Deuteronomo 21 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 21:1-23

Nsembe Yopepesera Munthu Akaphedwa Mosadziwika Bwino

1Ngati munthu apezeka ataphedwa mʼmunda mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kukhala lanu koma inu osadziwa amene wamupha, 2akuluakulu anu ndi oweruza adzapite ndi kuyeza kutalikirana kuchokera pamene pali mtembowo ndi mizinda yoyandikira. 3Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzatenge ngʼombe imene sinagwirepo ntchito kapena kuvalapo goli 4ndi kuyikusira ku chigwa chimene sichinalimidwepo ndiponso kumene kuli mtsinje woyenda. Ku chigwa kumeneko ayenera kukayithyola khosi ngʼombeyo. 5Ansembe, ana a Aaroni, adzapite patsogolo pangʼono, popeza ndiwo amene Yehova Mulungu wanu anawasankha kuti azitumikira, kupereka mdalitso mʼdzina la Yehova ndi kugamula milandu yonse yamikangano ndi yovulazana. 6Kenaka akuluakulu a mzinda wapafupi kwambiri ndi mtembowo adzasamba mʼmanja pamwamba pa ngʼombe yothyoledwa khosi ija, 7nadzatsimikiza kuti, “Manja athu sanakhetse magazi awa ndipo sitinaonerere kuphedwako. 8Yehova, landirani nsembe yopepesa ya anthu anu Aisraeli amene munawapulumutsa, ndipo muwakhululukire tchimo la kupha munthu wosalakwa.” Mukatero ndiye kuti adzapezeka kuti ndi osalakwa. 9Kotero mudzadzichotsera nokha tchimo lokhetsa magazi wosalakwa, popeza mwachita zoyenera pamaso pa Yehova.

Kukwatira Mkazi Wogwidwa ku Nkhondo

10Mukapita kukachita nkhondo ndi adani anu, Yehova Mulungu wanu nawapereka adani anuwo mʼmanja mwanu muwagwira ukapolo, 11ndiye ngati muona mkazi wokongola pakati pa ogwidwawo nakutengani mtima, mukhoza kumutenga kuti akhale mkazi wanu. 12Mumutengere ku nyumba kwanu, kumumeta tsitsi lake, mumuwenge zikhadabo zake 13ndipo avulidwe zovala zimene anagwidwa nazo. Atakhala mʼnyumba mwanu nalira maliro a abambo ndi amayi ake kwa mwezi wathunthu, ndiye mukhoza kupita kwa iye ndi kukhala mwamuna wake ndipo iyeyo adzakhala mkazi wanu. 14Ngati simukukondweretsedwa naye, muloleni kuti apite kumene afuna. Musamugulitse kapena kumuzunza ngati kapolo, popeza mwamuchotsa ulemu.

Ufulu wa Mwana Woyamba Kubadwa

15Ngati munthu ali ndi akazi awiri, nakonda wina koposa mnzake, onsewa ndikubereka ana aamuna koma woyamba nakhala mwana wa mkazi amene samukondayo, 16akamagawa chuma chake akanali moyo kwa ana akewo, asapereke ufulu wa mwana woyamba kubadwa kwa mwana wamwamuna wa mkazi amene amamukonda mʼmalo mwa mwana wake woyamba kubadwa weniweni amene ndi mwana wamkazi amene samukonda. 17Iye ayenera kuonetsa kuti mwana wake wamwamuna wa mkazi wosakondedwayo ndiye woyamba kubadwa pomupatsa miyeso iwiri ya zonse zimene ali nazo. Mwana wamwamuna ameneyo ndiye chizindikiro cha mphamvu za abambo ake. Ufulu wokhala mwana wamwamuna woyamba ndi wake.

Mwana Wamwamuna Wowukira

18Ngati munthu ali ndi mwana wamwamuna wosamvera ndi wowukira amene samvera a abambo ake ndi amayi ake akamuweruza, 19abambo ndi amayi ake amugwire ndi kupita naye kwa akuluakulu ku chipata cha mzinda wake ndipo 20akawawuze akuluakuluwo kuti, “Mwana wathu wamwamunayu ndi wosamva ndi wowukira. Iyeyu satimvera. Ndi mwana wadyera komanso ndi chidakwa.” 21Pamenepo anthu onse a mu mzinda wake adzamuphe ndi miyala. Muyenera kuchotsa zoyipa pakati panu. Aisraeli onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha.

Malamulo Osiyanasiyana

22Ngati munthu wopezeka ndi mlandu wopha mnzake waphedwa ndipo mtembo wake wapachikidwa pamtengo, 23musasiye mtembowo pa mtengopo usiku wonse. Muonetsetse kuti mwakawukwirira tsiku lomwelo, chifukwa aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu. Musayipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani ngati cholowa chanu.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 21:1-23

Кад се не зна ко је убица

1Ако се у земљи коју ти Господ, Бог твој, даје у посед, нађе тело усмрћеног човека да лежи у пољу, а не зна се ко га је убио, 2нека изађу старешине и судије, па нека измере удаљеност од убијеног до околних градова. 3Онда нека старешине града, који је најближи убијеном, узму јуницу која још није радила, то јест, која није вукла под јармом. 4Затим старешине тог града нека сведу јуницу у неки непресушни поток, у долину која се не обрађује нити сеје. Нека тамо код потока сломе врат јуници. 5Тада нека приступе свештеници, Левити, јер је њих изабрао Господ, Бог твој, да служе и да благосиљају у име Господње; они ће разрешавати сваки спор и насиље. 6Потом старешине града који буде најближи убијеном, нека оперу руке у потоку над јуницом којој је сломљен врат, 7и изјаве: ’Наше руке нису пролиле ову крв, нити смо својим очима ишта видели. 8Зато опрости своме народу Израиљу, који си откупио, Господе, и не сваљуј кривицу за недужну крв на свој народ.’ Тако ће им кривица за проливену крв бити опроштена. 9Ти ћеш уклонити проливање недужне крви из своје средине, ако будеш чинио што је право у Господњим очима.

Понашање према заробљеницима

10Кад пођеш у рат против својих непријатеља и Господ, Бог твој, их преда у твоје руке, те их заробиш, 11па међу заробљеницима видиш лепу жену, заљубиш се у њу и пожелиш да је узмеш себи за жену, 12доведи је у своју кућу. Онда нека се ошиша до главе, подреже нокте 13и баци одећу у којој је била заробљена, па нека проведе месец дана у твојој кући оплакујући свога оца и своју мајку. Након тога можеш да јој приступиш као муж, па нека ти буде жена. 14А ако ти не буде по вољи, пусти је да иде где год хоће. Не смеш је продати за новац, нити поступати с њом као са робињом, зато што си је понизио.

Право првородства

15Ако неки човек има две жене: једну коју воли, а другу коју не воли, па му и она што је воли и она што је не воли роде синове, али првенац буде син невољене – 16кад дође дан да подели своју имовину у наследство својим синовима – он не сме доделити право првородства сину вољене на штету сина невољене, који му је прави првенац. 17Наиме, он мора да призна сина невољене за првенца и да му да двоструки део своје имовине, зато што је он првенац његове снаге – њему припада право првородства.

Непослушни син

18Ако неко има сина који је тврдоглав и бунтован, који не слуша свог оца и мајку, чак ни када га опомињу, 19нека га његов отац и мајка одведу пред градске старешине, код врата свога места. 20Онда нека кажу градским старешинама: ’Ово је наш тврдоглави и бунтовни син који неће да нас слуша. Изјелица је и пијаница.’ 21Затим нека га сви људи у граду заспу камењем да умре. Тако ћеш искоренити ово зло из своје средине. Цели Израиљ ће чути за ово, па ће се бојати.

Различити закони

22Ако неко учини грех који заслужује смртну казну и буде погубљен вешањем о дрво, 23његово тело не сме остати да виси преко ноћи. Он мора да буде сахрањен истог дана, јер је проклет пред Богом свако ко је обешен о дрво. Тако нећеш оскрнавити земљу коју ти Господ, Бог твој, даје у наследство.