Deuteronomo 23 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 23:1-25

Wosayenera mu Msonkhano

1Mwamuna aliyense wofulidwa kapena woduka chiwalo chachimuna asalowe nawo mu msonkhano wa Yehova.

2Aliyense wobadwa mʼbanja losavomerezeka, kapena mdzukulu wake wina aliyense, ngakhale mibado khumi pambuyo pake, asalowe mu msonkhano wa Yehova.

3Mwamoni kapena Mmowabu asalowe mu msonkhano wa anthu a Yehova ngakhale mibado khumi yobwera pambuyo pake. 4Pakuti iwowa sanabwere kudzakulonjerani ndi chakudya kapena madzi pamene mumadutsa pochokera ku Igupto, mʼmalo mwake anakalemba ganyu Balaamu mwana wa Beori wochokera ku Petori ku Mesopotamiya kuti akutemberereni. 5Komabe Yehova Mulungu wanu sanamvere Balaamu koma anatembenuza temberero kukhala dalitso kwa inu chifukwa Yehova Mulungu wanu amakukondani. 6Musachite nawo mgwirizano uliwonse wa mtendere pa moyo wanu wonse.

7Musapeputse Mwedomu pakuti ndi mʼbale wanu ndithu. Musapeputse Mwigupto chifukwa munali alendo mʼdziko lake. 8Mʼbado wachitatu wa ana awo akhoza kulowa mu msonkhano wa anthu a Yehova.

Masamalidwe a Msasa

9Mukamakhala pa msasa pokonzekera adani anu, musayandikane ndi china chilichonse chodetsedwa. 10Wina mwa asilikali anu akadziwonongera ndi umuna usiku, ayenera kuchoka pa msasapo ndipo akhale kunja kwa msasa. 11Koma dzuwa likapendeka ayenera kusamba ndipo polowa dzuwa akhoza kubwerera ku msasa.

12Mukonze malo kunja kwa msasa kumene mukhoza kukadzithandizirako. 13Pakati pa zida zanu muzikhala ndi china chokumbira, ndipo pokadzithandiza muzikumba kadzenje ndi kukwirira chimbudzi chanu. 14Pakuti Yehova Mulungu wanu amayendayenda ku msasa wanu kukutchinjirizani ndi kupereka adani anu kwa inu. Nʼchifukwa chake msasa wanu uzikhala wopatulika kuti mwina angaone china chonyansa nabwerera osakuyandikirani.

Malamulo Osiyanasiyana

15Ngati kapolo wathawa mbuye wake nakabisala kwanu, musamuperekenso kwa mbuye wakeyo. 16Mumulole akhale pakati panu, paliponse pamene angakonde, mʼmudzi umene angasankhe ndipo musamupondereze.

17Pasapezeke Mwisraeli wamwamuna kapena wamkazi wochita chiwerewere ku Nyumba ya Mulungu. 18Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi.

19Musamalipitse mʼbale wanu chiwongoladzanja, kaya pa ndalama, kapena pa chakudya, kapena pa china chilichonse choti nʼkupereketsa chiwongoladzanja. 20Mlendo mukhoza kumulipitsa chiwongoladzanja koma osati mʼbale wanu Mwisraeli, kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa zochitika zanu zonse mʼdziko mukulowamoli.

21Mukalumbira kupereka kanthu kwa Yehova Mulungu wanu, musamachedwetse kupereka, chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakufunsanibe kanthuko ndipo mudzapezeka wochimwa. 22Koma ngati mupewa kupanga mapangano simudzapezeka ochimwa. 23Zilizonse zimene mulumbira ndi pakamwa panu muzitsimikiza kuzichita, chifukwa mwalumbira mwaufulu pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi pakamwa panu.

24Mukalowa mʼmunda wamphesa wa mnzanu mukhoza kudya mphesa mmene mungafunire koma musayike zina mʼdengu mwanu. 25Mukalowa mʼmunda wa tirigu wa mʼbale wanu, mukhoza kutengako ngala mʼmanja mwanu, koma osasenga tirigu ndi chikwakwa.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 23:1-25

Who Can Join in Worship With the Lord’s People?

1No man whose sex organs have been crushed or cut can join in worship with the Lord’s people.

2No one born to an unmarried woman can join in worship with the Lord’s people. That also applies to the person’s children for all time to come.

3The people of Ammon and Moab can’t join in worship with the Lord’s people. That also applies to their children after them for all time to come. 4The Ammonites and Moabites didn’t come to meet you with food and water on your way out of Egypt. They even hired Balaam from Pethor in Aram Naharaim to put a curse on you. Balaam was the son of Beor. 5The Lord your God wouldn’t listen to Balaam. Instead, he turned the curse into a blessing for you. He did it because he loves you. 6So don’t make a peace treaty with the Ammonites and Moabites as long as you live.

7Don’t hate the people of Edom. They are your relatives. Don’t hate the people of Egypt. After all, you lived as outsiders in their country. 8The great-grandchildren of the Edomites and Egyptians can join in worship with the Lord’s people.

Keep the Camp of the Soldiers Pure and “Clean”

9There will be times when you are at war with your enemies. And your soldiers will be in camp. Then keep away from anything that isn’t pure and “clean.” 10Suppose semen flows from the body of one of your soldiers during the night. Then that will make him “unclean.” He must go outside the camp and stay there. 11But as evening approaches, he must wash himself. When the sun goes down, he can return to the camp.

12Choose a place outside the camp where you can go to the toilet. 13Keep a shovel among your tools. When you go to the toilet, dig a hole. Then cover up your waste. 14The Lord your God walks around in your camp. He’s there to keep you safe. He’s also there to hand your enemies over to you. So your camp must be holy. Then he won’t see anything among you that is shameful. He won’t turn away from you.

Several Other Laws

15If a slave comes to you for safety, don’t hand them over to their master. 16Let them live among you anywhere they want to. Let them live in any town they choose. Don’t treat them badly.

17A man or woman in Israel must not become a temple prostitute. 18The Lord your God hates the money that men and women get for being prostitutes. So don’t take that money into the house of the Lord to pay what you promised to give.

19Don’t charge your own people any interest. Don’t charge them when they borrow money, food or anything else. 20You can charge interest to people from another country. But don’t charge your own people. Then the Lord your God will bless you in everything you do. He will bless you in the land you are entering to take as your own.

21Don’t put off giving to the Lord your God everything you promise him. He will certainly require it from you. And you will be guilty of committing a sin. 22But if you don’t make a promise, you won’t be guilty. 23Make sure you do what you promised to do. With your own mouth you made the promise to the Lord your God. No one forced you to do it.

24When you enter your neighbor’s vineyard, you can eat all the grapes you want. But don’t put any of them in your basket. 25When you enter your neighbor’s field, you can pick heads of grain. But don’t cut down their standing grain.