Deuteronomo 10 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 10:1-22

Miyala Ngati Yoyamba Ija

1Pa nthawi imeneyo Yehova anati kwa ine, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo ubwere nayo kwa Ine ku phiri. Upangenso bokosi lamatabwa. 2Ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya. Ndipo iwe ukuyenera kuyika miyalayo mʼbokosimo.”

3Choncho ndinapanga bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha ndi kusema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo ndinapita ku phiri nditanyamula miyala iwiri mʼmanja mwanga. 4Yehova analemba pa miyala iwiriyo zimene analemba poyamba, Malamulo Khumi amene analengeza kwa inu pa phiri paja, mʼmoto, pa tsiku la msonkhano. Ndipo Yehova anawapereka kwa ine. 5Tsono ndinatsika ku phiri kuja ndi kuyika miyalayo mʼbokosi ndinapanga lija monga Yehova anandilamulira, ndipo panopa ili mʼmenemo.

6Aisraeli anayenda kuchokera ku Beeroti Beni Yaakani mpaka ku Mosera. Kumeneko Aaroni anamwalira nayikidwa mʼmanda, ndipo mwana wake Eliezara anakhala wansembe mʼmalo mwake. 7Kuchokera kumeneko Aisraeli anapita ku Gudigoda, napitirira mpaka ku Yotibata, ku dziko la mitsinje ya madzi. 8Pa nthawi imeneyo Yehova anapatula fuko la Levi kuti anyamule bokosi la pangano la Yehova lija, kuti ayimirire pamaso pa Yehova, kutumikira ndi kunena madalitso pa dzina lake monga amachitira mpaka lero. 9Nʼchifukwa chake Alevi alibe gawo kapena cholowa pakati pa abale awo. Yehova ndiye cholowa chawo monga momwe Yehova Mulungu wanu anawawuzira.

10Tsopano ndinakhala ku phiri kuja kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku monga ndinachitira poyamba, ndipo Yehova anandimveranso nthawi iyi. Sichinali chifuniro chake kuti akuwonongeni. 11Yehova anati kwa ine, “Pita ndi kutsogolera anthuwa pa njira yawo, kuti alowe ndi kulandira dziko limene ndinalumbira kwa makolo awo kuti ndiwapatse.”

Kuopa Yehova

12Tsopano inu Aisraeli, nʼchiyani chimene Yehova afuna kwa inu? Iye akufuna kuti muzimuopa poyenda mʼnjira zake zonse ndi kumamukonda Iye, kumutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, 13ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene ndikukupatsani lero kuti zizikuyenderani bwino.

14Yehova Mulungu wanu ndiye mwini wake kumwamba ngakhale mmwambamwamba, dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo. 15Yehova anayika mtima wake pa makolo anu okha ndipo anawakondadi nasankha adzukulu awo mwa mitundu yonse pa dziko lapansi, kunena inuyo monga mulili lero. 16Motero chitani mdulidwe wa mitima yanu ndipo musakhalenso opulupudza. 17Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa milungu, Ambuye wa ambuye, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa, amene sakondera ndipo salandira ziphuphu. 18Iye amatchinjiriza ana amasiye ndi akazi amasiye, ndipo amakonda mlendo namupatsa chakudya ndi chovala. 19Muzikonda alendo popeza inuyo munali alendo mʼdziko la Igupto. 20Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye. Mumukakamire Iyeyo ndi kuchita malumbiro anu mʼdzina lake. 21Iye ndiye matamando anu, Mulungu wanu amene anakuchitirani zodabwitsa zazikulu ndi zoopsa zimene munaona ndi maso anu zija. 22Makolo anu amene anapita ku Igupto analipo makumi asanu ndi awiri onse pamodzi, ndipo tsopano Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani ngati nyenyezi zakumwamba.

New Russian Translation

Второзаконие 10:1-22

Новые каменные плитки

(Исх. 34:1-9)

1Тогда Господь сказал мне: «Высеки две каменные плитки, подобные прежним, и поднимись ко Мне на гору. Еще сделай деревянный ковчег. 2Я напишу на плитках слова, что были на первых плитках, которые ты разбил. Затем ты положишь их в ковчег».

3Я сделал ковчег из дерева акации, вытесал две каменные плитки, подобные прежним, и поднялся на гору с ними в руках. 4Господь написал на этих плитках то же, что и прежде, десять заповедей10:4 Букв.: «десять слов»., которые Он объявил вам на горе, из огня, в день собрания. И Господь дал их мне. 5Затем я вернулся, спустившись с горы, и положил плитки в ковчег, который я сделал, как повелел мне Господь, они и сейчас там.

Смерть Аарона и служение левитов

6(Израильтяне отправились от колодцев яаканитов10:6 Евр.: «беерот-бене-яакан». в Мосеру. Там Аарон умер и был похоронен, а Элеазар, его сын, унаследовал его священство. 7Оттуда они путешествовали в Гудгод, а далее в Иотвафу, землю, где много рек. 8В то время Господь отделил род Левия, чтобы они носили ковчег завета Господа, стояли перед Господом, служили Ему и благословляли Его именем, что они делают и до сих пор. 9Вот почему у левита нет доли и наследия среди своих братьев; Господь – его наследие, как Господь, твой Бог, и сказал ему.)

10Я пробыл на горе сорок дней и ночей, как и в первый раз, и Господь снова внял мне. Он не захотел истребить тебя. 11«Иди, – сказал мне Господь, – и веди народ в путь, чтобы они вошли и завладели землей, которую Я клялся отдать их отцам».

Повеление бояться Господа

12Итак, Израиль, о чем же просит тебя Господь, твой Бог, кроме того, чтобы ты боялся Господа, своего Бога, ходил всеми Его путями, любил Его, служил Господу, своему Богу, от всего сердца и от всей души 13и соблюдал повеления и установления Господа, которые я даю тебе сегодня для твоего же блага?

14Господу, твоему Богу, принадлежат небеса, даже небеса небес, земля и все, что на ней. 15И все-таки Господь пожелал любить твоих отцов и выбрал вас, их потомков, из всех народов, как это и есть сегодня. 16Обрежьте крайнюю плоть вашего сердца10:16 Люди с необрезанными сердцами – это метафора, обозначающая людей непокорных Богу. и больше не упрямьтесь. 17Ведь Господь, ваш Бог, – Бог богов и Владыка владык, великий Бог, могучий и грозный, беспристрастный и не берущий взятки. 18Он защищает дело сироты и вдовы, любит чужеземца, кормит и одевает его. 19И вам следует любить чужеземцев, потому что вы сами были чужеземцами в Египте. 20Бойся Господа, своего Бога, и служи Ему. Прилепись к Нему и клянись Его именем. 21Он – твоя хвала; Он – твой Бог, совершивший для тебя великие и страшные чудеса, которые ты видел своими собственными глазами. 22Твоих отцов, которые отправились в Египет, было семьдесят человек, а теперь Господь, твой Бог, сделал тебя многочисленным, как звезды на небе.