Deuteronomo 28 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 28:1-68

Madalitso Akumvera

1Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi. 2Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:

3Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.

4Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.

5Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.

6Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

7Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.

8Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.

9Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake. 10Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani. 11Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.

12Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense. 13Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi. 14Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.

Matemberero Akusamvera

15Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:

16Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.

17Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.

18Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.

19Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.

20Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova. 21Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali. 22Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka. 23Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo. 24Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.

25Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi. 26Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse. 27Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo. 28Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo. 29Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.

30Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake. 31Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa. 32Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako. 33Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse. 34Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu. 35Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.

36Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala. 37Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.

38Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga. 39Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo. 40Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka. 41Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo. 42Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.

43Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi. 44Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.

45Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani. 46Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale. 47Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino, 48chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.

49Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva, 50mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana. 51Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja. 52Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

53Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani. 54Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo, 55ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse. 56Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi 57zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.

58Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu, 59Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika. 60Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani. 61Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka. 62Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu. 63Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.

64Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo. 65Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika. 66Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu. 67Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona. 68Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 28:1-68

Благословения за послушание

(Лев. 26:1-13; Втор. 7:12-16)

1Если ты будешь полностью послушен Вечному, твоему Богу, и будешь прилежно исполнять все Его повеления, которые я даю тебе сегодня, то Вечный, твой Бог, поставит тебя выше всех народов на земле. 2Все эти благословения ты получишь, если будешь слушаться Вечного, твоего Бога.

3Ты будешь благословен в городе и благословен в селении28:3 Или: «на поле», также в ст. 16..

4Благословен будешь ты множеством детей, земля твоя принесёт обильный урожай, а стада твои и отары – большой приплод: телят и ягнят.

5Твоя корзина и твоя квашня никогда не будут пусты.

6Ты будешь благословен, когда будешь входить и когда будешь выходить.

7Вечный сделает так, что враги, которые поднимутся против тебя, будут разбиты перед тобой. Они пойдут на тебя по одной дороге, но побегут от тебя по семи.

8Вечный наполнит твои амбары и благословит всё, что ты будешь делать своими руками. Вечный, твой Бог, благословит тебя на земле, которую Он даёт тебе.

9Вечный поставит тебя Своим святым народом, как Он клялся тебе, если ты будешь исполнять повеления Вечного, твоего Бога, и ходить Его путями. 10Тогда все народы на земле увидят, что над тобой провозглашено имя Вечного, и будут бояться тебя. 11Вечный даст тебе изобилие во всём – в твоих детях, приплоде скота и урожаях земли – на земле, которую Он клялся твоим предкам дать тебе.

12Вечный откроет тебе небеса, свою богатую сокровищницу, чтобы посылать дождь в срок на твою землю и благословлять всякое дело твоих рук. Ты будешь давать взаймы многим народам, а занимать не будешь ни у кого. 13Вечный сделает тебя головой, а не хвостом. Если ты будешь внимателен к повелениям Вечного, твоего Бога, которые я даю тебе сегодня, и будешь прилежно исполнять их, то ты всегда будешь наверху, а не внизу. 14Не уклоняйся ни от одного из повелений, которые я даю тебе сегодня, ни вправо, ни влево, не следуй за другими богами и не служи им.

Проклятия за непослушание

(Лев. 26:14-39)

15Но если ты не будешь послушен Вечному, твоему Богу, и не будешь прилежно исполнять все Его повеления и установления, которые я даю тебе сегодня, все эти проклятия придут на тебя и будут с тобой.

16Ты будешь проклят в городе и проклят в селении.

17Твоя корзина и твоя квашня всегда будут пусты.

18Дети твои будут немногочисленны, твоя земля будет давать скудный урожай, а стада твои и отары принесут мало приплода: телят и ягнят.

19Ты будешь проклят, когда будешь входить и когда будешь выходить.

20Вечный будет посылать на тебя проклятие, смятение и неудачу во всех делах твоих рук, пока ты не будешь истреблён и не придёшь к быстрой погибели из-за того зла, которое ты сделал, оставив Меня. 21Вечный будет насылать на тебя мор за мором, пока не истребит тебя с земли, в которую ты вступаешь, чтобы завладеть ею. 22Вечный нашлёт на тебя чахотку, лихорадку и воспаление, жару и засуху, знойный ветер и плесень, которые будут преследовать тебя, пока ты не погибнешь. 23Небо над твоей головой станет медью, земля под тобой – железом28:23 То есть не будет дождя, небо будет источать жар, и земля не будет способна что-либо произрастить.. 24Вечный даст твоей стране пыль вместо дождя, и только прах будет падать на тебя с небес, пока ты не погибнешь.

25Вечный сделает так, что ты будешь разбит врагами. Ты пойдёшь на них по одной дороге, а побежишь от них по семи и станешь отвратителен всем царствам на земле. 26Твои трупы будут пищей всем небесным птицам и земным зверям, и некому будет отпугнуть их. 27Вечный нашлёт на тебя нарывы и опухоли Египта28:27 См. Исх. 9:8-11., гноящиеся язвы и чесотку, от которых ты не сможешь исцелиться. 28Вечный поразит тебя безумием, слепотой и помрачением ума. 29В полдень ты будешь бродить на ощупь, как слепец во тьме. Ты будешь неудачлив во всём, что будешь делать; изо дня в день тебя будут притеснять и грабить, и не будет у тебя защитника.

30Ты обручишься с женщиной, но другой возьмёт её и будет спать с ней. Ты построишь дом, но не будешь в нём жить. Ты посадишь виноградник, но не успеешь собрать даже первый урожай. 31Твоего вола заколют у тебя на глазах, но ты не будешь есть его мясо. Твоего осла уведут у тебя силой и не вернут. Твои овцы достанутся врагам, и никто не спасёт их для тебя. 32Твоих сыновей и дочерей отдадут другому народу, и ты истомишь свои глаза, разыскивая их изо дня в день, бессильный хоть что-нибудь сделать. 33Народ, которого ты не знал, будет есть то, что ты произвёл своим трудом на своей земле, а тебя будут только жестоко притеснять всю твою жизнь. 34Ты сойдёшь с ума от того, что увидишь. 35Вечный поразит твои колени и голени болезненными неисцелимыми нарывами, которые распространятся от ступней твоих ног до самого темени.

36Вечный уведёт тебя и царя, которого ты поставишь над собой, к народу неизвестному ни тебе, ни твоим предкам. Там ты будешь служить другим богам, богам из дерева и камня. 37Тебя будут презирать и над тобой будут насмехаться, ты будешь отвратителен всем тем народам, к которым уведёт тебя Вечный.

38Ты будешь сеять на поле много семян, но соберёшь бедный урожай, потому что его пожрёт саранча. 39Ты будешь сажать виноградники и ухаживать за ними, но не пить тебе вина, не собирать плода, потому что виноград сожрут черви. 40По всей стране будут расти маслины, но не видать тебе масла, потому что оливки осыплются. 41У тебя будут сыновья и дочери, но ты не сохранишь их, потому что их уведут в плен. 42Рои саранчи захватят твои деревья и урожаи твоей земли.

43Живущий у тебя чужеземец будет подниматься над тобой всё выше и выше, а ты будешь опускаться всё ниже и ниже. 44Он будет давать тебе взаймы, а ты не будешь давать ему взаймы. Он будет головой, а ты будешь хвостом.

45Все эти проклятия падут на тебя. Они будут преследовать и настигать тебя, пока ты не погибнешь, потому что ты не слушался Вечного, твоего Бога, и не соблюдал повелений и установлений, которые Он дал тебе. 46Эти бедствия будут свидетельством и знамением для тебя и твоего потомства вовеки. 47Так как ты не служил Вечному, твоему Богу, с весельем и радостью во время изобилия, 48то в голоде и жажде, в наготе и страшной нищете ты будешь служить врагам, которых Вечный пошлёт на тебя. Он наденет тебе на шею железное ярмо, пока не погубит тебя.

49Вечный нашлёт на тебя народ издалека, с дальних концов земли, подобный налетающему орлу, народ, чьего языка ты не будешь понимать, 50безжалостный народ, не уважающий старика и не щадящий юноши. 51Он будет пожирать приплод твоего скота и урожаи твоей земли, пока не истребит тебя. Он не оставит тебе ни зерна, ни молодого вина, ни масла, ни телят твоего стада, ни ягнят твоей отары, пока не погубит тебя. 52Он будет осаждать все твои города по всей земле, пока высокие, укреплённые стены, на которые ты полагаешься, не падут. Он будет осаждать все города по всей земле, которую Вечный, твой Бог, даёт тебе.

53Из-за страданий, которые враги причинят тебе во время осады, ты будешь есть своих детей, плоть своих сыновей и дочерей, которых дал тебе Вечный, твой Бог. 54Даже самый изнеженный и чувствительный из ваших людей не станет сострадать28:54 Букв.: «У человека изнеженного и чувствительного среди вас будет дурной глаз против…» См. сноску на 15:9. собственному брату, или любимой жене, или своим уцелевшим детям 55и не даст никому из них ничего из плоти своих детей, которых будет есть сам. Это всё, что у него останется. Вот какие страдания враг причинит тебе во время осады всех твоих городов. 56Самая изнеженная и чувствительная из твоих женщин – такая изнеженная и чувствительная, что не привыкла ступать по земле – поскупится дать28:56 Букв.: «У женщины изнеженной и чувствительной среди вас… будет дурной глаз против…» См. сноску на 15:9. любимому мужу и собственному сыну или дочери 57послед из своего чрева и детей, которых родит. Ведь она захочет съесть их тайно во время осады и в бедствии, которое враг причинит тебе во всех твоих городах.

58Если ты не будешь прилежно следовать всем словам Закона, который записан в этом свитке, и не будешь чтить славное и страшное имя Вечного, твоего Бога28:58 Чтить чьё-либо имя, значит чтить самого носителя этого имени, в данном случае чтить Вечного., 59то Вечный наведёт на тебя и на твоих потомков ужасные несчастья, жестокие и продолжительные бедствия и свирепые, затяжные болезни. 60Он наведёт на тебя все недуги Египта, которых ты ужасался, и они пристанут к тебе. 61Ещё Вечный наведёт на тебя такие болезни и беды, о которых не говорится в этом свитке Закона, пока ты не погибнешь. 62Вас было много, как звёзд на небе, но останется мало, потому что вы не были послушны Вечному, вашему Богу. 63Как Вечный радовался, делая вам добро и умножая ваше число, так Он будет радоваться, губя и истребляя вас. Вы будете искоренены из земли, куда вы вступаете, чтобы завладеть ею.

64Тогда Вечный рассеет вас по всем народам, от одного конца земли до другого. Там вы будете служить другим богам – богам из дерева и камня, которых не знали ни вы, ни ваши предки. 65Между теми народами вы не обретёте покоя, и не будет спокойного места, куда могла бы ступить ваша нога. Там Вечный заставит ваше сердце трепетать, истомит тоской ваши глаза и наполнит отчаянием вашу душу. 66Вы будете жить в постоянной тревоге, полные ужаса и днём, и ночью, никогда не уверенные в своей жизни. 67Утром вы скажете: «Ах, скорее бы вечер!» – а вечером: «О, скорее бы утро!» – от ужаса, который наполнит ваши сердца, и из-за того, что увидят ваши глаза. 68Вечный возвратит вас на кораблях в Египет тем путём, о котором я говорил, что вы никогда не проделаете его вновь. Там вы будете предлагать себя на продажу как рабов и рабынь своим врагам, но никто вас не купит.