Deuteronomo 15 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 15:1-23

Chaka Chokhululukira Ngongole

1Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole. 2Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa. 3Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo. 4Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu. 5Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero. 6Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.

7Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo. 8Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna. 9Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa. 10Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza. 11Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.

Kumasula Akapolo a Chihebri

12Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri. 13Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja. 14Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani. 15Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.

16Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu, 17pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.

18Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.

Ziweto Zoyamba Kubadwa

19Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa. 20Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe. 21Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu. 22Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala. 23Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 15:1-23

The Year for Forgiving People What They Owe

1At the end of every seven years you must forgive people what they owe you. 2Have you made a loan to one of your own people? Then forgive what is owed to you. You can’t require that person to pay you back. The Lord’s time to forgive what is owed has been announced. 3You can require someone from another nation to pay you back. But you must forgive what any of your own people owes you. 4There shouldn’t be any poor people among you. The Lord will greatly bless you in the land he is giving you. You will take it over as your own. 5The Lord your God will bless you if you obey him completely. Be careful to follow all the commands I’m giving you today. 6The Lord your God will bless you, just as he has promised. You will lend money to many nations. But you won’t have to borrow from any of them. You will rule over many nations. But none of them will rule over you.

7Suppose someone is poor among you. And suppose they live in one of the towns in the land the Lord your God is giving you. Then don’t be mean to them. They are poor. So don’t hold back money from them. 8Instead, open your hands and lend them what they need. Do it freely. 9Be careful not to have an evil thought in your mind. Don’t say to yourself, “The seventh year will soon be here. It’s the year for forgiving people what they owe.” If you think like that, you might treat the needy people among you badly. You might not give them anything. Then they might make their appeal to the Lord against you. And he will find you guilty of sin. 10So give freely to needy people. Let your heart be tender toward them. Then the Lord your God will bless you in all your work. He will bless you in everything you do. 11There will always be poor people in the land. So I’m commanding you to give freely to those who are poor and needy in your land. Open your hands to them.

Set Your Hebrew Servants Free

12Suppose any Hebrew men or women sell themselves to you. If they do, they will serve you for six years. Then in the seventh year you must let them go free. 13But when you set them free, don’t send them away without anything to show for all their work. 14Freely give them some animals from your flock. Also give them some of your grain and wine. The Lord your God has blessed you richly. Give to them as he has given to you. 15Remember that you were slaves in Egypt. The Lord your God set you free. That’s why I’m giving you this command today.

16But suppose your servant says to you, “I don’t want to leave you.” He loves you and your family. And you are taking good care of him. 17Then take him to the door of your house. Poke a hole through his earlobe into the doorpost. And he will become your servant for life. Do the same with your female servant.

18Don’t think you are being cheated when you set your servants free. After all, they have served you for six years. The service of each of them has been worth twice as much as the service of a hired worker. And the Lord your God will bless you in everything you do.

Male Animals Born First to Their Mothers

19Set apart every male animal among your livestock that was born first to its mother. Set it apart to the Lord your God. Don’t put a firstborn cow to work. Don’t clip the wool from a firstborn sheep. 20Each year you and your family must eat them. Do it in front of the Lord your God at the place he will choose. 21Suppose an animal has something wrong with it. It might not be able to see or walk. Or it might have a bad flaw. Then you must not sacrifice it to the Lord your God. 22You must eat it in your own towns. Those who are “clean” and those who are “unclean” can eat it. Eat it as if it were antelope or deer meat. 23But you must not eat meat that still has blood in it. Pour the blood out on the ground like water.