Deuteronomo 27 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 27:1-26

Guwa Lansembe ku Phiri la Ebala

1Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino. 2Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza. 3Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani. 4Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize. 5Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo. 6Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu. 7Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 8Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”

Matemberero Kuchokera ku Phiri la Ebala

9Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu. 10Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”

11Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:

12Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini. 13Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.

14Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:

15“Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

16“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

17“Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

18“Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

19“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

20“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

21“Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

22“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

23“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

24“Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

25“Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”

26“Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”

Pamenepo anthu onse adzati, “Ameni!”