Deuteronomo 33 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 33:1-29

Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli

1Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2Iye anati:

“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai

ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;

anawala kuchokera pa Phiri la Parani.

Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo

kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.

3Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;

opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.

Onse amagwada pansi pa mapazi anu

kuchokera kwa inu amalandira malangizo,

4malamulo amene Mose anatipatsa,

chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.

5Iye anali mfumu ya Yesuruni

pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

pamodzi ndi mafuko a Israeli.

6“Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,

anthu ake asachepe pa chiwerengero.”

7Ndipo ponena za Yuda anati:

“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;

mubweretseni kwa anthu ake.

Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.

Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”

8Za fuko la Alevi anati:

“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za

mtumiki wanu wokhulupirika.

Munamuyesa ku Masa;

munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.

9Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,

‘Sindilabadira za iwo.’

Sanasamale za abale ake

kapena ana ake,

koma anayangʼanira mawu anu

ndipo anateteza pangano lanu.

10Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu

ndi malamulo anu kwa Israeli.

Amafukiza lubani pamaso panu

ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.

11Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse

ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.

Menyani adani awo mʼchiwuno

kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”

12Za fuko la Benjamini anati:

“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,

pakuti amamuteteza tsiku lonse,

ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”

13Za fuko la Yosefe anati:

“Yehova adalitse dziko lake

ndi mame ambiri ochokera kumwamba

ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;

14ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa

ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;

15ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa

ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;

16ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo

ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.

Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,

wapaderadera pakati pa abale ake.

17Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;

nyanga zake zili ngati za njati.

Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,

ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.

Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;

nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”

18Za fuko la Zebuloni anati:

“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,

ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.

19Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,

kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;

kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,

chuma chobisika mu mchenga.”

20Za fuko la Gadi anati:

“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!

Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,

kukhadzula mkono kapena mutu.

21Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;

gawo la mtsogoleri anasungira iye.

Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,

anachita chifuniro cha Yehova molungama,

ndiponso malamulo onena za Israeli.”

22Za fuko la Dani anati:

“Dani ndi mwana wamkango,

amene akutuluka ku Basani.”

23Za fuko la Nafutali anati:

“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova

ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;

cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”

24Za fuko la Aseri anati:

“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;

abale ake amukomere mtima,

ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.

25Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,

ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.

26“Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,

amene amakwera pa thambo kukuthandizani

ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.

27Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,

ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.

Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,

adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’

28Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;

zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere

mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,

kumene thambo limagwetsa mame.

29Iwe Israeli, ndiwe wodala!

Wofanana nanu ndani

anthu opulumutsidwa ndi Yehova?

Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu

ndi lupanga lanu la ulemerero.

Adani ako adzakugonjera,

ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”

Hoffnung für Alle

5. Mose 33:1-29

Mose segnet die Stämme Israels

1Vor seinem Tod segnete Mose, der Mann Gottes, die Israeliten mit diesen Worten:

2»Der Herr kam vom Berg Sinai, wie die Sonne erhob er sich über dem Gebirge Seïr. Über den Bergen von Paran zeigte er sich ihnen in seinem Glanz. Unzählige Engel begleiteten ihn, und Feuer fuhr aus seiner rechten Hand.33,2 Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten.

3Der Herr liebt die Stämme Israels, schützend hält er alle Menschen in seiner Hand, die zu ihm gehören. Sie werfen sich vor ihm nieder und achten auf seine Worte.

4Ich habe euch, den Nachkommen von Jakob, das Gesetz gegeben, es ist unser reiches Erbe.

5Die führenden Männer und alle Stämme Israels versammelten sich, und der Herr wurde König seines geliebten Volkes33,5 Wörtlich: Jeschurun. – So auch in Vers 26. Vgl. die Anmerkung zu Kapitel 32,15.

6Zuerst segnete Mose den Stamm Ruben:

»Ruben soll leben und nie untergehen, aber auch nicht zu groß werden33,6 Oder: und seine Anzahl soll groß werden.

7Dann segnete er den Stamm Juda:

»Herr, erhöre die Leute von Juda, wenn sie zu dir beten! Denn sie kämpfen für Israel. Hilf ihnen gegen ihre Feinde, und bring sie aus jedem Kampf sicher nach Hause zurück.«

8Über den Stamm Levi sagte Mose:

»Sie haben die heiligen Lose33,8 Wörtlich: Urim und Tummim. – Mit diesen beiden Gegenständen erfragte der Priester den Willen Gottes., weil sie dir, Herr, treu geblieben sind. Du hast sie in Massa herausgefordert und in Meriba auf die Probe gestellt.

9Sie haben dein Wort bewahrt und befolgt. Am Bund mit dir haben sie treu festgehalten, um deinetwillen stellten sie sich gegen ihre Eltern, Geschwister und Kinder.33,9 Zu den Versen 8‒9 vgl. 2. Mose 17,1‒7; 32,25‒29.

10Sie sollen den Israeliten immer wieder deine Gebote nahebringen, dein Gesetz den Nachkommen von Jakob weitergeben. Sie bringen dir Opfer dar auf dem Altar und verbrennen Weihrauch zu deiner Ehre.

11Herr, segne die Leviten, stärke sie! Freu dich über alles, was sie tun! Wer sie hasst und angreift, den zerschmettere, dass er nie wieder aufstehen kann.«

12Dann segnete Mose den Stamm Benjamin:

»Der Herr liebt die Benjaminiter besonders! Sie sollen immer in Frieden und Sicherheit leben. Der Herr wohnt bei ihnen und beschützt sie Tag und Nacht. An Gottes Brust sind sie geborgen.33,12 Wörtlich: Zwischen seinen Schultern wohnt er. – Möglicherweise bezieht sich die Aussage auch auf Gott und spielt auf das spätere Jerusalemer Heiligtum zwischen den Schultern, d.h. den Berghängen, im Stammesgebiet von Benjamin an.«

13Zum Stamm Josef sagte Mose:

»Der Herr segne euer Land mit kostbarem Regen vom Himmel und mit Quellwasser aus der Tiefe.

14Er segne euch mit den reichen Gaben, die Monat für Monat im Sonnenlicht wachsen.

15Er segne euch mit den herrlichsten Wäldern oben auf den uralten Bergen und Höhen.

16Er beschenke euch mit all den Schätzen und dem ganzen Reichtum, den die Erde hervorbringt. Ich bitte den Gott, der mir im Dornbusch erschien, dass er sich über euch freut und euch seine Liebe zeigt. Denn ihr vom Stamm Josef nehmt einen besonderen Platz unter den Israeliten ein.

17Stark seid ihr wie ein Stier, gefährlich wie ein wilder Büffel, der mit den Hörnern um sich stößt. Ihr Tausende aus Manasse und Zehntausende aus Ephraim, ihr besiegt alle Völker auf der ganzen Welt.«

18Zu den Stämmen Sebulon und Issachar sagte Mose:

»Ihr vom Stamm Sebulon, freut euch an euren Fahrten auf dem Meer! Und ihr vom Stamm Issachar, freut euch am Leben in euren Zelten!

19Ihr ladet Völker ein zum heiligen Berg und bringt dort mit aufrichtigem Herzen Opfer dar. Auf See werdet ihr reichen Handel treiben und am Strand verborgene Schätze heben.«

20Dann segnete Mose den Stamm Gad:

»Ich lobe Gott dafür, dass er euch ein weites Land schenkt. Wie eine Löwin lauert euer Stamm auf Beute. Und hat er sie gepackt, dann reißt er ihr den Kopf und den Arm ab.

21Ihr habt euch an die Spitze Israels gestellt und euer Volk so in den Kampf geführt. Die Befehle des Herrn habt ihr befolgt und zusammen mit den anderen Israeliten sein Gericht vollstreckt. Weil ihr die Anführer im Kampf wart, habt ihr auch das Gebiet bekommen, das zuerst erobert wurde. So habt ihr es euch selbst gewünscht.«

22Über den Stamm Dan sagte Mose:

»Dan ist wie ein junger Löwe, der aus dem Dickicht von Baschan hervorspringt.«

23Zum Stamm Naftali sagte er:

»Ihr von Naftali erfahrt die ganze Liebe des Herrn und werdet reich von ihm beschenkt. Euch gehört das Land, das sich vom See nach Süden erstreckt!«

24Dann segnete Mose den Stamm Asser:

»Asser soll der beliebteste Stamm in Israel sein und noch reicher gesegnet werden als die anderen. Möge es in seinem Land Olivenbäume im Überfluss geben!33,24 Wörtlich: Er tauche seinen Fuß in Öl.

25Seine Stadttore seien mit eisernen Riegeln gesichert, seine Kraft bleibe ungebrochen, solange er besteht.«

26Zuletzt sagte Mose:

»Keiner gleicht dem Gott Israels, der zu seinem geliebten Volk steht. Majestätisch fährt er am Himmel dahin und kommt euch auf den Wolken zu Hilfe.

27Er, der ewige Gott, breitet seine Arme aus, um euch zu tragen und zu schützen. Er hat eure Feinde besiegt und euch befohlen, sie zu vernichten.

28Ihr Israeliten lebt in Ruhe und Sicherheit, niemand stört euren Frieden, ihr Nachkommen von Jakob. Regen fällt vom Himmel auf euer Land, und überall wachsen Getreide und Wein.

29Ihr Israeliten könnt euch glücklich schätzen! Wer hat es so gut wie ihr? Ihr seid das Volk, das der Herr gerettet hat. Er beschützt euch wie ein Schild, und im Kampf ist er euer Schwert. Er bringt euch zu hohem Ansehen. Eure Feinde müssen sich vor euch verbeugen, und ihr besitzt ihr ganzes Land33,29 Oder: tretet auf ihren Rücken.