Deuteronomo 26 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 26:1-19

Zipatso Zoyamba ndi Chakhumi

1Mukalowa ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, 2mutengeko zina mwa zipatso zoyamba pa zonse zimene mudzakola mʼnthaka ya dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ndi kuziyika mʼdengu. Mukatero mupite kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzakhazikitsako dzina lake 3ndipo mudzamuwuze wansembe amene ali pa ntchito pa nthawiyo kuti, “Ndikunenetsa lero kwa Yehova Mulungu wanu kuti ndabwera ku dziko limene Yehova analumbirira makolo athu kuti adzatipatsa ife.” 4Wansembe adzatenga dengulo mʼmanja mwanu ndi kuliyika pansi patsogolo pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu. 5Ndipo mudzanenetsa pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, “Abambo anga anali Mwaramu woyendayenda, anapita ku Igupto ndi anthu ochepa nakhala kumeneko. Pambuyo pake anakhala mtundu waukulu, wamphamvu ndi wochuluka. 6Koma Aigupto anatisautsa natizunza, kumatigwiritsa ntchito yakalavulagaga. 7Kenaka tinafuwulira Yehova, Mulungu wa makolo athu ndipo Yehova anamva mawu athu ndi kuona kusauka, kuvutika ndi kuponderezedwa kwathu. 8Kotero Yehova anatitulutsa ku Igupto ndi dzanja lake lamphamvu ndi mkono wotambasuka ndi zoopsa zazikulu ndi zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa. 9Iye anatibweretsa ku malo ano natipatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi lino. 10Ndipo tsopano ndikubweretsa zipatso zoyamba zimene inu Yehova mwandipatsa.” Ikani dengulo pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kuwerama mopereka ulemu pamaso pake. 11Ndipo inu ndi Alevi pamodzi ndi alendo okhala pakati panu mudzakondwera mʼzinthu zonse zabwino zimene Yehova Mulungu wanu wakupatsani, inu ndi a pa banja panu.

12Mukatha kupatula chakhumi pa zonse zimene mwakolola mʼchaka chachitatu chimene ndi chaka chakhumi, muzichipereka kwa wansembe, mlendo, ana ndi akazi amasiye, kuti pamenepo adye mʼmizinda yanu nakhuta. 13Kenaka munene kwa Yehova Mulungu wanu kuti “Ndatulutsamo mʼnyumba mwanga gawo lopatulika ndipo ndalipereka kwa Mlevi, mlendo, ana ndi akazi amasiye, monga mwa zonse zimene munalamula. Sindinapatuke pa zimene munalamula kapena kuyiwala ndi chimodzi chomwe. 14Sindinadye kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndimalira maliro kapena kuchotsapo kalikonse ka gawo lopatulika pamene ndinali wodetsedwa, kapena kuperekako nsembe kwa akufa kalikonse ka gawoli. Ine ndamvera Yehova Mulungu wanga, ndachita chilichonse chimene inu munandilamula. 15Yangʼanani pa dziko kuchokera kumwamba, ku malo anu wopatulika, ndi kudalitsa anthu anu Aisraeli ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi limene mwatipatsa ife monga momwe munalonjezera pa malumbiro anu kwa makolo athu.”

Tsatirani Malamulo a Yehova

16Yehova Mulungu wanu akukulamulani lero lino kuti mutsate malangizo ndi malamulo ake ndipo muwasunge mosamalitsa ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse. 17Mwanena motsimikiza lero lino kuti Yehova ndiye Mulungu wanu ndi kuti mudzayenda mʼnjira zake, kusunga malangizo, malamulo ndi zonse akukulamulani ndi kutinso mudzamumvera. 18Ndipo Yehova wanenetsa lero lino kuti inu ndinu anthu ake, chuma chake chamtengowapatali monga momwe analonjezera, ndipo mukuyenera kusunga malamulo ake onse. 19Iye wanenetsa kuti adzakuyikani kukhala oyamikika, otchuka ndi olemekezeka koposa mitundu yonse imene anayilenga. Komanso mudzakhala anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu monga momwe analonjezera.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 26:1-19

Први плодови и десетак

1А кад дођеш у земљу коју ти Господ, Бог твој, даје у наследство, и ти је заузмеш и настаниш се у њој, 2узми нешто од првине свих пољских плодова које ти роди земља, коју ти даје Господ, Бог твој, стави их у кошару и иди на место које изабере Господ, Бог твој, да тамо настани своје име. 3Иди к свештенику који буде служио у то време и реци му: ’Изјављујем данас пред Господом, Богом твојим, да сам ушао у земљу за коју се Господ заклео нашим оцима да ће нам је дати.’ 4Затим нека свештеник узме кошару из твоје руке и положи је пред жртвеник Господа, Бога твога. 5Ти ћеш на то изговорити пред Господом, Богом твојим: ’Мој је отац био арамејски луталица који је сишао у Египат и боравио тамо као странац са шачицом људи. Тамо је постао народ велики, моћан и бројан. 6Али Египћани су нас злостављали и угњетавали, и наметнули нам тежак рад. 7Тада смо завапили Господу, Богу наших отаца, и Господ је чуо наш глас и видео наш јад, мукотрпни рад и потлаченост. 8Господ нас је извео из Египта моћном руком, испруженом мишицом, великом страхотом, те знацима и чудима. 9Он нас је довео до овог места и дао нам ову земљу, земљу којом теку млеко и мед. 10Сада, ево, приносим прве плодове земље, коју си ми ти, о, Господе, дао.’ Затим положи то пред Господа, Бога свога, па се поклони пред Господом, Богом својим. 11И радуј се заједно са Левитом и дошљаком у твојој средини за све добро што је теби и твоме дому дао Господ, Бог твој.

12А кад у трећој години, години десетка, завршиш са издвајањем свег десетка од годишњег урода, и кад га даш Левиту, странцу, сирочету и удовици, да једу и да се насите, 13реци пред Господом, Богом својим: ’Уклонио сам из куће све што је посвећено Господу. Шта више, то сам дао Левиту, странцу, сирочету и удовици, према твојој заповеди коју си ми дао. Нисам прекршио, нити заборавио, ниједну од твојих заповеди. 14У својој жалости ништа од тога нисам јео, ништа од тога нисам уклањао кад сам био нечист, нити сам ишта од тога приносио мртвацу. Послушао сам глас Господа, Бога свога, и учинио онако како ми је заповедио. 15Погледај с небеса, из свог светог Пребивалишта, па благослови свој народ, Израиљ, и земљу коју си нам дао, земљу којом теку млеко и мед – како си се заклео нашим оцима!’

Позив на послушност

16Данас ти Господ, Бог твој, заповеда да вршиш ове уредбе и прописе. Држи их и врши свим својим срцем и свом својом душом. 17Данас си изјавио да ће Господ бити твој Бог, и да ћеш следити његове путеве и држати његове уредбе и прописе, и слушати његов глас. 18Данас је Господ изјавио да си његов народ, његова драгоцена својина, као што ти је обећао, и да ћеш држати све његове заповеди. 19Он ће те узвисити чашћу, именом и славом над свим народима које је створио; ти ћеш бити народ посвећен Господу, Богу своме, како је обећао.“