Deuteronomo 33 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 33:1-29

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

1Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai

ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;

anawala kuchokera pa Phiri la Parani.

Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo

kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.

3Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;

opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.

Onse amagwada pansi pa mapazi anu

kuchokera kwa inu amalandira malangizo,

4malamulo amene Mose anatipatsa,

chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.

5Iye anali mfumu ya Yesuruni

pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

pamodzi ndi mafuko a Israeli.

6“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,

anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

7Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;

mubweretseni kwa anthu ake.

Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.

Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

8Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za

mtumiki wanu wokhulupirika.

Munamuyesa ku Masa;

munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.

9Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,

‘Sindilabadira za iwo.’

Sanasamale za abale ake

kapena ana ake,

koma anayangʼanira mawu anu

ndipo anateteza pangano lanu.

10Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu

ndi malamulo anu kwa Israeli.

Amafukiza lubani pamaso panu

ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.

11Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse

ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.

Menyani adani awo mʼchiwuno

kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,

pakuti amamuteteza tsiku lonse,

ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake

ndi mame ambiri ochokera kumwamba

ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;

14ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa

ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;

15ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa

ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;

16ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo

ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.

Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,

wapaderadera pakati pa abale ake.

17Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;

nyanga zake zili ngati za njati.

Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,

ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;

nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,

ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.

19Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,

kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;

kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,

chuma chobisika mu mchenga.”

20Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!

Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,

kukhadzula mkono kapena mutu.

21Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;

gawo la mtsogoleri anasungira iye.

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

anachita chifuniro cha Yehova molungama,

ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,

amene akutuluka ku Basani.”

23Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova

ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;

cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;

abale ake amukomere mtima,

ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.

25Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,

ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26“Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,

amene amakwera pa thambo kukuthandizani

ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.

27Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,

ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.

Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,

adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’

28Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;

zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere

mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,

kumene thambo limagwetsa mame.

29Iwe Israeli, ndiwe wodala!

Wofanana nanu ndani

anthu opulumutsidwa ndi Yehova?

Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu

ndi lupanga lanu la ulemerero.

Adani ako adzakugonjera,

ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

New International Reader’s Version

Deuteronomy 33:1-29

Moses Blesses the Tribes

1Here is the blessing that Moses, the man of God, gave to the Israelites before he died. 2He said,

“The Lord came from Mount Sinai.

Like the rising sun, he shone on his people from Mount Seir.

He shone on them from Mount Paran.

He came with large numbers of angels.

He came from his mountain slopes in the south.

3Lord, I’m sure you love your people.

All the holy ones are in your hands.

At your feet all of them bow down.

And you teach them.

4They learn the law Moses gave us.

It belongs to the community of the people of Jacob.

5The Lord was king over Israel

when the leaders of the people came together.

The tribes of Israel were also there.”

6Here’s what Moses said about Reuben.

“Let Reuben live. Don’t let him die.

And do not let his people be few.”

7Here’s what Moses said about Judah.

Lord, listen to Judah cry out.

Bring him to his people.

By his own power he stands up for himself.

Lord, help him fight against his enemies!”

8Here’s what Moses said about Levi.

“Your Thummim and Urim belong to your faithful servant.

You tested him at Massah.

You argued with him at the waters of Meribah.

9Levi didn’t show special favor to anyone.

He did not spare his father and mother.

He didn’t excuse his relatives or his children.

But he watched over your word.

He guarded your covenant.

10He teaches your rules to the people of Jacob.

He teaches your law to Israel.

He offers incense to you.

He sacrifices whole burnt offerings on your altar.

11Lord, bless all his skills.

Be pleased with everything he does.

Destroy those who rise up against him.

Strike down his enemies until they can’t get up.”

12Here’s what Moses said about Benjamin.

“Let the one the Lord loves rest safely in him.

The Lord guards him all day long.

The one the Lord loves rests in his arms.”

13Here’s what Moses said about Joseph.

“May the Lord bless Joseph’s land.

May he bless it with dew from the highest heavens.

May he bless it with water from the deepest oceans.

14May he bless it with the best crops the sun can produce.

May he bless it with the finest crops the moon can give.

15May he bless it with the best products of the age-old mountains.

May he bless it with the many crops of the ancient hills.

16May he bless it with the best gifts that fill the earth.

May he bless it with the favor of the God who spoke out of the burning bush.

Let all these blessings rest on the head of Joseph.

Let them rest on the head of the one who is prince among his brothers.

17His glory is like the glory of a bull born first to its mother.

His horns are like the horns of a wild ox.

He will use them to destroy the nations.

He’ll wipe out the nations that are very far away.

The ten thousands of men in Ephraim’s army are like the bull and the ox.

So are the thousands in the army of Manasseh.”

18Here’s what Moses said about Zebulun and Issachar.

“Zebulun, be filled with joy when you go out.

Issachar, be joyful in your tents.

19You will call for other people to go to the mountain.

There you will offer the sacrifices of those who do what is right.

You will enjoy the many good things your ships bring you.

You will enjoy treasures that are hidden in the sand.”

20Here’s what Moses said about Gad.

“May the God who gives Gad more land be praised!

Gad lives there like a lion

that tears off arms and heads.

21He chose the best land for his livestock.

The leader’s share was kept for him.

The leaders of the people came together.

Then Gad carried out the Lord’s holy plan.

He carried out the Lord’s decisions for Israel.”

22Here’s what Moses said about Dan.

“Dan is like a lion’s cub

that charges out of the land of Bashan.”

23Here’s what Moses said about Naphtali.

“The Lord greatly favors Naphtali.

The Lord fills him with his blessing.

Naphtali’s land will reach south to the Sea of Galilee.”

24Here’s what Moses said about Asher.

“Asher is the most blessed of sons.

Let his brothers be kind to him.

Let Asher wash his feet with olive oil.

25The bars of his gates will be made out of iron and bronze.

His strength will last as long as he lives.

26“There is no one like the God of Israel.

He rides across the heavens to help you.

He rides on the clouds in his glory.

27God lives forever! You can run to him for safety.

His powerful arms are always there to carry you.

He will drive out your enemies to make room for you.

He’ll say to you, ‘Destroy them!’

28So Israel will live in safety.

Jacob will live secure

in a land that has grain and fresh wine.

There the heavens drop their dew.

29Israel, how blessed you are!

Who is like you?

The Lord has saved you.

He keeps you safe. He helps you.

He’s like a glorious sword to you.

Your enemies will bow down to you in fear.

You will walk on the highest places of their lands.”