Deuteronomo 12 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 12:1-32

Malo Amodzi Opembedzera

1Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo. 2Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo. 3Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.

4Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa. 5Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako. 6Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu. 7Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.

8Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera, 9pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. 10Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa. 11Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova. 12Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo. 13Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune. 14Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.

15Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya. 16Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi. 17Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera, 18mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza. 19Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.

20Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire. 21Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire. 22Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya. 23Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama. 24Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi. 25Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.

26Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe. 27Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya. 28Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.

29Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo, 30ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.” 31Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.

32Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Второзаконие 12:1-32

О единственном месте для поклонения Аллаху

1Вот установления и законы, которым вы должны старательно следовать все дни, пока вы будете жить на земле, которую Вечный, Бог ваших предков, отдал вам во владение. 2Полностью уничтожьте все места, где народы, которых вы выселяете, служат своим богам: на высоких горах, на холмах и под тенистыми деревьями. 3Разрушьте их жертвенники, расколите священные камни и сожгите в огне столбы Ашеры. Разбейте истуканы их богов и сотрите в тех местах всякую память о них.

4Вы не должны служить Вечному, вашему Богу так, как они служат своим богам. 5Вы должны искать Вечного, вашего Бога, лишь на том месте, которое Он выберет среди всех ваших родов для поклонения Ему. Туда вы и должны приходить, 6туда приносите всесожжения и жертвы, десятины и особые дары, посвящённые по обету, добровольные приношения и первородное ваших стад и отар. 7Там, в присутствии Вечного, вашего Бога, вы и ваши семьи будете есть и радоваться всему, что сотворят ваши руки, потому что Вечный, ваш Бог, благословил вас.

8Вы не должны поступать так, как мы поступаем сегодня, – каждый, как ему кажется верным, 9потому что вы ещё не достигли мест покоя и наследия, которое Вечный, ваш Бог, даёт вам. 10Но вы перейдёте Иордан и поселитесь в земле, которую Вечный, ваш Бог, отдаёт вам в наследие, и Он даст вам покой от всех врагов вокруг вас, чтобы вы жили в безопасности.

11Тогда к месту, которое Вечный, ваш Бог, выберет для поклонения Ему, вы должны приносить всё, что я повелеваю вам: всесожжения и жертвы, десятины и особые дары, всё лучшее из имущества, что вы посвятили Вечному по обету. 12Веселитесь там перед Вечным, вашим Богом, вы, ваши сыновья и дочери, слуги и служанки, левиты из ваших городов, у которых нет ни собственного надела, ни наследия. 13Берегитесь, не приносите всесожжения там, где вам заблагорассудится. 14Приносите жертвы только в том месте, которое Вечный выберет в одном из ваших родов, и там соблюдайте всё, что я повелеваю вам.

Об употреблении мяса

15Впрочем, вы можете закалывать скот в любом из городов и есть столько мяса, сколько вам хочется по благословению, которое Вечный, ваш Бог, даёт вам, как если бы это было мясо газели или оленя. Все люди, ритуально нечистые и чистые, могут есть его. 16Но вы не должны есть кровь. Выливайте её на землю, как воду. 17Вы не должны есть у себя в городах десятины от зерна, молодого вина и масла, первородное ваших стад и отар, добровольные приношения, особые дары или всё то, что вы посвятили по обету. 18Всё это вы должны есть в присутствии Вечного, вашего Бога, на том месте, которое Вечный, ваш Бог, укажет вам, – все вы, ваши сыновья и дочери, слуги и служанки, левиты из ваших городов, – есть и радоваться перед Вечным, вашим Богом, всему, что сделали ваши руки. 19Смотрите, не пренебрегайте левитами, когда будете жить в своей земле.

20Когда Вечный, ваш Бог, расширит границы ваших земель, как Он и обещал вам, и вы захотите мясного и скажете: «Съем-ка я мяса», то тогда можете есть столько, сколько захотите. 21Если место, которое Вечный, твой Бог, выберет для поклонения Ему, будет слишком далеко от вас – можете закалывать скот из стад и отар, которые дал вам Вечный, и есть столько, сколько захотите у себя в городах, как я повелел вам. 22Ешьте их, как если бы это были газель или олень. И нечистый, и чистый человек может есть их.

Запрет употреблять в пищу кровь

23Но не ешьте кровь, потому что кровь – это жизнь, и вы не должны есть жизнь вместе с мясом. 24Вы не должны есть кровь; выливайте её на землю, как воду. 25Не ешьте её, и тогда с вами и с вашими детьми всё будет благополучно, потому что это будет правильно в глазах Вечного.

26Берите посвящённые вещи и то, что вы обещали отдать по обету, и приходите туда, куда укажет Вечный. 27Приносите свои всесожжения – и мясо, и кровь – на жертвенник Вечного, своего Бога. Кровь жертв вы должны выливать у жертвенника12:27 Или: «на жертвенник». Вечного, вашего Бога, а мясо можете съесть. 28Смотрите, следуйте всем установлениям, которые я даю вам, и тогда с вами и с вашими детьми всегда всё будет благополучно, потому что это правильно в глазах Вечного, вашего Бога.

Предупреждение об идолослужении

29Вечный, ваш Бог, искоренит перед вами народы, которые вы собираетесь завоёвывать и выселять. Но когда вы прогоните их и поселитесь на их земле, 30когда все они будут истреблены, тогда будьте осторожны и не угодите в западню, не интересуйтесь их богами и не говорите: «Как эти народы служат своим богам? Я буду делать точно так же». 31Вы не должны служить Вечному, вашему Богу, так, как они служат своим богам, потому что они творят всевозможные мерзости, которые Вечный ненавидит. Они даже сжигают своих сыновей и дочерей в огне как жертву своим богам.

32Смотрите, не делайте то, что я запрещаю вам. Не прибавляйте к этому ничего и ничего не убавляйте.