Deuteronomo 33 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 33:1-29

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

1Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai

ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;

anawala kuchokera pa Phiri la Parani.

Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo

kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.

3Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;

opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.

Onse amagwada pansi pa mapazi anu

kuchokera kwa inu amalandira malangizo,

4malamulo amene Mose anatipatsa,

chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.

5Iye anali mfumu ya Yesuruni

pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

pamodzi ndi mafuko a Israeli.

6“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,

anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

7Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;

mubweretseni kwa anthu ake.

Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.

Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

8Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za

mtumiki wanu wokhulupirika.

Munamuyesa ku Masa;

munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.

9Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,

‘Sindilabadira za iwo.’

Sanasamale za abale ake

kapena ana ake,

koma anayangʼanira mawu anu

ndipo anateteza pangano lanu.

10Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu

ndi malamulo anu kwa Israeli.

Amafukiza lubani pamaso panu

ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.

11Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse

ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.

Menyani adani awo mʼchiwuno

kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,

pakuti amamuteteza tsiku lonse,

ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake

ndi mame ambiri ochokera kumwamba

ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;

14ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa

ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;

15ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa

ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;

16ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo

ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.

Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,

wapaderadera pakati pa abale ake.

17Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;

nyanga zake zili ngati za njati.

Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,

ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;

nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,

ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.

19Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,

kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;

kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,

chuma chobisika mu mchenga.”

20Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!

Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,

kukhadzula mkono kapena mutu.

21Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;

gawo la mtsogoleri anasungira iye.

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

anachita chifuniro cha Yehova molungama,

ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,

amene akutuluka ku Basani.”

23Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova

ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;

cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;

abale ake amukomere mtima,

ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.

25Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,

ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26“Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,

amene amakwera pa thambo kukuthandizani

ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.

27Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,

ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.

Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,

adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’

28Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;

zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere

mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,

kumene thambo limagwetsa mame.

29Iwe Israeli, ndiwe wodala!

Wofanana nanu ndani

anthu opulumutsidwa ndi Yehova?

Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu

ndi lupanga lanu la ulemerero.

Adani ako adzakugonjera,

ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

New Russian Translation

Второзаконие 33:1-29

Моисей благословляет роды Израиля

1Вот благословение, которое Моисей, Божий человек, дал израильтянам перед смертью.

2Он сказал:

– Господь пришел от Синая,

взошел над Своим народом от Сеира;

воссиял от горы Паран33:2 Синай, Сеир и Паран – места, которые ассоциируются с заключением завета израильского народа с Богом и получением Закона (см. Исх. 19:18; Суд. 5:4-5; Авв. 3:3)..

Он шел с мириадами33:2 Или: «от мириад». святых

с юга, со склонов Своей горы33:2 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..

3Истинно Он любит Свой народ33:3 Свой народ – букв.: «народы».:

все Его святые в Его руке.

Все они припадают к Твоим стопам

и получают от Тебя наставление,

4Закон, который дал нам Моисей,

наследие народа Иакова.

5Он был царем над Ешуруном,

когда собирались вожди народа

вместе с родами Израиля.

6– Пусть живет Рувим и не умирает,

пусть не будут33:6 Или: «но пусть будут». малочисленны его потомки.

7А это он сказал об Иуде:

– Услышь, Господи, крик Иуды;

приведи его к его народу.

Своими руками пусть он защитит себя.

Будь ему подмогой против врагов!

8О Левии он сказал:

– Твои Туммим и Урим33:8 Туммим и Урим – по-видимому, средства для определения Божьей воли, способ использования которых нам неизвестен. принадлежат

благочестивому Твоему.

Ты испытал его в Массе;

спорил с ним у вод Меривы33:8 Масса и Мерива – см. Исх. 17:1-7 и Чис. 20:1-13..

9Он говорит об отце и матери:

«Мне нет дела до них».

Не признает своих братьев,

не знает своих детей,

потому что они соблюдают Твое слово

и хранят Твой завет.

10Они учат Твоим наставлениям Иакова

и Твоему Закону Израиль.

Они кладут перед Тобой благовония

и цельные всесожжения на Твой жертвенник.

11Благослови, Господи, его силу

и благоволи к делу его рук.

Порази чресла восстающих на него,

порази ненавидящих его,

чтобы они не смогли больше встать.

12О Вениамине он сказал:

– Пусть возлюбленный Господом

безопасно покоится при Нем,

ведь Он защищает его весь день.

Тот, кого любит Господь,

покоится между Его плечами.

13Об Иосифе он сказал:

– Пусть благословит Господь его землю

драгоценной росой с небес наверху

и ручьями, бегущими из земли;

14лучшим, что дает солнце,

лучшим, что порождает луна;

15отборнейшими дарами древних гор

и плодородием вечных холмов;

16лучшими дарами земли и ее полнотой,

милостью Того, Кто пребывал в горящем кусте33:16 См. Исх. 3:2..

Пусть все это сойдет на голову Иосифа,

на темя вождя между братьями33:16 Или: «темя отделенного от своих братьев»..

17Величием он подобен первородному быку,

его сила – сила дикого быка.

Рогами он станет бодать народы,

даже те, что на краях земли.

Таковы десятки тысяч Ефрема,

таковы тысячи Манассии.

18О Завулоне он сказал:

– Радуйся, Завулон, когда выходишь,

и ты, Иссахар, в своих шатрах.

19Они призовут народы к горе

и принесут там жертвы праведности.

Они будут наслаждаться изобилием морей,

сокровищами, скрытыми в песке.

20О Гаде он сказал:

– Благословен, расширяющий владения Гада!

Гад живет там, подобно льву,

терзая и мышцу, и голову.

21Он выбрал себе лучшую землю,

ему отведена доля вождя.

Когда собрались главы народа,

он исполнил праведную волю Господа

и Его правосудие Израилю.

22О Дане он сказал:

– Дан – львенок

прыгающий с Башана.

23О Неффалиме он сказал:

– Неффалим насыщен благоволением Господа

и исполнен Его благословением.

Он унаследует озеро и землю на юге.

24Об Асире он сказал:

– Асир – благословеннейший из сыновей;

пусть будет он в милости у братьев,

пусть омывает он ноги маслом.

25Засовы твоих ворот будут из железа и бронзы,

твое богатство будет неисчислимым, как твои дни.

26Нет подобного Богу Ешуруна,

Который мчится по небесам к тебе на помощь,

на облаках в Своем величии.

27Вечный Бог – твое прибежище,

руки вечные носят тебя.

Он прогонит врага от тебя,

и скажет: «Истреби его!»

28И будет Израиль жить безопасно один;

источник Иакова будет защищен

в земле пшеницы и молодого вина,

где небеса источают росу.

29Блажен ты, Израиль!

Кто подобен тебе,

народу, спасенному Господом?

Он тебе щит и помощник

и славный твой меч.

Враги твои будут пресмыкаться пред тобой,

а ты будешь попирать их высоты33:29 Или: «тела»..