Deuteronomo 23 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 23:1-25

Wosayenera mu Msonkhano

1Mwamuna aliyense wofulidwa kapena woduka chiwalo chachimuna asalowe nawo mu msonkhano wa Yehova.

2Aliyense wobadwa mʼbanja losavomerezeka, kapena mdzukulu wake wina aliyense, ngakhale mibado khumi pambuyo pake, asalowe mu msonkhano wa Yehova.

3Mwamoni kapena Mmowabu asalowe mu msonkhano wa anthu a Yehova ngakhale mibado khumi yobwera pambuyo pake. 4Pakuti iwowa sanabwere kudzakulonjerani ndi chakudya kapena madzi pamene mumadutsa pochokera ku Igupto, mʼmalo mwake anakalemba ganyu Balaamu mwana wa Beori wochokera ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni. 5Komabe Yehova Mulungu wanu sanamvere Balaamu koma anatembenuza temberero kukhala dalitso kwa inu chifukwa Yehova Mulungu wanu amakukondani. 6Musachite nawo mgwirizano uliwonse wa mtendere pa moyo wanu wonse.

7Musapeputse Mwedomu pakuti ndi mʼbale wanu ndithu. Musapeputse Mwigupto chifukwa munali alendo mʼdziko lake. 8Mʼbado wachitatu wa ana awo akhoza kulowa mu msonkhano wa anthu a Yehova.

Masamalidwe a Msasa

9Mukamakhala pa msasa pokonzekera adani anu, musayandikane ndi china chilichonse chodetsedwa. 10Wina mwa asilikali anu akadziwonongera ndi umuna usiku, ayenera kuchoka pa msasapo ndipo akhale kunja kwa msasa. 11Koma dzuwa likapendeka ayenera kusamba ndipo polowa dzuwa akhoza kubwerera ku msasa.

12Mukonze malo kunja kwa msasa kumene mukhoza kukadzithandizirako. 13Pakati pa zida zanu muzikhala ndi china chokumbira, ndipo pokadzithandiza muzikumba kadzenje ndi kukwirira chimbudzi chanu. 14Pakuti Yehova Mulungu wanu amayendayenda ku msasa wanu kukutchinjirizani ndi kupereka adani anu kwa inu. Nʼchifukwa chake msasa wanu uzikhala wopatulika kuti mwina angaone china chonyansa nabwerera osakuyandikirani.

Malamulo Osiyanasiyana

15Ngati kapolo wathawa mbuye wake nakabisala kwanu, musamuperekenso kwa mbuye wakeyo. 16Mumulole akhale pakati panu, paliponse pamene angakonde, mʼmudzi umene angasankhe ndipo musamupondereze.

17Pasapezeke Mwisraeli wamwamuna kapena wamkazi wochita chiwerewere ku Nyumba ya Mulungu. 18Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi.

19Musamalipitse mʼbale wanu chiwongoladzanja, kaya pa ndalama, kapena pa chakudya, kapena pa china chilichonse choti nʼkupereketsa chiwongoladzanja. 20Mlendo mukhoza kumulipitsa chiwongoladzanja koma osati mʼbale wanu Mwisraeli, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochitika zanu zonse mʼdziko mukulowamoli.

21Mukalumbira kupereka kanthu kwa Yehova Mulungu wanu, musamachedwetse kupereka, chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakufunsanibe kanthuko ndipo mudzapezeka wochimwa. 22Koma ngati mupewa kupanga mapangano simudzapezeka ochimwa. 23Zilizonse zimene mulumbira ndi pakamwa panu muzitsimikiza kuzichita, chifukwa mwalumbira mwaufulu pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi pakamwa panu.

24Mukalowa mʼmunda wamphesa wa mnzanu mukhoza kudya mphesa mmene mungafunire koma musayike zina mʼdengu mwanu. 25Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mʼbale wanu, mukhoza kutengako ngala mʼmanja mwanu, koma osasenga tirigu ndi chikwakwa.

New International Version

Deuteronomy 23:1-25

Exclusion From the Assembly

In Hebrew texts 23:1-25 is numbered 23:2-26. 1No one who has been emasculated by crushing or cutting may enter the assembly of the Lord.

2No one born of a forbidden marriage23:2 Or one of illegitimate birth nor any of their descendants may enter the assembly of the Lord, not even in the tenth generation.

3No Ammonite or Moabite or any of their descendants may enter the assembly of the Lord, not even in the tenth generation. 4For they did not come to meet you with bread and water on your way when you came out of Egypt, and they hired Balaam son of Beor from Pethor in Aram Naharaim23:4 That is, Northwest Mesopotamia to pronounce a curse on you. 5However, the Lord your God would not listen to Balaam but turned the curse into a blessing for you, because the Lord your God loves you. 6Do not seek a treaty of friendship with them as long as you live.

7Do not despise an Edomite, for the Edomites are related to you. Do not despise an Egyptian, because you resided as foreigners in their country. 8The third generation of children born to them may enter the assembly of the Lord.

Uncleanness in the Camp

9When you are encamped against your enemies, keep away from everything impure. 10If one of your men is unclean because of a nocturnal emission, he is to go outside the camp and stay there. 11But as evening approaches he is to wash himself, and at sunset he may return to the camp.

12Designate a place outside the camp where you can go to relieve yourself. 13As part of your equipment have something to dig with, and when you relieve yourself, dig a hole and cover up your excrement. 14For the Lord your God moves about in your camp to protect you and to deliver your enemies to you. Your camp must be holy, so that he will not see among you anything indecent and turn away from you.

Miscellaneous Laws

15If a slave has taken refuge with you, do not hand them over to their master. 16Let them live among you wherever they like and in whatever town they choose. Do not oppress them.

17No Israelite man or woman is to become a shrine prostitute. 18You must not bring the earnings of a female prostitute or of a male prostitute23:18 Hebrew of a dog into the house of the Lord your God to pay any vow, because the Lord your God detests them both.

19Do not charge a fellow Israelite interest, whether on money or food or anything else that may earn interest. 20You may charge a foreigner interest, but not a fellow Israelite, so that the Lord your God may bless you in everything you put your hand to in the land you are entering to possess.

21If you make a vow to the Lord your God, do not be slow to pay it, for the Lord your God will certainly demand it of you and you will be guilty of sin. 22But if you refrain from making a vow, you will not be guilty. 23Whatever your lips utter you must be sure to do, because you made your vow freely to the Lord your God with your own mouth.

24If you enter your neighbor’s vineyard, you may eat all the grapes you want, but do not put any in your basket. 25If you enter your neighbor’s grainfield, you may pick kernels with your hands, but you must not put a sickle to their standing grain.