndipo inanyamula dzombe lija nʼkulikankhira mʼNyanja Yofiira. Panalibe dzombe ndi limodzi lomwe limene linatsala mu Igupto. 20Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli apite.

Mliri wa Mdima

21Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Tambasulira dzanja lako kumwamba kuti kukhale mdima umene udzaphimba dziko lonse la Igupto, mdima wandiweyani.” 22Choncho Mose anakweza dzanja lake kumwamba ndipo mdima wandiweyani unaphimba dziko lonse la Igupto kwa masiku atatu. 23Palibe amene anatha kuona mnzake kapena kuchoka pa khomo pake kwa masiku atatu. Koma kumalo kumene kumakhala Aisraeli kunali kowala.

24Kenaka Farao anayitanitsa Mose ndi Aaroni nati, “Pitani kapembedzeni Yehova. Ngakhale akazi ndi ana anu apite pamodzi ndi inu. Koma musatenge ziweto zanu ndi ngʼombe zanu.”

25Koma Mose anati, “Ndiye inu mutipatse nsembe zopsereza zoti tikapereke kwa Yehova Mulungu wathu. 26Koma ayi, ife tipita ndi ziweto zathu. Palibe chiweto chilichonse chimene chitatsale kuno, popeza tikasankha komweko ziweto zokapembedzera Yehova. Sitingadziwe zimene tikagwiritse ntchito popembedza Yehova mpaka titakafika kumeneko.”

27Koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao ndipo sanafune kuwalola kuti apite. 28Farao anati kwa Mose, “Choka pamaso panga! Uwonetsetse kuti usadzaonekerenso pamaso panga! Tsiku limene ndidzakuonenso udzafa.”

29Mose anayankha kuti, “Monga momwe mwaneneramu, Ine sindidzaonekeranso pamaso panu.”

Священное Писание

Исход 10:1-29

Восьмое наказание: саранча

1Вечный сказал Мусе:

– Пойди к фараону. Я сделал его сердце и сердца его приближённых упрямыми, чтобы сотворить среди них знамения, 2чтобы ты мог потом рассказать детям и внукам, как сурово Я поступил с египтянами и как сотворил знамения среди них, и чтобы вы знали, что Я – Вечный.

3Муса и Харун пришли к фараону и сказали ему:

– Так говорит Вечный, Бог евреев: «Когда же, наконец, ты смиришься предо Мной? Отпусти Мой народ поклониться Мне. 4Если ты откажешься, то завтра Я наведу на твою страну саранчу. 5Она покроет землю так, что земли не будет видно. Она сожрёт всё то немногое, что осталось у вас после града, и даже деревья, которые растут у вас в полях. 6Она заполнит твои дворцы, дома твоих приближённых и всех египтян: такого не видели ни твои отцы, ни деды с того дня, как поселились в этой земле, и до сегодняшнего дня».

Муса повернулся и ушёл от фараона. 7Приближённые фараона сказали ему:

– Сколько ещё этот человек будет нас мучить? Отпусти этих людей поклониться Вечному, их Богу. Разве ты всё ещё не видишь, что Египет гибнет?

8Тогда Мусу и Харуна вернули к фараону.

– Пойдите, поклонитесь Вечному, вашему Богу, – сказал он. – Только кто же из вас пойдёт?

9Муса ответил:

– Мы пойдём с детьми и стариками, с сыновьями и дочерьми, с отарами и стадами: ведь у нас праздник Вечному.

10Фараон сказал:

– Если я когда-либо отпущу вас с женщинами и детьми, то Вечный действительно с вами! Но берегитесь, вас ждут большие неприятности10:10 Или: «Ясно, у вас злое намерение».. 11Нет уж! Пусть одни мужчины пойдут поклоняться Вечному, раз вы об этом просите.

И Мусу с Харуном выгнали от фараона.

12Вечный сказал Мусе:

– Протяни руку над египетской землёй, и появится саранча. Она сожрёт всё, что растёт в полях, всё то, что уцелело после града.

13Муса простёр посох над Египтом, и Вечный навёл на землю восточный ветер, который дул весь день и всю ночь. К утру ветер принёс саранчу. 14Она напала на Египет, опустившись на страну в огромном количестве. Такого нашествия саранчи не бывало прежде и не будет впредь. 15Она покрыла всю землю, так что земля почернела. Она сожрала всё, что осталось после града, – всё, что росло в полях, и плоды на деревьях. Ни на дереве, ни на каком другом растении во всём Египте не осталось зелени. 16Фараон спешно позвал Мусу и Харуна и сказал:

– Я согрешил перед Вечным, вашим Богом, и перед вами. 17Простите мой грех всего лишь ещё один раз. Помолитесь Вечному, вашему Богу, чтобы Он избавил меня от этого несчастья.

18Муса ушёл от фараона и помолился Вечному. 19Вечный переменил ветер на очень сильный западный, который подхватил саранчу и унёс в Тростниковое море10:19 Тростниковое море – буквальный перевод с языка оригинала. Среди современных специалистов существуют различные мнения, о каком водоёме здесь идёт речь. Тростниковым морем могли называть как цепи озёр, расположенных на Суэцком перешейке и, вероятно, соединявшихся тогда проливами с Красным морем, так и Суэцкий и Акабский заливы Красного моря (см. карту № 2 и, напр., 3 Цар. 9:26). В Инджиле эти же воды названы Красным морем.. В Египте совсем не осталось саранчи. 20Но Вечный сделал сердце фараона упрямым, и он не отпустил исраильтян.

Девятое наказание: тьма

21Вечный сказал Мусе:

– Подними руку к небу, и на Египет ляжет тьма – осязаемая тьма.

22Муса поднял руку к небу, и непроницаемая тьма покрыла Египет на три дня. 23Люди не могли ни видеть друг друга, ни передвигаться в течение трёх дней. А у исраильтян, там, где они жили, был свет. 24Тогда фараон позвал Мусу и сказал:

– Идите, поклонитесь Вечному. Оставьте здесь лишь ваши отары и стада, а женщины и дети пусть идут с вами.

25Муса ответил:

– Ты должен отпустить с нами скот, чтобы мы принесли жертвы всесожжения и пиршественные жертвы Вечному, нашему Богу! 26Весь наш скот должен пойти с нами, не останется и копыта. И там мы отберём животных для жертвы Вечному, нашему Богу, а пока мы не придём туда, мы не будем знать, каких животных следует принести в жертву Вечному.

27Вечный сделал сердце фараона упрямым, и он не захотел отпускать их. 28Он сказал Мусе:

– Прочь с моих глаз, чтобы я тебя больше не видел! В тот день, когда я тебя снова увижу, ты умрёшь.

29– Верно, – ответил Муса. – Больше ты меня не увидишь.