Deuteronomo 17 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 17:1-20

1Musapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ngʼombe kapena nkhosa imene ili ndi chilema kapena cholakwika chilichonse, pakuti zimenezi zimamunyansa.

2Ngati mwamuna kapena mkazi pakati panu, mʼmizinda imene Yehova akukupatsani apezeka akuchita zoyipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu pophwanya pangano lake, 3ndipo ngati motsutsana ndi lamulo langa wapembedza milungu ina, kuyigwadira milunguyo, kaya ndi dzuwa kapena mwezi kapena nyenyezi zakumwamba, 4ndipo inu nʼkuwuzidwa zimenezi, mufufuze bwinobwino. Ngati ndi zoona, ndipo ngati zatsimikizika kuti chonyansa choterechi chachitikadi mu Israeli, 5mumutengere mwamuna kapena mkazi amene wachita chonyansa choterechi ku chipata cha mzinda wanu ndi kumupha pomugenda miyala. 6Munthu aziphedwa pakakhala mboni ziwiri kapena zitatu koma osati mboni imodzi yokha ayi. 7Wochitira umboniwo ndiwo aziyamba kumupha munthuyo, ndipo kenaka anthu onse. Muyenera kuchotsa choyipa pakati panu.

Mabwalo a Milandu

8Ngati akubweretserani milandu mʼmabwalo anu imene ili yovuta kuweruza kaya ndi yokhetsa magazi, kaya ndi yophwanyirana ufulu, kaya ndi yovulazana, muyitengere kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 9Mudzapite kwa ansembe Alevi ndi kwa woweruza wa pa nthawi imeneyo. Kawafunseni ndipo iwowo adzakuwuzani zoyenera kuchita. 10Kachiteni zimene adzakuwuzenizo kuchokera ku malo amene Yehova adzasankhe. Kaonetsetseni kuti mukutsatira zonse zimene akuwuzanizo. 11Kachiteni motsatira malamulo ndi malangizo amene adzakuwuzeni; osawanyoza, potembenukira kumanja kapena kumanzere. 12Munthu aliyense amene adzanyoza woweruza kapena wansembe amene akutumikira kumeneko mʼmalo mwa Yehova Mulungu wanu, aphedwe ndithu. Muzichotsa choyipa pakati pa Israeli. 13Anthu onse adzamva zimenezi ndipo adzachita mantha, choncho sadzadzikuzanso.

Mfumu

14Mukalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mulitenge, ndipo mukakakhazikika mʼmenemo nimunena kuti, “Tiyeni tisankhe mfumu yoti izitilamulira monga imachitira mitundu yonse yotizungulirayi,” 15mudzakhazikitse mfumu yoti izikakulamulirani, mfumu imene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati panu. Mudzasankhe mfumuyo kuchokera pakati pa abale anu. Osasankha mlendo, munthu amene sachokera pakati pa abale anu Aisraeli. 16Komatu mfumuyo isadzikundikire akavalo, kapena kutuma anthu kupita ku Igupto kukayipezera akavalo ena, pakuti Ambuye akuti, “Simuyenera kubweranso ku Igupto mʼnjira yomweyo.” 17Asadziwunjikire akazi kuopa kuti mtima wake ungamusocheretse. Asadziwunjikirenso golide ndi siliva wambiri.

18Akakhala pa mpando waufumuwo, ayenera kulemba za iye mwini mʼbuku la malamuloli, kuchokera kwa ansembe Alevi. 19Asunge zimene walembazo ndipo ayenera kumaziwerenga masiku onse a moyo wake, kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wake posunga mosamalitsa malamulo ndi malangizowa. 20Asadzione kuti iyeyo ndi wopambana kuposa abale ake, nalekeratu kutsatira malamulo. Akasamala zimenezi iye ndi ana ake adzalamulira ufumu wa Israeli kwa nthawi yayitali.

Bibelen på hverdagsdansk

5. Mosebog 17:1-20

1De får, geder eller okser, I ofrer til Herren, må ikke være syge eller have fysiske skavanker. Den slags bryder Herren sig ikke om.

2-3Hvis I hører om nogle mænd eller kvinder i landets byer, der har brudt den pagt, I har sluttet med Herren, jeres Gud, og trodset hans befaling ved at dyrke afguder eller tilbede solen, månen eller stjernerne, 4skal I først undersøge, om rygtet taler sandt. Hvis der virkelig er tale om afgudsdyrkelse, 5skal vedkommende pågribes, føres uden for byen og stenes til døde. 6Henret aldrig nogen på grundlag af et enkelt vidneudsagn. Der skal mindst to eller tre vidner til. 7Vidnerne skal kaste de første sten, hvorefter de øvrige tilstedeværende skal stene den skyldige til døde. Derved fjerner I det onde fra jeres midte.

Den øverste domstol

8-9Visse retssager kan synes for komplicerede for de lokale dommere. Det kan dreje sig om ejendomsret, uagtsomt manddrab eller voldelige overfald. Den slags sager skal I overdrage til præsterne og den fungerende dommer ved helligdommen. 10-11Den dom, de fælder, kan ikke appelleres, men må følges til punkt og prikke. 12Hvis de anklagede nægter at anerkende den dom, som den ansvarlige præst eller dommer fælder, skal de straffes med døden. Den slags egenrådighed skal udryddes i Israel. 13Når folk hører om det, vil de blive bange og ikke gøre oprør en anden gang.

Bestemmelser om kongemagten

14Når I har indtaget det land, Herren, jeres Gud, vil give jer, og slået jer ned i landet, og I så tænker: ‚Vi burde have en konge ligesom vores nabofolk,’ 15må I ikke selv vælge en konge, men vente på, at Herren viser jer, hvem det skal være. Kongen skal være israelit, ikke udlænding, 16og han må ikke anskaffe sig masser af heste til sine krigstogter. Han må heller ikke sende folk til Egypten for at opkøbe heste, for Herren har udtrykkeligt advaret jer imod at vende tilbage til Egypten. 17Kongen må ikke tage sig mange koner, for at hans hjerte ikke skal vende sig fra Herren. Rigdom i store mængder må han heller ikke skaffe sig.

18Så snart han er blevet indsat og sætter sig på kongetronen, skal han få lavet sin egen kopi af lovbogen, som findes i præsternes varetægt.

19-20Denne kopi skal han altid have ved hånden, og han skal læse i den hver dag, så han kan lære at frygte Herren, adlyde hans befalinger og ikke føle sig hævet over sine landsmænd. Så vil han få lov at regere længe, og hans slægt vil få lov at sidde på Israels trone i mange generationer.