Deuteronomo 9 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 9:1-29

Osati Chifukwa cha Kulungama kwa Israeli

1Mvera Israeli. Watsala pangʼono kuwoloka Yorodani ndi kukathamangitsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa iweyo, imene mizinda yake ndi ikuluikulu yokhala ndi makoma ofika mpaka kumwamba. 2Anthuwo ndi ataliatali, Aanaki! Ukudziwa za iwo ndipo unamvapo zikunenedwa kuti, “Ndani amene angalimbane ndi Aanaki?” 3Koma khulupirira lero kuti Yehova Mulungu wako amene ali patsogolo pako ali ngati moto wonyeketsa. Adzawononga iwowo ndipo adzawagonjetsa iweyo ukuona. Pamenepo udzawathamangitsa ndi kuwakantha mwamsanga, monga momwe Yehova wakulonjezera.

4Yehova Mulungu wako akadzawapirikitsa pamaso pako, usadzanene mu mtima mwako kuti, “Yehova wandibweretsa kuno kudzalanda dziko lino chifukwa cha kulungama kwanga.” Ayi, koma ndi chifukwa cha kuyipa kwa anthu amene Yehova ati awapirikitse pamaso pako. 5Sukalowa ndi kutenga dziko lawolo chifukwa cha kulungama kwako kapena kukhulupirika kwako koma chifukwa cha kuyipa kwa anthuwo. Yehova Mulungu wako awapirikitsa pamaso pako kuti akwaniritse zimene analumbira kwa makolo ako Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 6Tsono zindikira kuti si chifukwa cha kulungama kwako kuti Yehova Mulungu wako akukupatsa dziko labwinoli kuti ulitenge popeza ndiwe wokanika.

Mwana Wangʼombe Wagolide

7Kumbukirani izi ndipo musayiwale mmene munaputira mkwiyo wa Yehova Mulungu mʼchipululu muja. Kuyambira tsiku limene munatuluka mu Igupto mpaka pamene munafika kuno, mwakhala owukira Yehova. 8Ku Horebu munaputa mkwiyo wa Yehova, kotero kuti anakwiya kwambiri nafuna kukuwonongani. 9Nditakwera ku phiri kuti ndikalandire miyala iwiri ya malamulo, ya pangano limene Yehova anachita ndi inu, ndinakhala ku phiriko kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana, sindinadye buledi kapena kumwa madzi. 10Yehova anandipatsa miyala iwiri yolembedwa ndi chala chake. Pa miyalapo panali malamulo onse amene Yehova analengeza kwa inu pa phiri kuchokera mʼmoto pa tsiku la msonkhano.

11Pakutha pa masiku makumi anayi usiku ndi usana, Yehova anandipatsa miyala iwiri, miyala ya pangano. 12Tsono Yehova anandiwuza, “Tsikako kuno msanga, chifukwa anthu ako aja unawatulutsa ku Iguptowa adziyipitsa. Iwo apatukapo mofulumira pa zimene ndinawalamulira ndipo adzipangira fano lachitsulo.”

13Ndipo Yehova anati kwa ine, “Anthu awa ndawaona ndipo ndi anthu okanikadi! 14Ndilekeni ndiwawononge ndi kufafaniza mayina awo pa dziko lapansi. Ndipo ndidzakuyesa iwe mtundu wa anthu wamphamvu ndi wochuluka kuposa iwo.”

15Choncho ndinatembenuka ndi kutsika phiri moto ukanayakabe. Ndipo miyala iwiri ya pangano inali mʼmanja mwanga. 16Ine poyangʼana ndinaona kuti inu munachimwira Yehova Mulungu wanu. Munadzipangira fano lowumbidwa ngati mwana wangʼombe. Inuyo munapatuka msanga kuchoka pa njira imene Yehova anakulamulirani. 17Motero ine ndinaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwanga, ndi kuyiphwanya inu mukuona.

18Tsono nthawi yomweyo ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usiku ndi usana. Sindinadye buledi kapena kumwa madzi chifukwa cha machimo onse amene munawachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kumukwiyitsa kwambiri. 19Ine ndinachita mantha ndi mkwiyo ndi ukali wa Yehova chifukwa anakwiya nanu kokwanira kukuwonongani. Koma Yehova anandimveranso. 20Ndipo Yehova anakwiya ndi Aaroni ndipo akanamuwononga, koma ine ndinamupemphereranso Aaroniyo. 21Ndiponso ndinatenga chinthu chanu choyipacho, mwana wangʼombe amene munapangayo, ndi kumuwotcha pa moto. Kenaka ndinamuphwanya ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi ndipo ndinawaza fumbilo mu mtsinje umene unkayenda kuchokera mʼphiri.

22Inu munamukwiyitsanso Yehova ku Tabera, ku Masa ndi ku Kibiroti Hatava.

23Ndipo Yehova atakutulutsani ku Kadesi Barinea anati, “Pitani mukatenge dziko limene ndakupatsani.” Koma munawukira ulamuliro wa Yehova Mulungu wanu. Inu simunamukhulupirire kapena kumumvera. 24Kuyambira pamene ndinakudziwani, mwakhala owukira Yehova.

25Ine ndinagwa chafufumimba pamaso pa Yehova kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku chifukwa Yehova ananena kuti akuwonongani. 26Ndinapemphera kwa Ambuye ndi kuti, “Haa Yehova Wamkulukulu, musawawononge anthu anu, chuma chanuchanu chimene munachipulumutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ku Igupto ndi dzanja lanu la mphamvu. 27Kumbukirani atumiki anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Musatengere kupulupudza, kuyipa ndi kuchimwa kwawo anthuwa. 28Kupanda kutero, ndiye kuti anthu a ku dziko lija munatitulutsaku adzati, ‘Yehova anawatulutsa kuti akawaphe mʼchipululu popeza sanathe kukawalowetsa mʼdziko limene anawalonjeza ndipo anadana nawo.’ 29Koma iwowa ndi anthu anu, chuma chanu chimene munachitulutsa ndi mphamvu yanu yayikulu ndi mkono wanu wotambasuka.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 9:1-29

以色列人的悖逆

1以色列人啊,你们要听!今天你们要过约旦河,去赶出那些比你们强大的民族。他们住在城墙高耸入云的大城里, 2是长得高大威猛的亚衲人。你们了解他们,也听人说过,‘谁能抵挡亚衲人呢?’ 3但今天你们要知道,你们的上帝耶和华要走在你们前面,像烈火一样吞噬他们。祂要制服他们,使你们迅速赶走他们,毁灭他们,正如祂对你们的应许。

4“你们的上帝耶和华赶走他们以后,你们不要以为耶和华带领你们占领那片土地是因为你们公义,其实是因为那里的民族邪恶,耶和华才将他们从你们面前赶走。 5你们能占领他们的土地并非因为你们公义、行为正直。你们的上帝耶和华从你们面前赶走那些民族,是因为他们邪恶,也是为了实现祂给你们祖先亚伯拉罕以撒雅各的誓言。 6你们要知道,耶和华赐给你们那佳美之地不是因为你们有好品德。其实你们是顽固不化的人。

7“要牢记你们在旷野怎样触怒你们的上帝耶和华。从你们离开埃及那天到现在,你们屡屡背叛耶和华。 8何烈山,你们触怒了耶和华,以致祂要毁灭你们。 9那时,我上山去接受耶和华与你们立约的石版,在山上待了四十昼夜,不吃也不喝。 10耶和华把两块立约的石版交给我,上面刻着那天你们聚会时祂在山上的火焰中对你们说的话,是祂用手指刻上去的。 11四十昼夜后,耶和华把那两块刻着约的石版交给我, 12对我说,‘快下山吧,你从埃及领出来的百姓已经败坏了。他们这么快就偏离了我吩咐他们走的道,为自己铸造了神像。’

13“耶和华又对我说,‘我已看出,这是顽固不化的百姓。 14不要拦我,我要毁灭他们,从世上抹去他们的名字。我要使你的子孙成为一个比他们更强大的民族。’ 15我双手拿着那两块石版,转身从烈火熊熊的山上下来, 16看见你们为自己铸造了牛犊像,得罪了你们的上帝耶和华,这么快就偏离了耶和华吩咐你们走的道, 17就当着你们的面摔碎了那两块石版。

18“我又俯伏在耶和华面前,四十昼夜不吃不喝,因为你们犯了大罪,做耶和华憎恶的事,惹祂发怒。 19耶和华向你们发烈怒,要毁灭你们,我非常惧怕。但耶和华再次垂听了我的祈求。 20耶和华对亚伦非常愤怒,以致要杀掉他,于是我也为他祈求。 21我焚烧了你们铸造的罪恶之物——牛犊像,把它磨成细粉,撒在从山上流下来的溪水中。

22“你们在他备拉玛撒基博罗·哈他瓦三番四次地触怒耶和华。 23你们的上帝耶和华吩咐你们离开加低斯·巴尼亚,去占领祂赐给你们的土地,你们却背叛祂,不信靠祂,也不听从祂。 24自从我认识你们以来,你们就不断地背叛耶和华。

25“因为耶和华说要毁灭你们,我就俯伏在耶和华面前四十昼夜, 26向祂祈求说,‘主耶和华啊,求你不要毁灭你的子民!他们是你的产业,是你用大能的手从埃及拯救出来的。 27求你看在你仆人亚伯拉罕以撒雅各的份上,不要计较这个民族的顽固和罪恶, 28免得你带领我们离开之地的人说,你不能把他们领到你应许给他们的地方,你憎恶他们,所以把他们带到旷野杀了。 29他们毕竟是你的子民,你的产业,是你伸出大能的臂膀从埃及带出来的。’