Deuteronomo 13 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 13:1-18

Kupembedza Milungu Ina

1Ngati mneneri kapena wina aliyense amene amanena zamʼtsogolo mwa maloto atuluka pakati panu, nalengeza za chizindikiro chozizwitsa kapena chodabwitsa, 2chinthu nʼkuchitikadi, tsono iyeyo nʼkunena kuti, “Tiyeni titsatire milungu ina, tiyeni tiyipembedze,” (kunena milungu imene simunayidziwe), 3musamumvere mneneriyo kapena wolotayo. Yehova Mulungu wanu afuna akuyeseni kuti aone ngati mumamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse. 4Muyenera kutsatira Yehova Mulungu wanu, ndipo ndi Iyeyo amene muyenera kumuopa. Muzisunga malamulo ake ndi kumamumvera, muzimutumikira ndipo kumukangamira Iyeyo. 5Mneneri kapena wolotayo ayenera kuphedwa, popeza analalikira zopandukira Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto ndi kukupulumutsani ku dziko la ukapolo. Wolalikirayo anafuna kukupatutsani pa njira imene Yehova Mulungu wanu anakulamulirani kuti muyitsatire. Muzichotsa choyipa pakati panu.

6Ngati mʼbale wanu weniweni kapena mwana wanu wamwamuna kapena wamkazi, kapena mkazi wanu wokondedwa, kapena mnzanu wapamtima akukakamizani mwachinsinsi, nʼkumati, “Tiyeni tipite tikapembedze milungu ina” (milungu imene inuyo kapena makolo anu sanayidziwe, 7milungu ya anthu okuzungulirani, kaya ndi apafupi kapena akutali, kuchokera kumapeto mpaka kumapeto kwina kwa dziko lapansi), 8musamugonjere kapena kumumvera. Musamumvere chisoni. Musamuleke kapena kumutchinjiriza. 9Mumuphe ndithu. Dzanja lanu likhale loyambirira kumupha, kenaka manja a anthu ena onse. 10Mumuponye miyala mpaka kumupha, chifukwa anafuna kukupatutsani pa njira ya Yehova Mulungu amene anakutulutsani ku Igupto, dziko la ukapolo. 11Tsono Aisraeli onse adzamva nachita mantha, ndipo palibe mmodzi pakati panu amene adzachitenso choyipa chotere.

12Ngati mumvetsedwa kuti ku umodzi mwa mizinda imene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti mukhalemo, 13kwapezeka anthu ena oyipa pakati panu ndipo asocheretsa anthu ambiri mʼmizinda yanu, pomanena kuti, “Tiyeni tikapembedze milungu ina” (milungu imene simunayidziwe), 14mukuyenera kufunsa, kulondola ndi kufufuza bwino nkhaniyo. Ndipo ngati zitatsimikizikadi kuti ndi zoona kuti chinthu chonyansa chotere chachitikadi pakati panu, 15muyenera kuwapha onse okhala mu mzinda umenewo. Muwonongeretu kwathunthu mzindawo, anthu ake ndi ziweto zake zomwe. 16Katundu yense wa anthu mu mzindawo mumuwunjike pamodzi pakatikati pa bwalo losonkhanako ndipo mutenthe mzindawo pamodzi ndi katundu wake yense monga nsembe yathunthu yopsereza ya kwa Yehova Mulungu wanu. Mzinda umenewo ukhale bwinja mpaka muyaya, usadzamangidwenso. 17Musapezeke ndi kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa kuti Yehova abweze mkwiyo wake wochititsa manthawu. Adzakuchitirani chifundo ndi kukumverani chisoni, ndipo adzakuchulukitsani monga analonjeza mwa lumbiro kwa makolo anu, 18chifukwa mumamvera Yehova Mulungu wanu, kusunga malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino ndi kuchita zoyenera pamaso pake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Второзаконие 13:1-18

1Если пророк или толкователь снов появится среди вас и предскажет знамение или чудо, 2и если это знамение или чудо сбудется, и он скажет: «Обратитесь к другим богам (богам, которых вы не знали) и служите им», 3то вы не должны слушать того пророка или толкователя снов. Это Вечный, ваш Бог, испытывает вас, чтобы узнать, любите ли вы Его всем сердцем и всей душой. 4Вы должны следовать только за Вечным, вашим Богом, и только Его вы должны чтить. Храните Его повеления и слушайтесь Его; служите Ему и храните Ему верность. 5А тот пророк или толкователь снов должен быть предан смерти, потому что он призывал к отступничеству от Вечного, вашего Бога, Который вывел вас из Египта, из земли рабства. Этот пророк или толкователь снов пытался сбить тебя, Исроил, с пути, которым повелел тебе идти Вечный, твой Бог. Очисти себя от этого зла.

6Если кто-нибудь, даже твой родной брат13:6 Букв.: «брат твой, сын матери твоей»., или сын, или дочь, или любимая жена, или твой ближайший друг станут тайно искушать тебя, говоря: «Пойдём, чтобы служить другим богам» (богам, которых не знал ни ты, ни твои предки, 7богам народов, которые живут вокруг тебя, далеко или близко, от одного конца земли до другого), 8то не уступай этому человеку и не слушай его. Не жалей его. Не щади и не покрывай. 9Ты непременно должен убить его. Ты первым должен кинуть в него камень, а потом и все остальные. 10Забей его камнями до смерти, потому что он пытался увести тебя от Всевышнего, твоего Бога, Который вывел тебя из Египта, из земли рабства. 11Тогда весь Исроил услышит об этом и испугается, и никто не станет делать впредь такого зла среди вас.

12Если ты услышишь об одном из городов, которые Вечный, твой Бог, даёт тебе для жизни, 13что там появились негодяи, сбившие с пути его жителей, которые говорят: «Пойдём и будем служить другим богам» (богам, которых ты не знал), 14то ты должен подробно расспросить, всё проверить и расследовать это. И если это правда, и ты сможешь доказать, что такая мерзость была сделана среди вас, 15то ты непременно должен предать мечу всех живущих в том городе. Истреби его полностью: и народ, и скот. 16Всё богатство этого города собери посередине площади и сожги город со всем добром без остатка, как всесожжение Вечному, твоему Богу. Он должен остаться в руинах навсегда и никогда не должен быть отстроен вновь. 17Ни одной из тех проклятых вещей не должно остаться у тебя в руках, чтобы Вечный не обрушил на тебя Свой пылающий гнев. И тогда Он окажет тебе милость, пожалеет тебя и сделает твой народ более многочисленным, как Он клялся твоим предкам. 18Потому что ты слушаешься Вечного, своего Бога, хранишь все Его повеления, которые я даю тебе сегодня, и поступаешь правильно в Его глазах.