Deuteronomo 2 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 2:1-37

Kuyendayenda Mʼchipululu

1Kenaka tinabwerera ndi kuyamba ulendo wolowera ku chipululu motsatira njira ya ku Nyanja Yofiira, monga mmene Yehova anatilamulira. Kwa nthawi yayitali tinayendayenda cha ku dziko la mapiri la Seiri.

2Ndipo Yehova anati kwa ine, 3“Mwazungulira mokwanira dziko la mapiri, tsopano tembenukirani kumpoto. 4Apatse anthu malamulo awa: ‘Muli pafupi kudutsa mʼchigawo cha abale anu adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Iwowa adzachita nanu mantha koma musamale kwambiri. 5Musayambane nawo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo ngakhale poti mungoyika phazi. Ndamupatsa Esau dziko lamapiri la Seiri kuti likhale lakelake. 6Inu muyenera kuwalipira ndi siliva pa chakudya chimene mudye ndi madzi amene mumwe.’ ”

7Yehova Mulungu wanu wakudalitsani mʼntchito zonse za manja anu. Iye wakuyangʼanirani pa ulendo wanu wodutsa mʼchipululu chachikulu. Yehova Mulungu wanu wakhala nanu mʼzaka makumi anayi, ndipo simunasowe kalikonse.

8Choncho tinapitiriza ulendo modutsa abale athu, adzukulu a Esau okhala ku Seiri. Tinapatukira njira ya ku Araba imene imachokera ku Elati ndi Ezioni Geberi ndipo tinayenda njira ya ku chipululu cha Mowabu.

9Ndipo Yehova anati kwa ine, “Musawavutitse Amowabu kapena kuwaputa kuti muchite nawo nkhondo popeza sindidzakupatsani gawo lina lililonse la dziko lawo. Ndinapereka Ari kwa adzukulu a Loti ngati chuma chawo.”

10(Aemi, anthu amphamvu ndi ochuluka komanso ataliatali ngati Aanaki amakhala kumeneko. 11Ngati Aanaki, nawonso ankawayesa kuti anali Arefai, koma Amowabu ankawatcha iwo Aemi. 12Ahori amakhala ku Seiri koma adzukulu a Esau anawapirikitsa. Iwo anawononga Ahori pamaso pawo nawakhalira pamalo pawo monga Aisraeli anachitira mʼdziko limene Yehova anawapatsa ngati chuma chawo).

13Ndipo Yehova anati, “Tsopano nyamukani ndipo muwoloke Chigwa cha Zeredi.” Choncho tinawoloka chigwacho.

14Panapita zaka 38 kuchokera pa nthawi imene tinachoka ku Kadesi Barinea mpaka pamene tinawoloka Chigwa cha Zeredi. Pa nthawi imeneyi nʼkuti mʼbado wonse wa anthu ankhondowo utawonongeka ku msasa monga Yehova anawalumbirira. 15Dzanja la Yehova linatsutsana nawo mpaka wonse anathera ku msasa.

16Tsono atafa munthu wotsiriza mwa anthu ankhondowo, 17Yehova anati kwa ine, 18“Lero mudutsa malire a Mowabu ku Ari podzera ku Ari. 19Mukafika kwa Aamoni, musawavutitse kapena kuwaputa, popeza sindidzakupatsani gawo lililonse la dziko la Aamoni. Ine ndalipereka dzikoli ngati chuma kwa adzukulu a Loti.”

20(Ilinso ankaliyesa dziko la Arefai amene ankakhala kumeneko. Koma Aamoni ankawatcha iwo Azamuzumi. 21Iwo anali anthu amphamvu ndiponso ochuluka, ataliatali ngati Aanaki. Yehova anawawononga ndi kuwachotsa pamaso pa Aamoni, amene anawapirikitsa nawakhalira pa malo pawo. 22Yehova anachitanso chimodzimodzi ndi adzukulu a Esau omwe anakhazikika ku Seiri atawononga Ahori powachotsa pamaso pawo. Iwo anawapirikitsa Ahoriwo ndi kuwakhalira pamalo pawo mpaka lero. 23Ndipo za Aavi omwe ankakhala mʼmidzi yofika mpaka ku Gaza, anagonjetsedwa ndi Akafitori wochokera ku Akafitori nakhala pamalo pawo).

Kugonjetsedwa kwa Sihoni Mfumu ya ku Hesiboni

24“Tsopano nyamukani, muwoloke khwawa la Arinoni. Taona ndapereka mʼmanja mwako Sihoni Mwamori mfumu ya Hesiboni ndi dziko lake lonse. Yambapo kutenga chuma chake ndi kumenyana naye nkhondo. 25Lero lomwe lino ndidzayamba kuyika chiopsezo ndi mantha pa mitundu yonse pansi pa thambo kuti akuope. Iwowo adzamva zambiri yako ndipo adzanjenjemera ndi kuwawidwa mtima chifukwa cha iwe.”

26Ine ndinatuma amithenga kuchokera ku chipululu cha Kedemoti kupita kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni kukanena mawu ofuna mtendere ndipo ndinati, 27“Tiloleni tidutse mʼdziko mwanu. Ife tidzangodutsa ndi msewu waukulu, ndipo sitidzapatukira kumanja kapena kumanzere. 28Mutigulitse chakudya kuti tidye ndi madzi kuti timwe pa mtengo wa siliva. Mungotilola kuti tidutse, tikuyenda pansi 29monga mmene anatichitira adzukulu a Esau okhala ku Seiri ndi Amowabu okhala ku Ari mpaka titawoloka Yorodani kufika ku dziko limene Yehova Mulungu wathu akutipatsa.” 30Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanalole kuti tidutse. Popeza Yehova Mulungu wanu analimbitsa mzimu wake, nawumitsa mtima wake kuti amupereke mʼmanja mwanu monga wachitira lero lino.

31Yehova anati kwa ine, “Taona ndayamba kumupereka Sihoni ndi dziko lake kwa iwe. Tsopano yamba kugonjetsa ndi kulanda dziko lake.”

32Sihoni ndi ankhondo ake atabwera kudzakumana nafe mwankhondo pa Yahazi, 33Yehova Mulungu anamupereka iye kwa ife ndipo tinankantha, pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse lankhondo. 34Pa nthawi imeneyi tinamulanda mizinda yake yonse ndi kuyiwononga kwathunthu, amuna, akazi ndi ana. Palibe amene anapulumuka. 35Koma ziweto ndi zinthu zonse zimene tinalanda mʼmizinda imene tinagonjetsayo, tinazitenga kukhala zathu. 36Kuchokera ku Aroeri mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni ndi ku mzinda wa ku mtsinjeko mpaka kukafika ku Giliyadi, panalibe ndi mzinda ndi umodzi omwe umene unatikanika kuwugonjetsa. Yehova Mulungu wathu anatipatsa onsewo. 37Molingana ndi lamulo la Yehova Mulungu wathu, simunalowerere dziko lililonse la Aamoni, ngakhale dera lonse la ku mtsinje wa Yaboki kapena dera lozungulira dera la ku mizinda ya ku mapiri.

Священное Писание

Второзаконие 2:1-37

Скитания в пустыне

1Затем мы повернули назад и отправились в пустыню в сторону Тростникового моря, как указал мне Вечный. Долго мы кружили вокруг нагорий Сеира.

2Затем Вечный сказал мне: 3«Довольно вам кружить вокруг этих нагорий, теперь поверните к северу. 4Дай народу такое повеление: „Сейчас вы будете проходить через землю ваших братьев, потомков Есава, которые живут в Сеире. Они испугаются вас, но будьте очень осторожны. 5Не побуждайте их к войне, потому что Я не дам вам ни пяди их земли. Я дал Есаву нагорья Сеира в собственность. 6Вы должны заплатить им серебром за пищу, которую будете есть, и за воду, которую будете пить. 7Вечный, ваш Бог, благословил вас во всяком деле ваших рук. Он охранял вас в путешествии через эту огромную пустыню. Эти сорок лет Вечный, ваш Бог, был с вами, и вы ни в чём не нуждались“».

8Так мы прошли мимо наших братьев, потомков Есава, которые живут в Сеире. Мы повернули с дороги Иорданской долины, которая поднимается от Елата и Эцион-Гевера, и путешествовали по дороге пустыни Моава.

9Вечный сказал мне: «Не тревожь моавитян и не побуждай их к войне, потому что Я не дам тебе их земли. Я дал Ар2:9 Ар – моавитский город, представляющий здесь всю страну Моав (см. ст. 18). во владение потомкам Лута».

10(Прежде там жили емиты – сильный и многочисленный народ, высокие, как анакиты. 11Подобно анакитам, они считались рефаитами, но моавитяне называли их емитами. 12А в Сеире прежде жили хорреи, но потомки Есава прогнали их. Они истребили хорреев и поселились на их земле – сделали так же, как сделал Исраил в земле, которую Вечный отдал ему во владение.)

13Вечный сказал: «Теперь встаньте и пересеките долину Заред». И мы пересекли долину.

14Тридцать восемь лет прошло с тех пор, как мы покинули Кадеш-Барни, до того времени, как мы пересекли долину Заред. К тому времени в лагере уже не осталось никого из прежнего поколения воинов, как и клялся им Вечный. 15Рука Вечного была против них, пока Он полностью не искоренил их из лагеря.

16И вот когда последний из этих воинов умер, 17Вечный сказал мне: 18«Пройди сегодня мимо земли Моава, то есть мимо Ара. 19Когда ты приблизишься к аммонитянам, не тревожь их и не побуждай к войне, потому что от земли, принадлежащей аммонитянам, Я не дам тебе во владение ничего. Я дал её во владение потомкам Лута».

20(Она также считалась землёй рефаитов, которые прежде жили там, но аммонитяне называли их замзумитами. 21Они были сильным и многочисленным народом, высоким, как анакиты. Вечный истребил их перед аммонитянами, которые прогнали их и поселились на их земле. 22Вечный сделал то же самое для потомков Есава, которые жили в Сеире, когда истребил перед ними хорреев. Они прогнали их и поселились на их месте, где живут и сейчас. 23А что до аввитов, которые жили в селениях до самой Газы, то кафтореи, вышедшие с Крита2:23 Букв.: «Кафтора»., истребили их и поселились на их месте.)

Победа над царём Сигоном

(Чис. 21:21-30)

24Вечный сказал: «Отправляйтесь в путь и перейдите реку Арнон. Смотри, Исраил, Я отдал в твои руки аморрея Сигона, царя Хешбона, и его страну. Приступай к захвату и начинай воевать с ним. 25С этого самого дня Я стану распространять ужас и страх перед тобой на все народы под небом. Они услышат вести о тебе и испугаются и затрепещут от страха».

26Из пустыни Кедемот я послал вестников к Сигону, царю Хешбона, чтобы предложить мир, и сказал: 27«Позволь нам пройти через твою страну. Мы будем держаться главной дороги – не свернём ни вправо, ни влево. 28Продай нам за серебро пищу, чтобы есть, и воду, чтобы пить. Позволь нам только пройти, 29как позволили потомки Есава, которые живут в Сеире, и моавитяне, которые живут в Аре, – пока мы не перейдём через Иордан в землю, которую Вечный, наш Бог, отдаёт нам». 30Но Сигон, царь Хешбона, не позволил нам пройти. Ведь Вечный, ваш Бог, сделал его сердце упрямым, а дух упорным, чтобы отдать его в ваши руки, как и произошло.

31Вечный сказал мне: «Смотри, Я отдаю Сигона и его страну тебе. Теперь захвати его землю и завладей ею».

32Когда Сигон выступил нам навстречу со всем своим войском к Иахацу, 33Вечный, наш Бог, отдал его нам в руки, и мы поразили его вместе с его сыновьями и всем войском. 34В то время мы взяли все его города и полностью истребили народ – мужчин, женщин и детей. Мы не оставили в живых никого. 35Но скот и добычу из захваченных городов мы взяли себе. 36От города Ароера на берегу реки Арнон и от города, что в долине, до самого Галаада не было города, который оказался бы неприступным для нас. Вечный, наш Бог, отдал нам всё. 37Но по повелению Вечного, нашего Бога, мы не посягнули ни на землю аммонитян, ни на землю вдоль реки Иаббок, ни на ту, что вокруг городов в горах.