Deuteronomo 5 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 5:1-33

Malamulo Khumi

1Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati:

Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata. 2Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu. 3Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero. 4Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja. 5(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:

6“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.

7“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.

8“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko. 9Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane, 10koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.

11“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.

12“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira. 13Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi, 14koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo. 15Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.

16“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.

17“Usaphe.

18“Usachite chigololo.

19“Usabe.

20“Usapereke umboni womunamizira mnzako.

21“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”

22Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.

23Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine. 24Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye. 25Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu. 26Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo? 27Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”

28Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino. 29Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.

30“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo. 31Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”

32Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere. 33Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 5:1-33

十誡

1摩西把所有的以色列人召來,對他們說:「以色列人啊,要留心聽我今天對你們宣講的律例和典章,要學習並謹慎遵行。 2我們的上帝耶和華曾在何烈山與我們立約, 3這約不是與我們祖先立的,乃是與我們今天還活著的人立的。 4耶和華在山上的烈火中面對面跟你們說話。 5那時,因為你們害怕那烈火,沒有到山上去,我就站在耶和華和你們中間,把耶和華的話傳給你們。耶和華說,

6「『我是你的上帝耶和華,曾把你領出埃及,使你不再受奴役。

7「『除我以外,你不可有別的神。

8「『不可為自己雕刻神像,不可仿照任何飛禽走獸或水族的樣子造神像, 9不可跪拜它們,也不可供奉它們,因為我——你的上帝耶和華痛恨不貞,我必追討背棄我之人的罪,從父到子直到三四代。 10但那些愛我、遵守我誡命的人,我必以慈愛待他們,直到千代。

11「『不可妄用你上帝耶和華的名,違者必被耶和華定罪。

12「『要遵照你的上帝耶和華的吩咐守安息日為聖日。 13你一週可工作六天, 14但第七天是你的上帝耶和華的安息日,你和兒女、僕婢、牛驢等牲畜以及你那裡的外族人在這一天不可做任何工,好讓僕婢和你一樣得到休息。 15要記住,你曾在埃及做奴隸,你的上帝耶和華伸出臂膀,用大能的手把你從那裡領出來。因此,你的上帝耶和華吩咐你守安息日。

16「『要遵照你的上帝耶和華的吩咐孝敬父母,以便在你的上帝耶和華要賜給你的土地上享長壽,蒙祝福。

17「『不可殺人。

18「『不可通姦。

19「『不可偷盜。

20「『不可作偽證陷害人。

21「『不可貪戀別人的妻子,不可貪圖別人的房屋、田地、僕婢、牛驢或其他任何物品。』

22「這是耶和華在山上的烈火、烏雲和幽暗中高聲頒佈給你們全體會眾的誡命。此外,祂沒有說別的。祂把這些話寫在兩塊石版上交給我。 23當時,山上燃燒著烈焰,你們聽見聲音從黑暗中傳來。你們各支派的首領和長老都到我跟前, 24說,『看啊,我們的上帝耶和華向我們彰顯了祂的榮耀和威嚴,我們聽見了祂從火中發出的聲音。今天我們已經看見,人聽見上帝說話後還能活著。 25但我們何必冒死,被這烈火吞噬呢?我們若再次聽到我們的上帝耶和華的聲音,必然喪命。 26世上有誰像我們一樣聽見永活上帝從火中說話後還能活著呢? 27你去聽聽我們上帝耶和華所說的話,然後回來告訴我們,我們必聽從、遵行。』

28「耶和華聽見了你們的話,就對我說,『我聽見了眾人對你說的話,他們所說的都對。 29但願他們常常敬畏我,遵從我的一切誡命,以便他們和他們的子孫世世代代可以蒙福。 30你吩咐他們回到自己的帳篷, 31然後你再回到我這裡來,我要把所有的誡命、律例和典章都賜給你,你要把這些傳授給眾人,使他們可以在我要賜給他們的土地上遵行。』 32所以,你們要謹遵你們上帝耶和華的吩咐,不可偏離左右。 33這樣,你們便得享長壽,並且可以在你們將要佔領的土地上興盛。