Deuteronomo 10 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Deuteronomo 10:1-22

Miyala Ngati Yoyamba Ija

1Pa nthawi imeneyo Yehova anati kwa ine, “Sema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija ndipo ubwere nayo kwa Ine ku phiri. Upangenso bokosi lamatabwa. 2Ndidzalembapo mawu amene anali pa miyala yoyamba ija, imene unayiphwanya. Ndipo iwe ukuyenera kuyika miyalayo mʼbokosimo.”

3Choncho ndinapanga bokosi lamatabwa amtengo wa mkesha ndi kusema miyala iwiri yofanana ndi yoyamba ija, ndipo ndinapita ku phiri nditanyamula miyala iwiri mʼmanja mwanga. 4Yehova analemba pa miyala iwiriyo zimene analemba poyamba, Malamulo Khumi amene analengeza kwa inu pa phiri paja, mʼmoto, pa tsiku la msonkhano. Ndipo Yehova anawapereka kwa ine. 5Tsono ndinatsika ku phiri kuja ndi kuyika miyalayo mʼbokosi ndinapanga lija monga Yehova anandilamulira, ndipo panopa ili mʼmenemo.

6Aisraeli anayenda kuchokera ku Beeroti Beni Yaakani mpaka ku Mosera. Kumeneko Aaroni anamwalira nayikidwa mʼmanda, ndipo mwana wake Eliezara anakhala wansembe mʼmalo mwake. 7Kuchokera kumeneko Aisraeli anapita ku Gudigoda, napitirira mpaka ku Yotibata, ku dziko la mitsinje ya madzi. 8Pa nthawi imeneyo Yehova anapatula fuko la Levi kuti anyamule bokosi la pangano la Yehova lija, kuti ayimirire pamaso pa Yehova, kutumikira ndi kunena madalitso pa dzina lake monga amachitira mpaka lero. 9Nʼchifukwa chake Alevi alibe gawo kapena cholowa pakati pa abale awo. Yehova ndiye cholowa chawo monga momwe Yehova Mulungu wanu anawawuzira.

10Tsopano ndinakhala ku phiri kuja kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku monga ndinachitira poyamba, ndipo Yehova anandimveranso nthawi iyi. Sichinali chifuniro chake kuti akuwonongeni. 11Yehova anati kwa ine, “Pita ndi kutsogolera anthuwa pa njira yawo, kuti alowe ndi kulandira dziko limene ndinalumbira kwa makolo awo kuti ndiwapatse.”

Kuopa Yehova

12Tsopano inu Aisraeli, nʼchiyani chimene Yehova afuna kwa inu? Iye akufuna kuti muzimuopa poyenda mʼnjira zake zonse ndi kumamukonda Iye, kumutumikira Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse, 13ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene ndikukupatsani lero kuti zizikuyenderani bwino.

14Yehova Mulungu wanu ndiye mwini wake kumwamba ngakhale mmwambamwamba, dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo. 15Yehova anayika mtima wake pa makolo anu okha ndipo anawakondadi nasankha adzukulu awo mwa mitundu yonse pa dziko lapansi, kunena inuyo monga mulili lero. 16Motero chitani mdulidwe wa mitima yanu ndipo musakhalenso opulupudza. 17Pakuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa milungu, Ambuye wa ambuye, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa, amene sakondera ndipo salandira ziphuphu. 18Iye amatchinjiriza ana amasiye ndi akazi amasiye, ndipo amakonda mlendo namupatsa chakudya ndi chovala. 19Muzikonda alendo popeza inuyo munali alendo mʼdziko la Igupto. 20Muziopa Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iye. Mumukakamire Iyeyo ndi kuchita malumbiro anu mʼdzina lake. 21Iye ndiye matamando anu, Mulungu wanu amene anakuchitirani zodabwitsa zazikulu ndi zoopsa zimene munaona ndi maso anu zija. 22Makolo anu amene anapita ku Igupto analipo makumi asanu ndi awiri onse pamodzi, ndipo tsopano Yehova Mulungu wanu wakuchulukitsani ngati nyenyezi zakumwamba.

La Bible du Semeur

Deutéronome 10:1-22

L’Eternel pardonne

1Alors, l’Eternel m’a dit : « Taille-toi deux tablettes de pierre pareilles aux premières et viens me trouver sur la montagne ; tu fabriqueras aussi un coffre en bois. 2J’inscrirai sur les tablettes les paroles qui étaient gravées sur les premières que tu as brisées et tu les déposeras dans le coffre. » 3Je fabriquai donc un coffre en bois d’acacia et je taillai deux tablettes de pierre semblables aux premières. Après quoi, je gravis la montagne, les deux tablettes en main. 4L’Eternel écrivit sur les nouvelles tablettes comme il l’avait fait sur les premières, les dix commandements qu’il vous avait communiqués sur la montagne du milieu du feu, le jour où vous étiez assemblés, et il me les remit. 5Je m’en retournai et redescendis de la montagne. Puis je déposai les tablettes dans le coffre que j’avais fabriqué : elles y sont restées comme l’Eternel me l’avait ordonné.

6Les Israélites10.6 Les v. 6-9 se rapportent à des événements postérieurs à ceux du Sinaï. partirent des puits des descendants de Yaaqân pour Moséra. C’est là que mourut Aaron, et qu’il fut enseveli. Eléazar, son fils, lui succéda comme grand-prêtre10.6 Voir Nb 20.28 ; 33.38.. 7De là, ils partirent pour Goudgoda, puis de là pour Yotbata où abondent les cours d’eau10.7 Dernière marche dans le désert, la quarantième année de leurs pérégrinations.. 8C’est à cette époque que l’Eternel choisit la tribu de Lévi pour porter le coffre de l’alliance de l’Eternel et se tenir en sa présence, pour être à son service et pour bénir le peuple en son nom – comme elle l’a fait jusqu’à ce jour10.8 Voir Nb 3.5-8 ; 8.5-19.. 9C’est pour cela que la tribu de Lévi n’a reçu ni part, ni patrimoine foncier comme ses tribus sœurs ; c’est l’Eternel ton Dieu qui est son patrimoine, comme il le lui a promis.

10Moi donc, je suis resté sur la montagne pendant quarante jours et quarante nuits, comme la première fois10.10 Voir Ex 34.28.. Et cette fois-ci encore, l’Eternel m’exauça et renonça à vous détruire. 11Il me dit : « Lève-toi, va prendre la tête de ce peuple pour qu’ils partent à la conquête du pays que j’ai promis par serment à leurs ancêtres ! »

L’appel à changer de vie

12Et maintenant, Israël, qu’attend de toi l’Eternel ton Dieu ? Simplement que tu le craignes en suivant toutes les voies qu’il t’a prescrites, en l’aimant et en le servant de tout ton cœur et de tout ton être, 13en observant ses commandements et ses lois que je te prescris aujourd’hui pour ton bien. 14Voici : le ciel, et même les cieux les plus élevés, appartiennent à l’Eternel ton Dieu ainsi que la terre et tout ce qu’elle contient. 15Et pourtant, c’est uniquement à tes ancêtres que l’Eternel s’est attaché pour les aimer, et c’est leurs descendants, c’est-à-dire vous, qu’il a choisis parmi tous les peuples, comme vous le constatez aujourd’hui. 16Opérez donc aussi une circoncision dans votre cœur et ne vous rebellez plus contre l’Eternel ; 17car l’Eternel votre Dieu est le Dieu suprême et le Seigneur des seigneurs10.17 Titre repris en 1 Tm 6.15 ; Ap 17.14 ; 19.16., le grand Dieu, puissant et redoutable, qui ne fait pas de favoritisme10.17 Voir Ac 10.34 ; Rm 2.11 ; Ep 6.9. et ne se laisse pas corrompre par des présents. 18Il rend justice à l’orphelin et à la veuve et témoigne son amour à l’étranger en lui assurant le pain et le vêtement. 19Vous aussi, vous aimerez l’étranger parmi vous, car vous avez été étrangers en Egypte.

Israël face à un choix

Craindre l’Eternel

20C’est l’Eternel ton Dieu que tu craindras, c’est à lui que tu rendras un culte, à lui seul que tu t’attacheras, et si tu prêtes serment, c’est par son nom que tu le feras. 21Il est le sujet de tes louanges, il est ton Dieu ; c’est lui qui a accompli pour toi ces œuvres extraordinaires et redoutables dont tu as été témoin10.21 Voir Ex 7 à 12.. 22Tes ancêtres vinrent en Egypte au nombre de soixante-dix10.22 Voir Gn 46.27 ; Ex 1.5 ; Ac 7.14., et maintenant l’Eternel ton Dieu t’a rendu aussi nombreux10.22 Voir Gn 15.5 ; 22.17 ; Hé 11.12. que les étoiles du ciel.