Deuteronomo 6 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 6:1-25

Konda Yehova Mulungu Wako

1Awa ndi malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene Yehova Mulungu wanu anandilamula kuti ndikuphunzitseni kuti mukawatsatire mʼdziko limene mukuwolokera Yorodani kuti mukalitenge, 2kuti inuyo, ana anu, ndi zidzukulu zanu mʼtsogolomo mudzaope Yehova Mulungu wanu moyo wanu wonse posunga malangizo ndi malamulo ake onse amene ndinakupatsani inu kuti musangalale ndi moyo wautali. 3Mvera Israeli ndipo usamalitse kuchita malamulowa kuti zinthu zikuyendere bwino mʼdziko ndi kuti muchuluke kwambiri mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.

4Tamvani inu Aisraeli, Yehova Mulungu wathu, Yehova ndi mmodzi. 5Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse. 6Malamulo amene ndakupatsani lero ayenera kukhala mu mtima mwanu. 7Muziwaphunzitsa mwachangu kwa ana anu. Muzikamba za malamulowa pamene muli mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mukugona ndi pamene mukudzuka. 8Muwamange ngati zizindikiro pa manja anu ndi kuwamangirira pa zipumi zanu. 9Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu.

10Pamene Yehova Mulungu wanu akukulowetsani ndi kukupatsani dziko limene analumbirira makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo, dziko lokhala ndi mizinda ikuluikulu imene inu simunamange, 11nyumba zodzaza ndi zinthu za mitundu yonse zimene inu simunayikemo, zitsime zimene inu simunakumbe, minda ya mpesa ndi mitengo ya olivi zimene inuyo simunadzale, tsono mukadya ndi kukhuta, 12samalani kuti mungayiwale Yehova amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani mu ukapolo.

13Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye yekha, ndipo muzilumbira pa dzina lake. 14Musamatsatire milungu ina, milungu ya anthu ena okuzungulirani, 15pakuti Yehova Mulungu wanu amene ali pakati panu, ndi Mulungu wansanje ndipo adzakukwiyirani kwambiri ndi kukuwonongani, kukufafanizani mʼdziko. 16Musamuyese Yehova Mulungu wanu monga munachitira ku Masa. 17Onetsetsani kuti mukusunga malamulo a Yehova Mulungu wanu, malangizo ake ndi zikhazikitso zake zimene anakulamulirani. 18Chitani zoyenera ndi zabwino pamaso pa Yehova, kuti zikuyendereni bwino ndi kuti mukhoza kukalowa ndi kulanda dziko labwinolo limene Yehova analonjeza molumbira kwa makolo anu, 19kupirikitsiratu adani anu onse, monga Yehova wanenera.

20Mʼtsogolo muno, ana anu akadzakufunsani kuti, “Kodi tanthauzo la ndondomeko, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo amene Yehova Mulungu wathu anakulamulani nʼchiyani?” 21Inu mudzawawuze kuti, “Ife tinali akapolo a Farao ku Igupto, koma Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lamphamvu. 22Ifeyo tikuona Yehova anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa, zazikulu ndi zoopsa, pa Aigupto ndi Farao pamodzi ndi banja lake lonse. 23Koma anatitulutsa kumeneko ndi kutilowetsa kuno natipatsa dziko limene analonjeza mwa lumbiro kwa makolo athu. 24Yehova anatilamula kuti tizimvera malamulo onsewa, kuti tizimuopa kuti zinthu zizitiyendera bwino pa moyo wathu monga momwe zilili leromu. 25Ndipo ngati tisamala kumvera malamulo onsewa pamaso pa Yehova Mulungu wathu monga momwe anatilamulira ife, chimenecho chidzakhala chilungamo chathu.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

申命记 6:1-25

最大的诫命

1“你们的上帝耶和华吩咐我教导你们以下的诫命、律例和典章,以便你们在将要占领的土地上遵行。 2这样,你们就会得享长寿,你们及子孙就会终生敬畏你们的上帝耶和华,遵守祂借我吩咐你们的一切律例和诫命。 3以色列人啊,你们要留心听,谨慎遵行,以便你们在那奶蜜之乡可以凡事顺利、子孙众多,正如你们祖先的上帝耶和华给你们的应许。 4听啊,以色列人,耶和华是我们的上帝,耶和华是独一的。 5你们要全心、全意、全力爱你们的上帝耶和华。 6要将我今天吩咐你们的话牢记在心, 7并教导你们的儿女,无论在家在外,或起或卧,都要讲论这些律例和诫命。 8要把它们系在手上、戴在额上作记号, 9要写在城门上和自家的门框上。

10“你们的上帝耶和华将带你们进入祂向你们祖先亚伯拉罕以撒雅各起誓要赐给你们的土地。那里的宏伟城邑不是你们建造的, 11满屋的美物不是你们积攒的,井不是你们挖掘的,葡萄园和橄榄树也不是你们栽种的。你们在那里吃饱喝足之后, 12要小心,不可忘记把你们从受奴役之地——埃及救出来的耶和华。 13要敬畏你们的上帝耶和华,事奉祂,凭祂的名起誓。 14不可随从周围各族的神明, 15免得你们的上帝耶和华向你们发怒,把你们从世上消灭;因为祂住在你们当中,祂痛恨不贞。

16“不可像在玛撒那样试探你们的上帝耶和华。 17要谨遵你们的上帝耶和华吩咐你们的诫命、法度和律例。 18你们要做耶和华视为正与善的事,以便你们可以凡事顺利,得到耶和华起誓赐给你们祖先的佳美之地, 19赶出所有敌人,正如耶和华所言。

20“将来你们的子孙会问,‘我们的上帝耶和华给你们颁布这些法度、律例和典章是什么意思?’ 21你们要告诉他们,‘我们曾在埃及做法老的奴隶,耶和华用大能的手领我们离开埃及22我们亲眼看见耶和华行伟大而可畏的神迹奇事,惩罚埃及和法老全家。 23祂带领我们离开埃及,为要把我们带进祂起誓赐给我们祖先的这片土地。 24我们的上帝耶和华吩咐我们遵守这一切律例、敬畏祂,以便我们可以常常受益,生命无忧,正如今日的情形。 25如果我们按照我们的上帝耶和华的吩咐,在祂面前谨遵这一切诫命,我们便被算为义人。’