Deuteronomo 14 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 14:1-29

Zoletsedwa pa Maliro

1Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira, 2pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.

3Musamadye chinthu chilichonse chonyansa. 4Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi, 5mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale. 6Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya. 7Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye. 8Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.

9Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba. 10Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.

11Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya. 12Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba, 13nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba, 14mtundu uliwonse wa khwangwala, 15kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi, 16kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi, 17tsekwe, vuwo, dembo, 18indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.

19Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi. 20Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.

21Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.

Musamaphike mwana wambuzi mu mkaka wa mayi wake.

Za Chakhumi

22Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse. 23Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu. 24Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri), 25ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe. 26Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera. 27Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.

28Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu, 29kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.

New International Reader’s Version

Deuteronomy 14:1-29

“Clean” and “Unclean” Food

1You are the children of the Lord your God. Don’t cut yourselves to honor the dead. Don’t shave the front of your heads to honor the dead. 2You are a holy nation. The Lord your God has set you apart for himself. He has chosen you to be his special treasure. He chose you out of all the nations on the face of the earth.

3Don’t eat anything the Lord hates. 4Here are the only animals you can eat. You can eat oxen, sheep, goats, 5deer, gazelles, roe deer, wild goats, ibexes, antelope and mountain sheep. 6You can eat any animal that has a divided hoof. But it must also chew the cud. 7Some animals only chew the cud. Others only have a divided hoof. The camel, rabbit and rock badger chew the cud, but they don’t have a divided hoof. So you can’t eat them. They are not “clean” for you. 8Pigs aren’t “clean” for you either. They have a divided hoof, but they don’t chew the cud. So don’t eat their meat. And don’t touch their dead bodies.

9Many creatures live in water. You can eat all the ones that have fins and scales. 10But don’t eat anything that doesn’t have fins and scales. It isn’t “clean” for you.

11You can eat any “clean” bird. 12But there are many birds you can’t eat. They include eagles, vultures, and black vultures. 13They include red kites, black kites and all kinds of falcons. 14They include all kinds of ravens. 15They include horned owls, screech owls, gulls and all kinds of hawks. 16They include little owls, great owls, white owls 17and desert owls. They include ospreys and cormorants. 18They include storks and all kinds of herons. They also include hoopoes and bats.

19All flying insects are “unclean” for you. So don’t eat them. 20But you can eat any creature that has wings and is “clean.”

21If you find something that’s already dead, don’t eat it. You can give it to an outsider living in any of your towns. They may eat it. Or you can sell it to someone from another country. But you are a holy nation. The Lord your God has set you apart for himself.

Don’t cook a young goat in its mother’s milk.

Give a Tenth of What You Produce

22Be sure to set apart a tenth of everything your fields produce each year. 23Here are the things you should eat in the sight of the Lord your God. You should eat a tenth part of your grain, olive oil and fresh wine. You should also eat the male animals among your livestock that were born first to their mothers. Eat all these things at the special place the Lord your God will choose. He will put his Name there. You will learn to honor him always. 24But suppose the place the Lord will choose for his Name is too far away from you. And suppose your God has blessed you. And your tenth part is too heavy for you to carry. 25Then sell it for silver. Take the silver with you. Go to the place the Lord your God will choose. 26Use the silver to buy anything you like. It can be cattle or sheep. It can be any kind of wine. In fact, it can be anything else you wish. Then you and your family can eat there in the sight of the Lord your God. You can be filled with joy. 27Don’t forget to take care of the Levites who will live in your towns. They won’t receive any part of the land as their share.

28At the end of every three years, bring a tenth of everything you produce that year. Store it in your towns. 29Then the Levites can come and eat. That’s because they won’t receive any part of the land as their share. The outsiders and widows who live in your towns can come. So can the children whose fathers have died. Everyone can have plenty to eat. Then the Lord your God will bless you in everything you do.