Deuteronomo 2 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 2:1-37

Kuyendayenda Mʼchipululu

1Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.

2Ndipo Yehova anati kwa ine, 3“Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto. 4Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri. 5Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake. 6Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’ ”

7Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.

8Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.

9Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”

10(Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko. 11Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi. 12Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).

13Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.

14Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira. 15Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.

16Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo, 17Yehova anati kwa ine, 18“Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari. 19Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”

20(Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi. 21Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo. 22Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero. 23Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).

Kugonjetsedwa kwa Sihoni Mfumu ya ku Hesiboni

24“Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo. 25Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”

26Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati, 27“Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere. 28Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi 29monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.” 30Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.

31Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”

32Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi, 33Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo. 34Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka. 35Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu. 36Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo. 37Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.

New Serbian Translation

5. Мојсијева 2:1-37

Лутање у пустињи

1Окренули смо се и запутили у пустињу према Црвеном мору како нам је рекао Господ. Дуго времена смо се вртели око горе Сир.

2Тада ми је Господ рекао: 3’Доста сте се вртели око ове горе. Окрените се према северу! 4Заповеди народу: „Сада пролазите кроз подручје ваше браће, Исавових потомака, који живе у Сиру. Они вас се боје, али се ви добро чувајте! 5Не упуштајте се у сукоб са њима, јер вам нећу дати ни стопу од њихове земље. Наиме, Сир сам дао Исаву у посед. 6Храну од њих купујте за новац, да имате шта да једете, а такође и воду плаћајте новцем.“’

7Јер, Господ, Бог твој, који те је благословио у свим твојим подухватима, зна да пролазиш кроз ову велику пустињу. Господ, Бог твој, ових је четрдесет година био с тобом, те ти ништа није недостајало.

8Тако смо заобишли своју браћу, потомке Исавове, који живе у Сиру, путем што води у Араву, Елат и Есион-Гевер, па смо скренули на пут што води у моавску пустињу.

9Господ ми рече: ’Не нападај Моавце, нити ступај у рат с њима, јер ти нећу дати у посед њихову земљу: Лотовим потомцима сам дао Ар у посед.’ 10(Тамо су некада живели Емијци. Био је то народ велики и бројан; високи као Енаковци. 11Њих, као и Енаковце, такође сврставају у Рефаимце, иако их Моавци зову Емијцима. 12У Сиру су некада живели Хоријци. Исавови потомци су присвојили њихову земљу, истребили их и населили се на њихово место. То исто је учинио Израиљ у земљи коју му је Господ дао у посед.)

13’А сад устаните и пређите преко потока Зареда.’ Тако смо прешли преко потока Зареда.

14Путовали смо тридесет осам година од Кадис-Варније до преласка потока Зареда, све док није помро читав тај нараштај људи у табору способних за ратовање, као што им се Господ заклео. 15Шта више, Господња рука се окренула против њих да их смете усред табора, док сви нису били истребљени.

16А када су помрли у народу сви људи способни за ратовање, 17Господ ми рече: 18’Данас прелазиш преко моавског подручја код Ара. 19Кад се приближиш Амонцима, не нападај их, нити се упуштај у сукоб са њима, јер ти нећу дати у посед земљу Амонаца. Наиме, њу сам је дао у посед Лотовим потомцима.’ 20(Та земља је некада припадала Рефаимцима, које су Амонци звали и ’Замзумићанима’. 21То је био народ велики и бројан; били су високог раста као Енаковци. Господ их је истребио пред Амонцима који су присвојили њихову земљу и населили се на њихово место. 22То су исто учинили и потомци Исава који живе у Сиру. Они су истребили Хоријце, присвојили њихову земљу и настанили се на њихово место где живе све до данас. 23А Авинце, који су живели у селима око Газе, истребили су Кафтореји, који долазе из Кафтора, и населили се на њихово место.)

Пораз Сихона, цара есевонског

24’Устаните и наставите пут, па пређите преко потока Арнона! Ево, предао сам вам у руке Сихона, цара есевонског, Аморејца, и његову земљу. Почни да је освајаш! Ступи у рат против њега! 25Данас почињем да пред тобом ширим страх и трепет међу народе под целим небом. Они ће чути гласине о теби, па ће дрхтати од страха пред тобом и спопадаће га ужас од тебе.’

26Тада сам из пустиње Кедемот послао гласнике есевонском цару Сихону с мирољубивом поруком: 27’Дозволи ми да прођем преко твоје земље. Ићи ћу главним путем и нећу скретати ни десно ни лево. 28Храну за јело и воду за пиће продај ми за новац. Само ми дозволи да прођем пешице, 29док не пређем преко Јордана у земљу коју нам даје Господ, Бог наш. Тако су ми учинили и Исавови потомци који живе у Сиру и Моавци који живе у Ару.’ 30Али Сихон, цар есевонски, није нам дао да прођемо, јер је Господ, Бог твој, учинио његов дух непопустљивим а његово срце тврдим, како би га предао у твоје руке, као што и јесте данас.

31Господ ми рече: ’Ево, почео сам да ти предајем Сихона и његову земљу. Почни да освајаш његову земљу, како би је присвојио!’

32Тада је Сихон изашао пред нас, он и сав његов народ у бој код Јасе. 33Али, Господ, Бог наш, нам га је предао, тако да смо поразили њега, његове синове и његов народ. 34У то време смо заузели све његове градове и извршили клето уништење над сваким градом – над мушкарцима, женама и децом – никог живог нисмо оставили. 35Запленили смо само стоку и однели плен из градова које смо освојили. 36Од Ароира, који се налази код потока Арнона и града који је код потока, све до Галада, није било града који је био превисок за нас. Све нам их је предао Господ, Бог наш. 37Само се земљи Амонаца ниси приближавао: потоку Јавоку, нити градовима у горју, баш како је заповедио Господ, Бог наш.