Deuteronomo 17 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 17:1-20

1Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.

2Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake, 3ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba, 4ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli, 5mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala. 6Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi. 7Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

Mabwalo a Milandu

8Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 9Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita. 10Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo. 11Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere. 12Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli. 13Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.

Mfumu

14Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,” 15mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli. 16Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.” 17Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.

18Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi. 19Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa. 20Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

New Russian Translation

Второзаконие 17:1-20

1Не приноси в жертву Господу, своему Богу, вола или овцу с каким бы то ни было изъяном или недостатком, потому что это будет Ему отвратительно.

2Если найдутся у тебя в одном из городов, которые дает тебе Господь, мужчина или женщина, творящие зло в глазах Господа, твоего Бога, и нарушающие Его завет; 3если кто-нибудь, вопреки моему повелению, будет служить другим богам, поклоняясь им, или солнцу, или луне, или небесным звездам, 4и ты узнаешь об этом, то тщательно расследуй это дело. Если это окажется правдой и будет доказано, что в Израиле было сделано такое отвратительное дело, 5то приведи мужчину или женщину, которые сделали это, к городским воротам и забей их камнями до смерти. 6Человек может быть предан смерти по свидетельству двух или трех очевидцев, но никого нельзя предавать смерти по показанию только одного свидетеля. 7Свидетели должны первыми бросить в него камень, а потом и все остальные. Удали зло из твоей среды.

Суды

8Если на твой суд представят дело, которое слишком трудно рассудить, – будь то кровопролитие, тяжба или побои, – приведи судящихся на место, которое выберет Господь, твой Бог. 9Пойди к священникам из левитов и к судье, который будет в те дни, и спроси их. Они объявят тебе судейское решение. 10А ты должен поступить в соответствии с решением, объявленным на месте, которое выберет Господь. Смотри, сделай все, что они укажут тебе. 11Поступи по закону, которому они тебя научат, и по решению, которое они тебе дадут. Не уклоняйся от того, что они тебе скажут, ни вправо, ни влево. 12Тот, кто поступит дерзко и не послушает судью или священника, который служит Господу, твоему Богу, должен быть предан смерти. Ты должен искоренить зло в Израиле. 13Весь народ услышит об этом и испугается, и впредь не будет дерзким.

Царь

14Когда ты войдешь в землю, которую дает тебе Господь, твой Бог, завладеешь ею, поселишься в ней и скажешь: «Поставлю-ка я над собой царя, как все народы вокруг», 15то поставь царя, которого выберет Господь, твой Бог. Он должен быть из твоего народа. Не ставь над собой чужеземца, который будет не из твоего народа. 16Царь не должен приобретать множества коней и отправлять народ назад в Египет, чтобы приобрести еще больше, потому что Господь сказал вам: «Вы не должны возвращаться этим путем». 17Он не должен брать себе много жен, иначе его сердце развратится. Он не должен набирать для себя чрезмерно много серебра и золота.

18Заняв престол своего царства, он должен написать на свитке копию этого Закона, снятую с той, что у священников из левитов. 19Она должна быть у него, и он должен читать ее всю свою жизнь, чтобы учиться чтить Господа, своего Бога, и прилежно следовать всем словам этого Закона и этим установлениям: 20не мнить себя лучше всех своих братьев и не уклоняться от заповеди ни вправо, ни влево. Тогда он и его потомки будут долгое время царствовать над Израилем.