Deuteronomo 32 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 32:1-52

1Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula;

imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.

2Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula

ndipo mawu anga atsike ngati mame,

ngati mvumbi pa udzu watsopano,

ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.

3Ndidzalalikira dzina la Yehova.

Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!

4Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro,

njira zake zonse ndi zolungama.

Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa,

Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.

5Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake,

iwo si ana akenso,

koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.

6Kodi mukumubwezera Yehova chotere,

inu anthu opusa ndi opanda nzeru?

Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu,

amene anakupangani ndi kukuwumbani?

7Kumbukirani masiku amakedzana;

ganizirani za mibado yakalekale.

Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza,

akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.

8Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo,

pamene analekanitsa anthu onse,

anayikira malire anthu onse

molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.

9Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake,

Yakobo ndiye cholowa chake.

10Anamupeza mʼchipululu,

ku malo owuma ndi kopanda kanthu.

Anamuteteza ndi kumusamalira;

anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,

11ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake

nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake,

chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo

ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.

12Yehova yekha ndiye anamutsogolera;

popanda thandizo la mulungu wachilendo.

13Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko

ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda.

Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe,

ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,

14pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa,

ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi,

pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani

ndiponso tirigu wabwino kwambiri.

Munamwa vinyo wa thovu lofiira.

15Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira;

atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi.

Anasiya Mulungu amene anamulenga

ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.

16Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo

ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.

17Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu,

milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe,

milungu yongobwera kumene,

milungu imene makolo anu sankayiopa.

18Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani;

munayiwala Mulungu amene anakubalani.

19Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana

chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.

20Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga,

ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani;

pakuti ndi mʼbado wopotoka,

ana amene ndi osakhulupirika.

21Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu

ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe.

Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake;

ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.

22Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto,

umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa.

Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake

ndipo udzapsereza maziko a mapiri.

23“Ndidzawawunjikira masautso

ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.

24Ndidzawatumizira njala yoopsa,

malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo;

ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta,

ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.

25Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana;

mantha adzalamulira nyumba zawo.

Anyamata ndi atsikana adzafa,

ngakhalenso makanda ndi okalamba.

26Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza

ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,

27koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze,

mwina adani anga sadzandimvetsetsa

ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife;

Yehova sanachite zonsezi.’ ”

28Iwo ndi mtundu wopanda maganizo,

iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.

29Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi

ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!

30Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000

kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse,

Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa,

Yehova akanapanda kuwataya?

31Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu,

ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.

32Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu

ndiponso ku minda ya ku Gomora.

Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha

ndipo maphava ake ndi owawa.

33Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka,

ululu woopsa wa mphiri.

34“Kodi zimenezi sindinazisunge

ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?

35Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine.

Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera;

tsiku lawo la masautso layandikira

ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”

36Yehova adzaweruza anthu ake

ndipo adzachitira atumiki ake chifundo

pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha

ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.

37Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo,

thanthwe limene ankabisalamo,

38milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo

ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?”

Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni!

Ibwere kuti idzakutetezenitu!

39“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo!

Palibe mulungu wina koma Ine ndekha.

Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo,

ndavulaza ndipo ndidzachiritsa,

ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.

40Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti,

‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,

41pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira

ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo,

ndidzabwezera chilango adani anga

ndi kulanga onse odana nane.

42Mivi yanga idzakhuta magazi awo

pamene lupanga langa lidzawononga mnofu:

magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo,

mitu ya atsogoleri a adani.’ ”

43Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake,

pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake;

adzabwezera chilango adani ake

ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.

44Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva. 45Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli, 46iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa. 47Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”

Mose Adzafera pa Phiri la Nebo

48Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti, 49“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo. 50Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake. 51Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli. 52Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 32:1-52

1«Внимайте, небеса, я буду говорить;

слушай, земля, слова моих уст.

2Пусть польётся моё учение, словно дождь,

пусть сойдут мои слова, как роса,

словно ливень на зелень,

как дождь на побеги.

3Имя Вечного провозглашу,

славьте величие нашего Бога!

4Он – скала, Его дела совершенны,

все Его пути праведны.

Верен Всевышний, не творящий неправды,

Он праведен и честен.

5Перед Ним они развратились,

и не дети они Ему,

но род упрямый и извращённый,

к своему стыду.

6Так ли воздаёте вы Вечному,

народ безрассудный и глупый?

Разве Он не Отец, не Творец твой,

Тот, Кто создал, основал тебя?

7Вспомни древние дни;

подумай об ушедших поколениях.

Спроси своего отца, и он скажет тебе,

своих старейшин, и они объяснят тебе:

8когда Высочайший давал народам их наследие,

когда Он разделил весь человеческий род,

Он поставил пределы народов

по числу сынов Исроила32:8 Или: «сынов Всевышнего»..

9Ведь доля Вечного – народ Исроила,

потомки Якуба – наследственный удел Его.

10В пустынной земле Он его нашёл,

в степи печальной и дикой.

Ограждал его, пёкся о нём;

хранил его, как зеницу Своего ока.

11Как орёл защищает своё гнездо32:11 Или: «учит своих птенцов летать».

и парит над своими птенцами,

простирает свои крылья, берёт птенцов

и несёт на своих перьях,

12так Вечный один его вёл;

чужого бога не было с Ним.

13Он вознёс его на высоты земли

и питал плодами полей.

Он кормил его мёдом из сот,

что в скалистых расщелинах,

и маслом из оливкового дерева,

что растёт на каменистой почве,

14творогом и молоком от стада и отары

и упитанными ягнятами и козлами,

лучшими баранами Бошона

и отборной пшеницей.

Ты пил вино, кровь винограда.

15Исроил32:15 Букв.: «Иешурун» – это слово переводится как «праведный» и является другим, поэтическим именем Исроила. То же в 33:5, 26. растолстел и стал упрям;

растолстел, обрюзг и разжирел.

Он оставил Всевышнего, Который создал его,

и отверг Скалу своего спасения.

16Они возбудили в Нём ревность чужими богами

и разгневали Его мерзкими идолами.

17Они приносили жертвы демонам, а не Всевышнему –

богам, которых не знали,

богам, появившимся недавно,

богам, которых ваши предки не боялись.

18Вы покинули Скалу, родившую вас;

вы забыли Всевышнего, создавшего вас.

19Вечный увидел это и отверг их,

так как разгневался на Своих сыновей и дочерей.

20„Я скрою от них Своё лицо, – сказал Он, –

и увижу, каков будет их конец;

потому что они – извращённый род,

неверные дети.

21Они пробудили во Мне ревность тем, что не Бог,

и разгневали Меня ничтожными идолами.

Я пробужу в них ревность теми, кто не Мой народ;

Я разгневаю их невежественными язычниками;

22потому что от Моего гнева запылал огонь,

что жжёт до дна мира мёртвых.

Он пожрёт землю и её урожаи

и подожжёт основания гор.

23Я соберу на них беды,

выпущу в них свои стрелы.

24Я пошлю на них опустошительный голод,

истребляющий мор и смертельную заразу;

Я пошлю на них хищных зверей,

ядовитых змей, что ползают в прахе.

25На улицах меч лишит их детей,

в их домах будет царить ужас.

Будут гибнуть юноши и девушки,

младенцы и седовласые старики.

26Я сказал бы: рассею их

и изглажу их память из человеческого рода,

27если бы не опасался насмешек врагов,

чтобы противники не возомнили

и не сказали: «Нашей руки торжество;

не Вечный совершил всё это»“.

28Это народ, потерявший рассудок,

нет у них разума.

29О, если бы они были мудры,

то понимали бы это

и уразумели, какой их ждёт конец!

30Как мог бы один человек преследовать тысячу

или двое обратить в бегство десять тысяч,

если бы их Скала не отступилась от них,

если бы Вечный их не выдал?

31Ведь скала врагов не такова, как наша Скала:

даже наши враги сами признают это.

32Их виноград с лозы Содома

и с полей Гоморры.

Их плоды полны яда,

а их гроздья – горечи.

33Их вино – яд змей,

смертельный яд кобр.

34„Я сокрыл злые дела их врагов, – говорит Вечный, –

и запечатал их в своих кладовых.

35Предоставьте месть Мне, Я воздам.

Придёт время, поскользнутся ноги врага;

день их бедствия близок,

и участь их поспешает“.

36Вечный будет судить Свой народ

и пожалеет Своих рабов,

когда увидит, что исчезла их сила

и не осталось никого: ни раба, ни свободного.

37И скажет Он: „Где же их боги,

та скала, за которой они укрывались?

38Боги, которые ели жир их жертв,

пили вино их жертвенных возлияний?

Пусть восстанут, чтобы помочь вам!

Пусть дадут вам покров!

39Смотрите же ныне, что только Я Бог32:39 Букв.: «Я, Я есть Он».,

и нет Бога, кроме Меня.

Я умерщвляю и оживляю,

Я ранил, и Я исцелю,

и никто не может избавить от Моей руки.

40Я поднимаю руку к небу и объявляю:

Верно, как и то, что Я живу вовеки, –

41когда отточу Свой сияющий меч

и рука Моя примет его для суда,

Я отомщу Моим противникам

и воздам тем, кто Меня ненавидит.

42Я напою Мои стрелы кровью,

а Мой меч будет пожирать плоть,

кровь павших и пленных,

головы вражеских вождей“.

43Радуйтесь, народы, вместе с Его народом32:43 Или: «Обрадуйте Его народ, о народы». В некоторых рукописях: «Радуйтесь, небеса, вместе с Ним; пусть все ангелы Всевышнего поклонятся Ему! Радуйтесь, народы, вместе с Его народом; пусть посланники Всевышнего возвещают о Его могуществе!»,

потому что Он отомстит за кровь Своих рабов;

отомстит Он Своим врагам,

очистит Свою землю и Свой народ».

44Мусо пришёл с Иешуа, сыном Нуна, и произнёс народу все слова этой песни. 45Сказав эти слова всему Исроилу, Мусо 46добавил:

– Примите к сердцу все слова, которые я торжественно возвестил вам сегодня, чтобы вы велели своим детям прилежно слушаться всех слов этого Закона. 47Для вас это не пустые слова, в них – ваша жизнь. Они дадут вам долго жить на земле, в которую вы переходите за Иордан, чтобы овладеть ею.

48В тот же день Вечный сказал Мусо:

49– Поднимись на горную цепь Аварим, на гору Нево в Моаве, напротив Иерихона, и осмотри Ханон, землю, которую Я отдаю во владение исроильтянам. 50На этой горе, на которую ты поднимешься, ты умрёшь и присоединишься к своему народу так же, как твой брат Хорун умер на горе Ор и присоединился к своему народу. 51Это случится из-за того, что вы оба изменили Мне у вод Меривы-Кадеша, в пустыне Цин, на глазах у исроильтян, и из-за того, что вы не отстаивали Мою святость среди них32:51 См. Чис. 20:1-13.. 52Поэтому ты увидишь землю, которую Я даю народу Исроила, только на расстоянии – ты не войдёшь в неё.