Deuteronomo 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 17:1-20

1Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.

2Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake, 3ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba, 4ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli, 5mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala. 6Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi. 7Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

Mabwalo a Milandu

8Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 9Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita. 10Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo. 11Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere. 12Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli. 13Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.

Mfumu

14Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,” 15mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli. 16Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.” 17Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.

18Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi. 19Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa. 20Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 17:1-20

1Suppose an ox or sheep has anything at all wrong with it. Then don’t sacrifice it to the Lord your God. He hates it.

2Someone living among you might do what is evil in the sight of the Lord your God. It might happen in one of the towns the Lord is giving you. That person is breaking the Lord’s covenant. 3The person might have worshiped or bowed down to other gods. That person might have bowed down to the sun or moon or stars in the sky. I have commanded you not to do these things. 4When you hear that people have done something like that, check the matter out carefully. If it’s true, an evil thing has been done in Israel. The Lord hates that. 5So take the person who has done that evil thing to your city gate. Put that person to death by throwing stones at them. 6Two or three witnesses are required to put someone to death. No one can be put to death because of what only one witness says. Two or three witnesses are required. 7The witnesses must throw the first stones. Then the rest of the people must also throw stones. Get rid of that evil person.

Law Courts

8People will bring their cases to your courts. But some cases will be too hard for you to judge. They might be about murders, attacks or other crimes. Then take those hard cases to the place the Lord your God will choose. 9Go to a priest, who is a Levite. And go to the judge who is in office at that time. Ask them for their decision. They will give it to you. 10They’ll hand down their decisions at the place the Lord will choose. You must do what they decide. Be careful to do everything they tell you to do. 11Act according to whatever they teach you. Accept the decisions they give you. Don’t turn away from what they tell you. Don’t turn to the right or the left. 12Someone might show that they don’t respect the judge. Or they will show that they don’t respect the priest. The priest will serve the Lord your God at the place God will choose. If anyone doesn’t show respect for these people, that person must be put to death. Remove that evil person from Israel. 13All the Israelites will hear about it. And they will be afraid to disrespect a judge or priest again.

Appoint the King the Lord Chooses

14You will enter the land the Lord your God is giving you. You will take it as your own. You will make your homes in it. When you do, you will say, “Let’s appoint a king over us, just like all the nations around us.” 15When that happens, make sure you appoint over yourselves a king the Lord your God chooses. He must be from among your own people. Don’t appoint over yourselves someone from another country. Don’t choose anyone who isn’t from one of the tribes of Israel. 16The king must not get large numbers of horses for himself. He must not make the people return to Egypt to get more horses. The Lord has told you, “You must not go back there again.” 17The king must not have many wives. If he does, they will lead him astray. He must not store up large amounts of silver and gold.

18When he sits on the throne of his kingdom, he must make for himself a copy of the law. He must write on a scroll the law that I am teaching you. He must copy it from the scroll of a priest, who is a Levite. 19The king must keep the scroll close to him at all times. He must read it all the days of his life. Then he can learn to have respect for the Lord his God. He can carefully obey all the words of this law and these rules. 20He won’t think of himself as being better than his people are. He won’t turn away from the law. He won’t turn to the right or the left. Then he and his sons after him will rule over his kingdom in Israel for a long time.