Deuteronomo 3 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 3:1-29

Kugonjetsedwa kwa Ogi Mfumu ya ku Basani

1Kenaka tinakhota ndi kumayenda mokwera mtunda ndi njira yolowera ku Basani. Ndipo Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anakumana nafe ndipo anamenyana nafe ku Ederi. 2Yehova anati kwa ine, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”

3Choncho Yehova Mulungu wathu anapereka mʼmanja mwathu Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo. Tinawakantha onsewo osasiya ndi mmodzi yemwe. 4Pa nthawi imeneyo tinatenga mizinda yake yonse. Pa mizinda 60, panalibe ndi umodzi womwe umene sitinawalande, mʼdera lonse la ufumu wa Ogi ku Basani chimene ndi chigawo cha Arigobu. 5Mizinda yonseyi inali yotetezedwa ndi malinga ataliatali wokhala ndi zitseko ndi zitsulo, komabe panali midzi ina yambiri imene inalibe malinga. 6Tinawawonongeratu monga momwe tinachitira Sihoni, mfumu ya ku Hesiboni. Tinawononga mzinda uliwonse, amayi, amuna ndi ana omwe. 7Koma tinafunkha ziweto ndi katundu wawo yense.

8Choncho pa nthawi imeneyi tinalanda kwa mafumu awiri Aamori, dera la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku khwawa la Arinoni mpaka ku Phiri la Herimoni. 9(Asidoni amatcha Herimoni kuti Siriyoni, pamene Aamori amalitcha Seniri). 10Tinalanda mizinda yonse ya ku mapiri, ku Giliyadi, Basani mpaka ku Saleka ndi Ederi, mizinda ya mu ufumu wa Ogi wa ku Basani. 11(Ogi, mfumu ya ku Basani, anali yekhayo amene anatsala mwa mtundu wa anthu ataliatali a Chirefai. Bedi lake linali lachitsulo ndipo lalitali kuposa mamita anayi. Mulifupi mwake munali mamita awiri. Bedilo likanalipo ku Raba kwa Aamori).

Kugawana Dziko

12Dziko limene tinalanda nthawi imeneyo, ndinapatsa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi dera la kumpoto kwa Aroeri cha mʼmphepete mwa khwawa la Arinoni kuphatikizapo theka la dziko lamapiri la Giliyadi ndi mizinda yake. 13Theka la fuko la Manase ndinalipatsa dziko lonse lotsala la Giliyadi ndi Basani yense yemwe ndi dera la ufumu wa Ogi. (Chigawo chonse cha Arigobu mu Basani chinkadziwika kuti ndi dziko la Arefai. 14Yairi, mdzukulu wa Manase, anatenga chigawo chonse cha Arigobu mpaka ku malire a Agesuri ndi Amaakati. Anatcha chigawochi dzina lake, moti mpaka lero Basani amatchedwa Havoti Yairi). 15Ndipo ndinapereka Giliyadi kwa Makiri. 16Koma kwa fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi ndinapereka chigawo chochokera ku Giliyadi kutsetsereka mpaka ku khwawa la Arinoni (pakati pa khwawalo ndiye panali malire) ndi kupitirira mpaka ku mtsinje wa Yaboki umene ndi malire Aamoni. 17Malire ake a chakumadzulo anali Yorodani ku Araba, kuchokera ku Kinereti mpaka ku Nyanja ya Araba (Nyanja ya Mchere), mʼmunsi mwa matsitso a Pisiga.

18Ndinakulamulirani nthawi imene ija kuti, “Yehova Mulungu wanu wakupatsani dziko ili kuti likhale lanu. Koma amuna amphamvu onse ali ndi zida zankhondo, awoloke kutsogolera abale anu Aisraeli. 19Koma akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu (ndikudziwa kuti muli ndi ziweto zambiri) zikhoza kumakhalabe mʼmizinda imene ndakupatsani, 20mpaka Yehova atapereka mpumulo kwa abale anu, nawonso atatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa patsidya pa Yorodani, monga wachitira ndi inu. Kenaka, aliyense wa inu akhoza kudzabwerera ku dziko limene ndinakupatsani.”

Mose Aletsedwa Kuwoloka Yorodani

21Nthawi imeneyo ndinamulamula Yoswa kuti, “Waona wekha ndi maso ako zonse zimene Yehova Mulungu wako anachitira mafumu awiriwa. Yehova adzachita zomwezo ndi mafumu ena onse kumene mukupitako. 22Musawaope chifukwa Yehova Mulungu mwini adzakumenyerani nkhondo.”

23Nthawi imeneyo ndinachonderera Yehova kuti, 24“Ambuye Mulungu, mwayamba tsopano kuonetsa mtumiki wanu ukulu wanu ndi dzanja lanu lamphamvu. Ndi mulungu uti ali kumwamba kapena pa dziko lapansi amene angachite ntchito zozizwitsa zimene mumachita? 25Mundilole ndipite ndi kukaona dziko labwinolo kutsidya kwa Yorodani dziko la mapiri abwinowo ndi Lebanoni.”

26Koma chifukwa cha inu, Yehova anakwiya nane osandimvera. Yehova anati, “Basi pakwana, usayankhulenso ndi ine zimenezi. 27Pita pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo uyangʼane kumadzulo, kumpoto, kummwera ndi kummawa. Ulione dzikolo ndi maso ako pakuti suwoloka Yorodaniyu. 28Koma langiza Yoswa ndipo umulimbikitse ndi kumupatsa mphamvu pakuti adzatsogolera anthu awa kuwoloka ndipo adzawathandiza kuti atenge dziko limene ulioneli.” 29Ndipo tinakhala mʼchigwa pafupi ndi Beti-Peori.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 3:1-29

Победа над царём Огом

(Чис. 21:33-35)

1Потом мы повернули и поднялись по дороге к Бошону. Ог, царь Бошона, выступил нам навстречу со всем своим войском, чтобы сразиться с нами у города Эдреи. 2Вечный сказал мне: «Не бойся его, потому что Я отдам его в твои руки со всем его войском и землёй. Сделай с ним то же, что и с Сигоном, царём аморреев, который правил в Хешбоне». 3И Вечный, наш Бог, отдал в наши руки ещё и Ога, царя Бошона, и всё его войско. Мы поразили их, не оставив в живых никого. 4Тогда же мы взяли и все его города. Мы взяли все шестьдесят городов – всю область Аргов, царство Ога в Бошоне. 5Все эти города были укреплены высокими стенами, двойными воротами и запорами, а кроме них было множество селений, не обнесённых стенами. 6Мы полностью истребили их, как народ Сигона, царя Хешбона, истребляя всех – мужчин, женщин и детей. 7Но весь скот и добычу из их городов мы взяли себе.

8Итак, в то время мы взяли у этих двух аморрейских царей землю к востоку от Иордана, от реки Арнон до самой горы Хермон. 9(Сидоняне называют Хермон Сирионом, а аморреи – Сениром.) 10Мы взяли все их города на плоскогорье, весь Галаад и весь Бошон до Салхи и Эдреи, города царства Ога в Бошоне. 11(Ог, царь Бошона, был одним из последних рефаитов (народа гигантов). Его ложе3:11 Или: «саркофаг». было сделано из железа и имело четыре метра в длину и почти два метра3:11 Букв.: «девять… четыре локтя». в ширину. Оно и сейчас находится в Раббе, столице аммонитян.)

Раздел земли к востоку от Иордана

(Чис. 32:1-42)

12Из земли, которой мы завладели в то время, я отдал родам Рувима и Гада область к северу от Ароера у реки Арнон, включая половину нагорий Галаада вместе с городами. 13Остальную часть Галаада, а также весь Бошон, царство Ога, я отдал половине рода Манассы.

(Вся область Аргов в Бошоне прежде была известна как земля рефаитов. 14Иаир, потомок Манассы, захватил всю область Аргов до самой границы гешуритов и маахитян. Он назвал её своим собственным именем, и до сегодняшнего дня Бошон называется Хаввот-Иаир («селения Иаира»).)

15Я отдал Галаад клану Махира. 16А рувимитам и гадитам я дал землю, что спускается от Галаада к реке Арнон (с границей на середине реки) и к реке Иаббок, которая служит границей земель аммонитян. 17Я также дал им Иорданскую долину, включая Иордан с его восточными берегами, от Генисаретского озера до Мёртвого моря3:17 Букв.: «от Киннерета до моря Аравы, Солёного моря». и до склонов Фасги к востоку.

18В то время я повелел вам: «Вечный, ваш Бог, отдал вам эту землю, чтобы вы завладели ею. Все ваши мужчины, способные сражаться и вооружённые для битвы, должны переправиться за реку перед вашими братьями исроильтянами. 19Ваши жёны, дети и скот (я знаю, у вас много скота) могут остаться в городах, которые я вам дал, 20пока Вечный не даст покой вашим братьям, как и вам, и пока они не примут также во владение землю, которую Вечный, ваш Бог, даёт им за Иорданом. После этого каждый из вас может вернуться к владению, которое я вам дал».

21В то время я повелел Иешуа: «Ты своими глазами видел всё, что Вечный, ваш Бог, сделал с этими двумя царями. Вечный сделает то же самое со всеми царствами, которые ты будешь проходить. 22Не бойся их: Вечный, ваш Бог, Сам будет сражаться за вас».

Мусо запрещено переходить Иордан

23В то время я молил Вечного: 24«Владыка Вечный, Ты являешь Своему рабу Своё величие и силу. Разве есть какой-нибудь другой бог на небе или на земле, который смог бы совершить такие же подвиги и великие дела, какие делаешь Ты? 25Позволь мне переправиться и увидеть благодатную землю за Иорданом – те прекрасные нагорья и Ливан».

26Но из-за вас Вечный разгневался и не услышал меня. «Хватит, – сказал Вечный, – не говори Мне больше об этом. 27Поднимись на вершину Фасги и посмотри на запад, на север, на юг и на восток. Посмотри на землю своими собственными глазами, потому что ты не перейдёшь за Иордан. 28Но наставь Иешуа, утверди и укрепи его, потому что он переправится во главе народа и разделит между ними землю, которую ты увидишь». 29И мы остановились в долине рядом с Бет-Пеором.