Deuteronomo 19 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 19:1-21

Mizinda Yothawirako

1Yehova Mulungu wanu akadzawononga anthu amene dziko lawo akukupatsani, ndipo inu mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼmizinda ndi mʼnyumba zawo, 2mukapatule mizinda itatu imene ili pakati pa dziko lomwe Yehova Mulungu akukupatsani kukhala lanu. 3Mudzakonze misewu ndi kuligawa patatu dzikolo limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, kuti aliyense wopha munthu akhoza kuthawirako.

4Ili ndi lamulo lokhudza munthu amene wapha mnzake mosazindikira osati mwadala, nathawira kumeneko kupulumutsa moyo wake. Ndi munthu amene wapha mnzake mosazindikira, popanda maganizo oyipa. 5Mwachitsanzo, munthu atapita ku nkhalango ndi mnzake kukadula mitengo, ndiye posamula nkhwangwa kuti adule mtengo, nkhwangwa ikhoza kuguluka nʼkukagwera mnzake uja nʼkumupha. Munthu ameneyo akhoza kuthawira ku umodzi mwa mizindayo napulumutsa moyo wake. 6Kupanda kutero ndiye kuti wolipsira akhoza kumuthamangitsa mwaukali ndi kumugwira ngati mtunda utalika, ndipo akhoza kumupha ngakhale kuti sanayenera kufa popeza sanaphe mnzake mwadala. 7Ichi ndi chifukwa chake ndikukulamulani kuti mudzipatulire nokha mizinda itatu.

8Ngati Yehova Mulungu wanu akulitsa malire anu monga analonjezera pa malumbiro ndi makolo anu, nakupatsani dziko lonse monga analonjezera, 9chifukwa chotsatira bwino malamulo onse amene ndikukuwuzani lero, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kuyenda mʼnjira zake nthawi zonse, ndiye kuti mukuyenera kupatula mizinda itatu yowonjezera. 10Muchite zimenezi kuti musakhetse magazi wosalakwa mʼdziko lanu limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa, ndipo kuti musapezeke ndi mlandu wokhetsa magazi.

11Koma ngati munthu adana ndi mnzake namubisalira panjira nʼkumuvulaza mpaka kumupha, nathawira ku umodzi mwa mizindayi, 12akuluakulu a mu mzinda wake akamugwire ndi kumubwezera ku mzinda wake namupereka kwa wolipsira kuti aphedwe. 13Osamumvera chisoni. Muyenera kuchotsa tchimo lokhetsa magazi wosalakwa mu Israeli kuti zinthu zizikuyenderani bwino.

14Musamasunthe mwala wa malire anu ndi mnzanu amene anayikidwa ndi makolo anu pa cholowa chimene mulandire mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.

Mboni

15Mboni imodzi siyokwanira kupeza munthu kuti ndi wolakwa pa mlandu uliwonse umene wapalamula. Nkhani itsimikizike ndi umboni wa anthu awiri kapena atatu.

16Ngati mboni yonama ifuna kunamizira munthu mlandu, 17anthu awiri okhudzidwa ndi mlanduwo ayenera kuyima pamaso pa Yehova pali ansembe ndi oweruza amene ali pa ntchito pa nthawiyo. 18Oweruza afufuze bwinobwino, ndipo ngati zatsimikizika kuti mboniyo ndi yabodza, yopereka umboni wonama pa mʼbale wake, 19ndiye kuti amuchitire iyeyo zimene anafuna kuchitira mʼbale wakezo. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu. 20Anthu ena onse adzamva zimenezi nachita mantha, ndipo choyipa choterechi sichidzachitikanso pakati panu. 21Osachita chisoni, moyo uzilipira moyo, diso kulipira diso, dzino kulipira dzino, dzanja kulipira dzanja ndi phazi kulipira phazi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

申命記 19:1-21

設立避難城

1「你們的上帝耶和華毀滅那些民族,把他們的土地賜給你們,使你們趕走他們,住進他們的城邑和房屋後, 2-3你們要把土地劃分為三個地區,在每個地區設立一座避難城,修好通往這三座城的道路,以便誤殺人者可以逃往最近的避難城。

4「如果有人無意間殺了素無冤仇的同伴,他可以逃往避難城,以保住性命。 5例如,有人和朋友去森林砍樹,斧頭脫柄,誤殺了朋友,他就可以逃往避難城,以保住性命。 6否則,如果避難城離誤殺人者太遠,怒火中燒的報仇者就會追上去殺死他。其實他是不該死的,因為他與被誤殺的人素無冤仇。 7因此,我吩咐你們要設立三座避難城。

8-9「如果你們謹遵我今天吩咐你們的這一切誡命,愛你們的上帝耶和華,一生遵行祂的旨意,祂就會按照祂對你們祖先所起的誓,擴張你們的疆域,把應許給你們祖先的土地賜給你們。那時,你們要再設三座避難城, 10免得無辜人的血流在你們的上帝耶和華賜給你們作產業之地,以致你們擔當枉殺無辜的罪。

11「如果有人因憎恨鄰居而暗中埋伏,殺了鄰居,然後逃到避難城, 12他本城的長老要派人去把他帶回來,交給復仇的人,將他處死。 13不可憐憫他,要從以色列除掉這種濫殺無辜的罪,這樣你們才會順利。

14「在你們的上帝耶和華將要賜給你們作產業之地,你們不可挪動鄰居的界石,因為那是先人立的。

15「如果人犯了什麼罪或有什麼過失,不可憑一個證人作證就定罪,要有兩三個證人才可以定案。 16如果有人作偽證誣陷別人, 17訴訟雙方要站在耶和華面前,讓當值的祭司和審判官定奪。 18審判官要仔細審查案件,如果發現那人作偽證, 19就要按照他企圖加給被誣告者的傷害處罰他。這樣,就從你們當中除掉了罪惡。 20其他人聽說後,都會害怕,不敢再做這種惡事。 21你們對惡人不可心軟,要以命償命,以眼還眼,以牙還牙,以手還手,以腳還腳。