Deuteronomo 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 3:1-29

Kugonjetsedwa kwa Ogi Mfumu ya ku Basani

1Kenaka tinakhota ndi kumayenda mokwera mtunda ndi njira yolowera ku Basani. Ndipo Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anakumana nafe ndipo anamenyana nafe ku Ederi. 2Yehova anati kwa ine, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”

3Choncho Yehova Mulungu wathu anapereka mʼmanja mwathu Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo. Tinawakantha onsewo osasiya ndi mmodzi yemwe. 4Pa nthawi imeneyo tinatenga mizinda yake yonse. Pa mizinda 60, panalibe ndi umodzi womwe umene sitinawalande, mʼdera lonse la ufumu wa Ogi ku Basani chimene ndi chigawo cha Arigobu. 5Mizinda yonseyi inali yotetezedwa ndi malinga ataliatali wokhala ndi zitseko ndi zitsulo, komabe panali midzi ina yambiri imene inalibe malinga. 6Tinawawonongeratu monga momwe tinachitira Sihoni, mfumu ya ku Hesiboni. Tinawononga mzinda uliwonse, amayi, amuna ndi ana omwe. 7Koma tinafunkha ziweto ndi katundu wawo yense.

8Choncho pa nthawi imeneyi tinalanda kwa mafumu awiri Aamori, dera la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku khwawa la Arinoni mpaka ku Phiri la Herimoni. 9(Asidoni amatcha Herimoni kuti Siriyoni, pamene Aamori amalitcha Seniri). 10Tinalanda mizinda yonse ya ku mapiri, ku Giliyadi, Basani mpaka ku Saleka ndi Ederi, mizinda ya mu ufumu wa Ogi wa ku Basani. 11(Ogi, mfumu ya ku Basani, anali yekhayo amene anatsala mwa mtundu wa anthu ataliatali a Chirefai. Bedi lake linali lachitsulo ndipo lalitali kuposa mamita anayi. Mulifupi mwake munali mamita awiri. Bedilo likanalipo ku Raba kwa Aamori).

Kugawana Dziko

12Dziko limene tinalanda nthawi imeneyo, ndinapatsa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi dera la kumpoto kwa Aroeri cha mʼmphepete mwa khwawa la Arinoni kuphatikizapo theka la dziko lamapiri la Giliyadi ndi mizinda yake. 13Theka la fuko la Manase ndinalipatsa dziko lonse lotsala la Giliyadi ndi Basani yense yemwe ndi dera la ufumu wa Ogi. (Chigawo chonse cha Arigobu mu Basani chinkadziwika kuti ndi dziko la Arefai. 14Yairi, mdzukulu wa Manase, anatenga chigawo chonse cha Arigobu mpaka ku malire a Agesuri ndi Amaakati. Anatcha chigawochi dzina lake, moti mpaka lero Basani amatchedwa Havoti Yairi). 15Ndipo ndinapereka Giliyadi kwa Makiri. 16Koma kwa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi ndinapereka chigawo chochokera ku Giliyadi kutsetsereka mpaka ku khwawa la Arinoni (pakati pa khwawalo ndiye panali malire) ndi kupitirira mpaka ku mtsinje wa Yaboki umene ndi malire Aamoni. 17Malire ake a chakumadzulo anali Yorodani ku Araba, kuchokera ku Kinereti mpaka ku Nyanja ya Araba (Nyanja ya Mchere), mʼmunsi mwa matsitso a Pisiga.

18Ndinakulamulirani nthawi imene ija kuti, “Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili kuti likhale lanu. Koma amuna amphamvu onse ali ndi zida zankhondo, awoloke kutsogolera abale anu Aisraeli. 19Koma akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu (ndikudziwa kuti muli ndi ziweto zambiri) zikhoza kumakhalabe mʼmizinda imene ndakupatsani, 20mpaka Yehova atapereka mpumulo kwa abale anu, nawonso atatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa patsidya pa Yorodani, monga wachitira ndi inu. Kenaka, aliyense wa inu akhoza kudzabwerera ku dziko limene ndinakupatsani.”

Mose Aletsedwa Kuwoloka Yorodani

21Nthawi imeneyo ndinamulamula Yoswa kuti, “Waona wekha ndi maso ako zonse zimene Yehova Mulungu wako anachitira mafumu awiriwa. Yehova adzachita zomwezo ndi mafumu ena onse kumene mukupitako. 22Musawaope chifukwa Yehova Mulungu mwini adzakumenyerani nkhondo.”

23Nthawi imeneyo ndinachonderera Yehova kuti, 24“Ambuye Mulungu, mwayamba tsopano kuonetsa mtumiki wanu ukulu wanu ndi dzanja lanu lamphamvu. Ndi mulungu uti ali kumwamba kapena pa dziko lapansi amene angachite ntchito zozizwitsa zimene mumachita? 25Mundilole ndipite ndi kukaona dziko labwinolo kutsidya kwa Yorodani dziko la mapiri abwinowo ndi Lebanoni.”

26Koma chifukwa cha inu, Yehova anakwiya nane osandimvera. Yehova anati, “Basi pakwana, usayankhulenso ndi ine zimenezi. 27Pita pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo uyangʼane kumadzulo, kumpoto, kummwera ndi kummawa. Ulione dzikolo ndi maso ako pakuti suwoloka Yorodaniyu. 28Koma langiza Yoswa ndipo umulimbikitse ndi kumupatsa mphamvu pakuti adzatsogolera anthu awa kuwoloka ndipo adzawathandiza kuti atenge dziko limene ulioneli.” 29Ndipo tinakhala mʼchigwa pafupi ndi Beti-Peori.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 3:1-29

1Затим смо се окренули и кренули горе путем за Васан. Тада је Ог, васански цар, и сав његов народ, изашао у бој против нас код Едрајина. 2Тада ми Господ рече: ’Не бој га се, јер сам у твоје руке предао и њега, и сав његов народ и његову земљу. Учини с њим као што си учинио с аморејским царем Сихоном, који је живео у Есевону.’

3Господ, наш Бог, је предао у наше руке васанског цара Ога и сав његов народ; тако да му није остао ни један преживели. 4У то време смо заузели све његове градове. Није било града који им нисмо одузели – шездесет градова, то јест, целу област Аргов, Огово царство у Васану. 5Сви ови градови су били утврђени високим зидинама, вратима и преворницама. Уз њих је било много неутврђених села. 6И над њима смо извршили клето уништење, као што смо учинили са есевонским царем Сихоном, када смо извршили клето уништење над свим њиховим градовима: над мушкарцима, женама и децом. 7Запленили смо само стоку и однели плен из градова.

8Тако смо у оно време отели земљу из руку двојице аморејских царева, што се налази с оне стране Јордана, од потока Арнона до горе Ермон 9(Сидонци зову Ермон Сирјон а Аморејци га зову Сенир), 10све градове у равници, у целом Галаду, целом Васану, све до Салке и Едрајина – градове Оговог царства у Васану. 11(Ог, васански цар, је једини преостали Рефаимац. Његов гвоздени кревет се још увек налази у Рави амонској. Био је девет лаката дуг и четири лакта3,11 Око 4,5 m дуг и 2 m широк. широк, мерено обичним лактом.)

Подела земље

12У то време смо освојили ову земљу од Ароира који је код потока Арнона. Пола галадског горја и његове градове дао сам Рувимовом и Гадовом племену. 13Што је остало од Галада и цели Васан, Огово царство, дао сам половини Манасијиног племена. Цела арговска област и сав Васан некада су се звали ’земља Рефаимаца’. 14Јаир, Манасијин син, је освојио цели арговски крај до гесурске и махатске границе. Та васанска места је назвао по себи, тако да се и дан данас зову ’Јаирова села’. 15Махиру сам дао Галад. 16Рувимовом и Гадовом племену сам дао подручје од Галада код потока Арнона, чијом средином се пружа граница, све до потока Јавока, где је Амонска граница. 17(Јордан и Арава су служили као граница која се протезала од језера Хинерет до мора код Араве – Мртвог мора – подно обронака Фасге на истоку.)

18У оно време сам вам заповедио: ’Господ, Бог ваш, дао вам је ову земљу да је запоседнете. Сви ви који сте способни за бој крените наоружани испред своје браће. 19Нека само ваше жене, нејач и стока – јер знам да имате много стоке – остану у вашим градовима које сам вам дао. 20Кад Господ да починак вашој браћи и вама, те кад освоје земљу коју им Господ даје с оне стране Јордана, тада сваки човек нека се врати на посед који сам вам дао.’

21У оно време сам заповедио Исусу: ’Својим очима си видео све што је Господ, Бог твој, учинио овој двојици царева; Господ ће тако учинити и другим царствима кроз која будеш пролазио. 22Не плаши их се, јер ће се Господ, Бог ваш, борити за вас.’

Мојсију недозвољен прелазак Јордана

23У оно време сам молио Господа: 24’Господе, Боже, ти си почео да показујеш своме слузи своју величину и своју моћну руку. Јер, који то Бог на небесима или на земљи може да чини таква дела и чудеса? 25Сада ми допусти да уђем и видим добру земљу с оне стране Јордана, предивно горје и Ливан.’

26Али се Господ наљутио на мене због вас и није ме послушао. Господ ми је рекао: ’Доста! Не помињи ми више ово! 27Успни се на врх Фасге и дигни свој поглед према западу и северу, према југу и истоку. Добро погледај својим очима, јер нећеш прећи преко овог Јордана. 28Исуса уведи у дужност; охрабри га и осоколи, јер ће он предводити овај народ и довести их да приме у посед ову земљу коју ћеш видети.’ 29Тако смо остали у долини код Вет-Фегора.