Deuteronomo 22 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 22:1-30

1Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye. 2Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere. 3Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.

4Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.

5Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.

6Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe. 7Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.

8Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.

9Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.

10Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.

11Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.

12Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.

Malamulo a Ukwati

13Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso 14namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,” 15zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata. 16Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso. 17Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja, 18ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango. 19Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.

20Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke, 21iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.

22Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.

23Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye, 24muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

25Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa. 26Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye, 27pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.

28Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka, 29ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.

30Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.

New Russian Translation

Второзаконие 22:1-30

1Если увидишь, что вол или овца другого человека заблудились, не оставляй их, но отведи к хозяину. 2Если владелец не живет поблизости или ты не знаешь, кому они принадлежат, то отведи их к себе домой, и пусть они будут у тебя до тех пор, пока за ними не придет хозяин, и тогда ты должен возвратить их ему. 3Поступай так же, если найдешь чужого осла или одежду, или любую вещь, потерянную кем-то. Не уклоняйся от этого.

4Если осел или вол другого человека упадет на дороге, не оставляй их. Помоги ему поднять их на ноги. 5Женщина не должна надевать мужскую одежду, и мужчина не должен надевать женскую одежду, потому что Господу, твоему Богу, отвратителен любой, кто делает подобные вещи.

6Если в дороге тебе попадется птичье гнездо на каком-либо дереве или на земле, и если птица-мать сидит там со своими птенцами или на яйцах, то не забирай мать вместе с птенцами. 7Ты можешь взять себе птенцов, но мать отпусти. Если ты поступишь так, то тебе будет хорошо и ты проживешь долгую жизнь. 8Строя новый дом, сделай по краю крыши ограждение22:8 В древнем Израиле крыши домов были плоские и использовались и для работы, и для отдыха, поэтому, чтобы предотвратить случайное падение человека с крыши, вдоль края крыши сооружались перила., и тогда ты не будешь виновен в смерти, если кто-нибудь упадет с крыши.

9Не засевай свой виноградник еще какими-либо семенами, иначе ты осквернишь не только плоды посеянного семени, но и плоды виноградника. 10Не паши одновременно и на воле, и на осле. 11Не надевай одежду, сделанную из шерсти и льна вместе. 12Сделай кисточки22:12 Кисточки по углам верхней одежды служили постоянным напоминанием хозяину о законах Господа (см. Чис. 15:38-39). на четырех углах одеяния, которое ты носишь.

Законы о браке

13Если мужчина женится на девушке, но, переспав с ней, возненавидит ее, 14а затем будет клеветать и распространять сплетни о ней, говоря: «Я женился на этой женщине и был с ней, но она оказалась не девственницей», 15то тогда пусть отец и мать девушки вынесут старейшинам города к городским воротам доказательства того, что она была девственницей. 16И пусть отец девушки скажет старейшинам: «Я отдал свою дочь в жены этому человеку, а теперь он возненавидел ее. 17Этот человек оболгал мою дочь, сказав: „Я не нашел доказательства того, что твоя дочь девственница“. Так вот доказательство того, что моя дочь была девственницей». Затем пусть ее родители покажут простыню старейшинам города. 18И тогда старейшины города должны наказать клеветника22:18 Букв.: «его».. 19Пусть они наложат на него пеню в сто шекелей серебра22:19 Около 1200 г. серебра. и отдадут отцу девушки за то, что он пустил дурной слух о девственнице Израиля, и пусть она останется его женой, и он всю жизнь не сможет развестись с ней. 20Но если то, что муж сказал о жене, – правда, и у родителей нет доказательств ее девственности, 21то пусть девушку приведут к воротам отцовского дома, и там жители города пусть забьют ее камнями до смерти, потому что она совершила позорный поступок в Израиле: она распутствовала в доме своего отца. Ты должен искоренить зло из среды Израиля.

22Если выяснится, что мужчина спал с чужой женой, то они оба должны умереть. Ты должен искоренить зло из среды Израиля.

23Если мужчина встретит девушку, обрученную с другим, и переспит с ней, и это случится в городе, 24то приведите их обоих к городским воротам и забейте их камнями до смерти: убейте девушку за то, что она не позвала на помощь, хотя и была в городе, а мужчину убейте за то, что он согрешил с женой другого. Ты должен искоренить зло среди своих людей. 25Если же мужчина встретит в поле девушку, обрученную с другим, и обесчестит ее, то только мужчина должен быть предан смерти. 26С девушкой ничего не делайте, потому что она не сделала ничего, что заслуживало бы смерти. Это то же, как если бы человек напал на другого и убил его. 27Ведь он встретил девушку, обрученную с другим в поле и напал на нее, и она, может быть, и кричала, но некому было ей помочь.

28Если мужчина встретит девственницу, не обрученную с другим, и обесчестит ее, и если люди видели случившееся, 29то пусть он уплатит отцу девушки пятьдесят шекелей серебра22:29 Около 600 г. серебра., и пусть девушка станет его женой, потому что он опорочил ее. Всю свою жизнь он не сможет развестись с ней. 30Никто не должен спать с женой своего отца, потому что этим позорит его22:30 Букв.: «потому что открывает край одежды отца своего»..