Deuteronomo 19 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 19:1-21

Mizinda Yothawirako

1Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo, 2mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu. 3Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.

4Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa. 5Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake. 6Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala. 7Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.

8Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera, 9chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera. 10Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.

11Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi, 12akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe. 13Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.

14Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

Mboni

15Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.

16Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu, 17anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo. 18Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake, 19ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu. 20Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu. 21Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

Persian Contemporary Bible

تثنيه 19:1-21

شهرهای پناهگاه

(اعداد 35‏:9‏-28؛ يوشع 20‏:1‏-9)

1هنگامی كه خداوند، خدايتان قومهایی را كه بايد سرزمينشان را بگيريد، نابود كند و شما در شهرها و خانه‌هايشان ساكن شويد، 2‏-3آنگاه بايد سه شهر به عنوان پناهگاه تعيين كنيد تا اگر كسی تصادفاً شخصی را بكشد، بتواند به آنجا فرار كرده، در امان باشد. كشورتان را به سه منطقه تقسيم كنيد به طوری كه هر كدام از اين سه شهر در يكی از آن سه منطقه واقع گردد. جاده‌هايی را كه به اين شهرها می‌روند خوب نگه داريد.

4اگر كسی تصادفاً مرتكب قتل شود می‌تواند به يكی از اين شهرها فرار كرده، در آنجا پناه گيرد. 5مثلاً اگر مردی با همسايهٔ خود برای بريدن هيزم به جنگل برود و سر تبر از دسته‌اش جدا شده، باعث قتل همسايه‌اش گردد، آن مرد می‌تواند به يكی از اين شهرها گريخته، در امان باشد. 6‏-7بدين ترتيب مدعی خون مقتول نمی‌تواند او را بكشد. اين شهرها بايد پراكنده باشند تا همه بتوانند به آن دسترسی داشته باشند و گرنه مدعی عصبانی، ممكن است قاتل بی‌گناه را بكشد.

8اگر خداوند طبق وعده‌ای كه به پدران شما داده است مرزهای سرزمينتان را وسيعتر كند و تمام سرزمينی را كه وعده داده است، به شما ببخشد 9(البته چنين كاری بستگی دارد به اينكه از كليهٔ فرمانهايی كه امروز به شما می‌دهم اطاعت نموده خداوند، خدايتان را دوست بداريد و دائماً در راه او گام برداريد) در اين صورت بايد سه شهر پناهگاه ديگر نيز داشته باشيد. 10چنين عمل كنيد تا در سرزمينی كه خداوند به شما می‌دهد اشخاص بی‌گناه كشته نشوند و خون كسی به گردن شما نباشد.

11ولی اگر كسی از همسايهٔ خود نفرت داشته باشد و با قصد قبلی او را بكشد و سپس به يكی از شهرهای پناهگاه فرار نمايد، 12آنگاه ريش‌سفيدان شهر بايد دنبال او فرستاده، او را بازگردانند و تحويل مدعی خون مقتول بدهند تا او را بكشد. 13به او رحم نكنيد! اسرائيل را از خون بی‌گناه پاک كنيد تا در همهٔ كارهايتان كامياب باشيد.

مرزهای ملک همسايه

14هنگامی كه وارد سرزمينی شديد كه خداوند، خدايتان به شما می‌دهد، مواظب باشيد مرزهای ملک همسايه‌تان را كه از قديم تعيين شده است به نفع خود تغيير ندهيد.

شهادت در دادگاه

15هرگز كسی را بر اساس شهادت يک نفر محكوم نكنيد. حداقل دو يا سه شاهد بايد وجود داشته باشند. 16اگر كسی شهادت دروغ بدهد و ادعا كند كه شخصی را هنگام ارتكاب جرمی ديده است، 17هر دو نفر بايد به نزد كاهنان و قضاتی كه در آن موقع در حضور خداوند مشغول خدمتند، آورده شوند. 18قضات بايد اين امر را به دقت تحقيق كنند. اگر معلوم شد كه شاهد دروغ می‌گويد، 19مجازاتش بايد همان باشد كه او فكر می‌كرد مرد ديگر به آن محكوم می‌شد. به اين طريق شرارت را از ميان خود پاک خواهيد كرد. 20بعد از آن، كسانی كه اين خبر را بشنوند از دروغ گفتن در جايگاه شهود خواهند ترسيد. 21به شاهد دروغگو نبايد رحم كنيد. حكم شما در اين گونه موارد بايد چنين باشد: جان در برابر جان، چشم در برابر چشم، دندان در برابر دندان، دست در برابر دست و پا در برابر پا.