Deuteronomo 5 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 5:1-33

Malamulo Khumi

1Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati:

Tamverani inu Aisraeli, malangizo ndi malamulo amene ndikuwuzeni lero. Muwaphunzire ndi kuonetsetsa kuti mukuwatsata. 2Yehova Mulungu wathu anachita pangano ndi ife ku Horebu. 3Yehova sanachite pangano ndi makolo athu koma ndi ife, tonse amene tili moyo lero. 4Yehova anayankhula nanu maso ndi maso kuchokera mʼmoto pa phiri paja. 5(Pa nthawi imeneyo ine ndinayimirira pakati pa Yehova ndi inu kuti ndikuwuzeni mawu a Yehova, chifukwa inu munkachita mantha ndi moto ndipo simunakwere ku phiri). Ndipo Iye anati:

6“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.

7“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.

8“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko. 9Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane, 10koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda ndi kusunga malamulo anga.

11“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.

12“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika monga momwe Yehova Mulungu wako anakulamulira. 13Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi, 14koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi kapena wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu kapena ngʼombe yanu kapena bulu wanu kapena ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu, motero ndiye kuti wantchito wanu wamwamuna ndi wantchito wanu wamkazi adzapumula monga inuyo. 15Kumbukira kuti unali kapolo ku Igupto ndipo Yehova Mulungu wako anakutulutsa kumeneko ndi dzanja lamphamvu ndi lotambasuka. Choncho Yehova Mulungu wako akukulamula kuti uzisunga tsiku la Sabata.

16“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako monga Yehova Mulungu wako wakulamulira iwe kuti ukhale ndi moyo wautali ndi kuti zikuyendere bwino mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.

17“Usaphe.

18“Usachite chigololo.

19“Usabe.

20“Usapereke umboni womunamizira mnzako.

21“Usasirire mkazi wa mnzako. Usasirire nyumba ya mnzako kapena munda wake, wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”

22Awa ndi malamulo amene Yehova anayankhula ndi mawu okweza kwa gulu lanu lonse pa phiri paja mʼmoto, mtambo ndi mdima woopsa, sanawonjezerepo kanthu. Ndipo anawalemba pa mapale awiri amiyala ndi kundipatsa.

23Mutamva mawu kuchokera mu mdimawo, phiri lili moto lawilawi, atsogoleri onse a mafuko anu ndi akuluakulu anu anabwera kwa ine. 24Ndipo munati, “Yehova Mulungu wathu wationetsa ulemerero ndi ukulu wake, ndipo tamva mawu ake kuchokera mʼmoto. Lero taona kuti munthu akhoza kukhala ndi moyo ngakhale Mulungu atayankhula naye. 25Koma tsopano tife chifukwa chiyani? Moto waukuluwu utinyeketsa, ndipo tifa tikapitirirabe kumva mawu a Yehova Mulungu wathu. 26Pakuti ndi munthu uti wolengedwa amene anamvapo mawu a Mulungu wamoyo akuyankhula kuchokera mʼmoto, monga tachitiramu, nakhala ndi moyo? 27Pita pafupi kuti ukamvetsere zonse zimene Yehova Mulungu wathu akunena. Kenaka udzatiwuze chilichonse chimene Yehova Mulungu wathu akunena ndipo tidzamvera ndi kuchita.”

28Yehova anakumvani pamene munkayankhula kwa ine ndipo Yehova anati kwa ine, “Ndamva zimene anthuwa anena kwa iwe. Chilichonse chimene anena ndi chabwino. 29Zikanakhala bwino akanakhala ndi mtima wondiopa ndi kusunga malamulo anga nthawi zonse kuti zinthu ziziwayendera bwino, iwowo pamodzi ndi ana awo kwamuyaya.

30“Pita uwawuze kuti abwerere ku matenti awo. 31Koma iwe ukhale kuno ndi ine kuti ndikupatse malamulo, malangizo ndi ziphunzitso zimene azitsatira mʼdziko limene ndiwapatse kuti alitenge.”

32Choncho samalirani kuchita zimene Yehova Mulungu wanu akukulamulirani inu, musapatukire kudzanja lamanja kapena lamanzere. 33Muyende mʼnjira yonse imene Yehova Mulungu wanu wakulamulirani kuti mukhale ndi moyo ndi kupambana, ndi kuti masiku anu achuluke mʼdziko limene mudzatengelo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 5:1-33

Десять повелений

(Исх. 20:1-17)

1Мусо созвал весь народ Исроила и сказал:

– Слушай, Исроил, установления и законы, которые я объявляю тебе сегодня. Выучи их и храни, чтобы следовать им. 2Вечный, наш Бог, заключил с нами священное соглашение у горы Синай. 3Не только с нашими родителями Вечный заключил это соглашение, но с нами, со всеми, кто здесь сегодня жив. 4Вечный говорил с вами лицом к лицу из огня на горе. 5(В то время я стоял между Вечным и вами, чтобы объявлять вам слово Вечного, потому что вы боялись огня и не поднимались на гору.) Он сказал:

6«Я Вечный, твой Бог, Который вывел тебя из Египта, земли рабства.

7Пусть не будет у тебя других богов, кроме Меня.

8Не делай себе идола – никакого изображения того, что на небе вверху, или на земле внизу, или в водах ниже земли. 9Не поклоняйся им и не служи им, ведь Я, Вечный, твой Бог, – ревнивый Бог, наказывающий детей за грехи отцов до третьего и четвёртого поколения тех, кто ненавидит Меня. 10Но Я дарую любовь тысячам поколений тех, кто5:10 Или: «тысячам тех, кто…» любит Меня и соблюдает Мои повеления.

11Не произноси имени Вечного, твоего Бога, напрасно, потому что Вечный не оставит безнаказанным никого, кто произносит Его имя напрасно.

12Соблюдай субботний день, храни его святым, как повелел тебе Вечный, твой Бог. 13Шесть дней трудись и делай всю свою работу, 14но седьмой день – это суббота, она принадлежит Вечному, твоему Богу. Не делай в этот день никакой работы ни ты, ни твой сын или дочь, ни слуга или служанка, ни вол, ни осёл, ни какой другой скот, ни чужеземец в твоих городах, чтобы твои слуга и служанка могли отдохнуть, как и ты сам. 15Помни, что ты был рабом в Египте и что Вечный, твой Бог, вывел тебя оттуда могучей и простёртой рукой. Поэтому Вечный, твой Бог, повелел тебе соблюдать субботний день.

16Почитай отца и мать, как повелел тебе Вечный, твой Бог, чтобы тебе жить долго и благополучно на земле, которую даёт тебе Вечный, твой Бог.

17Не убивай.

18Не нарушай супружескую верность.

19Не кради.

20Не лжесвидетельствуй.

21Не желай жены ближнего. Не желай дома или земли ближнего, его слуги или служанки, его вола или осла: ничего из того, что принадлежит ближнему твоему».

Ответ народа

(Исх. 20:18-21)

22Это повеления, которые Вечный объявил громким голосом всему народу там, на горе, из огня, облака и кромешной тьмы. Больше Он ничего не добавил. Потом Он написал эти повеления на двух каменных плитках и дал их мне.

23Когда вы слышали голос из тьмы, а гора пылала огнём, все вожди ваших родов и ваши старейшины пришли ко мне 24и сказали: «Вечный, наш Бог, показал нам Свою славу и величие, и мы слышали Его голос из огня. Сегодня мы увидели, что человек может жить, даже если Всевышний говорит с ним. 25Но зачем нам рисковать жизнью ещё раз? Этот великий огонь пожрёт нас, и мы погибнем, если и дальше будем слышать голос Вечного, нашего Бога. 26Ведь кто из смертных когда-либо слышал, как мы, голос живого Бога, говорящего из огня, и остался жив? 27Иди и выслушай, что говорит Вечный, наш Бог. Потом перескажи нам всё, что Вечный, наш Бог, тебе скажет. Мы выслушаем и исполним».

28Вечный услышал вас, когда вы говорили со мной, и сказал мне: «Я услышал всё, что говорили тебе эти люди. Всё, что они сказали, хорошо. 29О если бы их сердце побуждало их всегда жить в страхе предо Мной и соблюдать все Мои повеления, то с ними и с их детьми всё было бы благополучно!

30Иди, скажи им, чтобы они вернулись к своим шатрам. 31Но сам останься здесь со Мной, чтобы Я дал тебе все повеления, установления и законы. Ты должен научить их следовать им в земле, которую Я отдаю им во владение».

32Смотрите же, исполняйте то, что повелел вам Вечный, ваш Бог; не уклоняйтесь ни вправо, ни влево. 33Всегда идите тем путём, которым повелел вам идти Вечный, ваш Бог, чтобы жить и преуспевать и умножить свои дни в земле, которой вы завладеете.