Deuteronomo 15 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 15:1-23

Chaka Chokhululukira Ngongole

1Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole. 2Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa. 3Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo. 4Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu. 5Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero. 6Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.

7Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo. 8Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna. 9Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa. 10Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza. 11Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.

Kumasula Akapolo a Chihebri

12Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri. 13Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja. 14Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani. 15Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.

16Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu, 17pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.

18Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.

Ziweto Zoyamba Kubadwa

19Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa. 20Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe. 21Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu. 22Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala. 23Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

New Russian Translation

Второзаконие 15:1-23

Год прощения долгов

1Раз в семь лет ты должен прощать долги. 2Вот как это следует делать: каждый заимодавец пусть простит долг, который он дал ближнему. Пусть он не требует уплаты долга со своего друга или брата, потому что провозглашено Господнее время для прощения долгов. 3Ты можешь требовать уплаты с чужеземца, но должен простить все, что должен тебе твой брат. 4Среди вас не должно быть бедняка, ведь в земле, которую Господь, твой Бог, отдает тебе во владение как твое наследие, Он щедро благословит тебя. 5Но только если ты будешь полностью послушен Господу, своему Богу, и будешь прилежно следовать всем этим повелениям, которые я даю тебе сегодня. 6И тогда Господь, твой Бог, благословит тебя, как и обещал, и ты будешь давать в долг многим народам, но ни у кого не будешь брать взаймы. Ты будешь править многими народами, но ни один из них не будет править тобой.

7Если среди твоих братьев в каком-либо из городов земли, которую дает тебе Господь, твой Бог, окажется бедняк, то не будь жестоким и скаредным к нуждающемуся брату. 8Будь щедрым и охотно дай ему взаймы все, в чем бы он ни нуждался. 9Берегись, чтобы не затаить подлую мысль: «Седьмой год, год прощения долгов, близок», и чтобы от того не озлобиться на своего нуждающегося брата и не отказать ему. Иначе он взмолится к Господу против тебя, и ты окажешься виновным в грехе. 10Дай ему щедро и сделай это без злобы в сердце – ведь за это Господь, твой Бог, благословит тебя во всех твоих делах и во всем, что ты делаешь своими руками. 11В этой земле всегда будут бедняки. Поэтому я повелеваю тебе быть щедрым к братьям, и к бедным, и к нуждающимся в твоей земле.

Освобождение слуг

(Исх. 21:2-6)

12Если твой соплеменник-еврей, мужчина или женщина, продаст себя15:12 Или: «будет продан». тебе и прослужит у тебя шесть лет, то на седьмой год ты должен отпустить его на свободу. 13А отпуская на свободу, не отсылай его с пустыми руками. 14Дай ему долю от своего мелкого рогатого скота, от своего гумна и винного пресса. Дай ему то, чем благословил тебя Господь, твой Бог. 15Помни, что ты сам был рабом в Египте, а Господь, твой Бог, избавил тебя от рабства. Поэтому я и даю тебе сегодня такое повеление.

16Но если раб скажет тебе: «Я не хочу уходить от тебя», потому что он любит тебя и твою семью, и у тебя ему хорошо, 17то возьми шило и приколи им его ухо к двери, и он останется твоим рабом на всю жизнь. Сделай то же самое и с рабыней.

18Не считай для себя убытком освободить раба, ведь он прослужил тебе шесть лет за половину стоимости наемника. Господь, твой Бог, благословит тебя во всем, что бы ты ни делал.

О первородном скота

19Отделяй для Господа, своего Бога, всех первородных самцов из стад и отар. Не работай на первородном воле и не стриги первородного барана. 20Каждый год ты и твоя семья должны есть их в присутствии Господа, твоего Бога, в месте, которое Он выберет. 21Если у животного есть изъян, если оно хромое или слепое, или у него есть какой-либо серьезный недостаток, то ты не должен приносить его в жертву Господу, твоему Богу. 22Ты должен съесть его в своем городе. И ритуально нечистый, и чистый человек может есть его мясо, как если бы это была газель или олень. 23Но ты не должен есть кровь. Выливай ее на землю, как воду.