Deuteronomo 22 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 22:1-30

1Ngati uwona ngʼombe kapena nkhosa ya mʼbale wako ikusochera, usayilekerere koma uyesetse kuyibwezera kwa iye. 2Ngati mʼbale wakoyo sakhala pafupi kapena sukudziwa kuti ndi yandani, uyitengere ku nyumba kwako ndi kuyisamala mpaka mwini wake atayilondola ndipo umubwezere. 3Uzitero ndithu ngati upeza bulu kapena mkanjo kapena chilichonse chimene chatayika. Osachilekerera.

4Ngati wapeza bulu kapena ngʼombe ya mʼbale wako itagwa panjira, usayilekerere. Ithandize kuti idzuke.

5Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi.

6Ukapeza chisa cha mbalame mʼmphepete mwa msewu, kaya ndi mu mtengo kapena pansi, mbalame yayikazi itafungatira ana kapena mazira, usatenge mbalameyo pamodzi ndi ana ake omwe. 7Anawo mukhoza kutenga koma onetsetsani kuti mayi wawo mwamutaya kuti apite, kuti zinthu zizikuyenderani bwino ndiponso kuti mukhale ndi moyo wautali.

8Mukamanga nyumba yatsopano, mutchingire khonde lake la pa denga kuti inu musapezeke ndi mlandu wopha munthu ngati wina agwa kuchokera pa khonde la pa dengalo.

9Musadzale mbewu zamitundu iwiri mʼmunda wanu wa mpesa, ngati mutero, si mbewu zanu zokha zimene zidzakhale zodetsedwa, komanso zipatso za mʼmunda wamphesawo.

10Musatipule pogwiritsa ntchito ngʼombe ndi bulu pa goli limodzi.

11Musamavale chovala chopangidwa mophatikiza ubweya ndi thonje.

12Muzipanga mphonje mʼngodya za mkanjo umene mumavala.

Malamulo a Ukwati

13Ngati munthu akwatira mkazi, ndipo atagona naye nʼkusamufunanso 14namunyoza ndi kumuyipitsira dzina nʼkumati, “Ine ndinakwatira mkazi uyu, koma pamene ndinakhala naye, sindinachione chizindikiro cha unamwali wake,” 15zikatero abambo ndi amayi ake ayenera kubweretsa chitsimikizo chakuti anali namwali kwa akuluakulu a mzinda ku chipata. 16Abambo ake a mtsikanayo adzanene kwa akuluakuluwo kuti, “Ine ndinamupatsa munthu uyu mwana wanga wamkazi kuti amukwatire, koma sakumufunanso. 17Tsopano wamunyoza ndipo wanena kuti, ‘Ine sindinapeze kuti mwana wanu wamkaziyu ndi namwali.’ Koma tsopano onani chitsimikizo ichi cha unamwali wa mwana wanga wamkazi.” Kenaka makolo a mtsikanayo adzaonetse kansalu kwa akuluakulu aja, 18ndipo akuluakuluwo adzamugwire munthuyo namupatsa chilango. 19Iwo adzamulipitse ndalama zasiliva zokwana 100 nazipereka kwa abambo a mtsikana, chifukwa munthu uyu wayipitsa dzina la mtsikana wa Chiisraeli. Ayenera kukhalabe mkazi wake ndipo asadzamuleke moyo wake wonse.

20Koma ngati zomunenerazo ndi zoona, ndipo kuti chitsimikizo cha unamwali wa mtsikanayo sichinapezeke, 21iyeyu ayenera kumutengera pa khomo pa abambo ake pamene anthu a mu mzinda wake akamuphere ndi miyala. Iyeyo wachita chinthu chochititsa manyazi mu Israeli pochita chiwerewere akanali pa khomo pa abambo ake. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu.

22Ngati munthu apezeka akugona ndi mkazi wa mwini wake, ayenera kuphedwa munthuyo pamodzi ndi mkazi yemwe wagona nayeyo. Muyenera kuchotsa zoyipa mu Israeli.

23Ngati munthu mu mzinda akumana ndi mkazi yemwe anachita kale chinkhoswe nagona naye, 24muwatengere awiriwo ku chipata cha mzinda ndi kuwapha ndi miyala. Aphedwe chifukwa mtsikanayo anali pafupi ndi anthu ndipo sanakuwe kuti ena amuthandize ndipo mwamunayo chifukwa anayipitsa mkazi wa mwini. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

25Koma ngati munthu akumana ndi mkazi kutchire yemwe anachita kale chinkhoswe namugwiririra, mwamuna yekhayo ndiye woyenera kuphedwa. 26Mtsikanayo musamuchite chilichonse, palibe tchimo limene wachita loti ayenera kuphedwa. Mlandu uwu ufanana ndi wa munthu amene alimbana ndi kupha mnzake woyandikana naye, 27pakuti mwamunayo anamupeza mtsikanayo kutchire, ndipo ngakhale mtsikana wachinkhosweyo anakuwa, panalibe anamulanditsa.

28Ngati munthu apezana ndi namwali woti sanachite chinkhoswe, namugwiririra, munthuyo nʼkupezeka, 29ayenera kuwalipira abambo ake a namwaliyo ndalama za siliva makumi asanu. Iye ayenera kumukwatira mkaziyo chifukwa wamuyipitsa, ndipo sadzamulekanso moyo wake wonse.

30Munthu asakwatire mkazi wa abambo ake pakuti ayenera kuchitira ulemu pogona pa abambo ake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 22:1-30

1Если увидишь, что вол или овца другого человека заблудились, не оставляй их, а отведи к хозяину. 2Если владелец живёт далеко, или ты не знаешь, кому они принадлежат, то отведи их к себе домой, и пусть они будут у тебя до тех пор, пока за ними не придёт хозяин. И тогда ты должен возвратить их ему. 3Поступай так же, если найдёшь чужого осла, или одежду, или любую вещь, потерянную кем-то. Не уклоняйся от оказания помощи.

4Если осёл или вол другого человека упадёт на дороге, то не оставляй их. Помоги ему поднять их на ноги.

5Женщина не должна надевать мужскую одежду, и мужчина не должен надевать женскую одежду, потому что Вечному, твоему Богу, отвратительны те, кто делает подобные вещи.

6Если в дороге тебе попадётся птичье гнездо на каком-нибудь дереве или на земле, и если птица-мать сидит в нём на яйцах или с птенцами, то не забирай мать вместе с птенцами. 7Ты можешь взять себе птенцов, но мать отпусти. Если ты поступишь так, то тебе будет хорошо и ты проживешь долгую жизнь.

8Строя новый дом, сделай по краю крыши ограждение22:8 В древнем Исроиле крыши домов были плоские, они использовались и для работы, и для отдыха., и тогда ты не будешь виновен в смерти, если кто-нибудь упадёт с крыши.

9Не засевай свой виноградник ещё какими-либо семенами, иначе ты осквернишь не только плоды посеянного семени, но и плоды виноградника.

10Не паши одновременно и на воле, и на осле.

11Не надевай одежду, сделанную из шерсти и льна вместе.

12Сделай кисточки на четырёх углах одеяния, которое ты носишь22:12 Кисточки по углам верхней одежды служили постоянным напоминанием хозяину о законах Всевышнего (см. Чис. 15:38-39)..

Законы о браке

13Если мужчина женится на девушке, но, переспав с ней, возненавидит её, 14а затем будет клеветать и распространять сплетни о ней, говоря: «Я женился на этой женщине и был с ней, но она оказалась не девственницей», 15то тогда пусть отец и мать девушки вынесут старейшинам города к городским воротам доказательства того, что она была девственницей. 16И пусть отец девушки скажет старейшинам: «Я отдал свою дочь в жёны этому человеку, а теперь он возненавидел её. 17Этот человек оболгал мою дочь, сказав: „Я не нашёл доказательств того, что твоя дочь девственница“. Так вот доказательство того, что моя дочь была девственницей». Затем пусть её родители покажут простыню старейшинам города. 18И тогда старейшины города должны наказать клеветника. 19Пусть они наложат на него пеню в один килограмм и двести граммов22:19 Букв.: «сто шекелей». серебра и отдадут их отцу девушки за то, что этот человек пустил дурной слух о девственнице Исроила, и пусть она останется его женой, и он уже всю жизнь не сможет развестись с ней.

20Но если то, что муж сказал о жене, – правда, и у родителей нет доказательств её девственности, 21то пусть девушку приведут к воротам отцовского дома, и там жители города пусть забьют её камнями до смерти, потому что она совершила позорный поступок в Исроиле: она распутствовала в доме своего отца. Ты должен искоренить зло из своей среды.

22Если выяснится, что мужчина спал с чужой женой, то они оба должны умереть. Ты должен искоренить зло из среды Исроила.

23Если мужчина встретит девушку, обручённую с другим, и переспит с ней, и всё это случится в городе, 24то приведи их обоих к городским воротам и забей их камнями до смерти: убейте девушку за то, что она не позвала на помощь, хотя и была в городе, и убейте мужчину за то, что он согрешил с невестой другого. Ты должен искоренить зло из своей среды.

25Если же мужчина встретит в поле девушку, обручённую с другим, и обесчестит её, то только мужчина должен быть предан смерти. 26С девушкой ничего не делайте, потому что она не сделала ничего, что заслуживало бы смерти. Это то же, как если бы человек напал на другого и убил его. 27Ведь он встретил девушку, обручённую с другим, в поле и напал на неё, и она, может быть, и кричала, но некому было ей помочь.

28Если мужчина встретит девственницу, не обручённую с другим, и обесчестит её, и если люди видели случившееся, 29то пусть он уплатит отцу девушки шестьсот граммов22:29 Букв.: «пятьдесят шекелей». серебра, и пусть девушка станет его женой, потому что он опорочил её. Всю свою жизнь он не сможет развестись с ней.

30Никто не должен спать с женой своего отца, потому что этим позорит его.