Danieli 6 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 6:1-28

Danieli Mʼdzenje la Mikango

1Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse, 2ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke. 3Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse. 4Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito. 5Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”

6Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali! 7Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango. 8Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.” 9Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.

10Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale. 11Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize. 12Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?”

Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”

13Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.” 14Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.

15Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”

16Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”

17Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli. 18Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.

19Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija. 20Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”

21Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali! 22Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”

23Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.

24Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.

25Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti,

“Mtendere uchuluke pakati panu!

26“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.

“Popeza Iye ndi Mulungu wamoyo

ndi wamuyaya;

ufumu wake sudzawonongeka,

ulamuliro wake sudzatha.

27Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,

amachita zizindikiro ndi zozizwitsa

kumwamba ndi pa dziko lapansi.

Iye walanditsa Danieli

ku mphamvu ya mikango.”

28Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

New International Reader’s Version

Daniel 6:1-28

Daniel Is Thrown Into a Den of Lions

1It pleased Darius to appoint 120 royal rulers over his entire kingdom. 2He placed three leaders over them. One of the leaders was Daniel. The royal rulers were made accountable to the three leaders. Then the king wouldn’t lose any of his wealth. 3Daniel did a better job than the other two leaders or any of the royal rulers. He was an unusually good and able man. So the king planned to put him in charge of the whole kingdom. 4But the other two leaders and the royal rulers heard about it. So they looked for a reason to bring charges against Daniel. They tried to find something wrong with the way he ran the government. But they weren’t able to. They couldn’t find any fault with his work. He could always be trusted. He never did anything wrong. And he always did what he was supposed to. 5Finally these men said, “We want to bring charges against this man Daniel. But it’s almost impossible for us to come up with a reason to do it. If we find a reason, it will have to be in connection with the law of his God.”

6So the two leaders and the royal rulers went as a group to the king. They said, “King Darius, may you live forever! 7All the royal leaders, high officials, royal rulers, advisers and governors want to make a suggestion. We’ve agreed that you should give an order. And you should make sure it’s obeyed. Your Majesty, here is the command you should make your people obey for the next 30 days. Don’t let any of your people pray to any god or human being except to you. If they do, throw them into the lions’ den. 8Now give the order. Write it down in the law of the Medes and Persians. Then it can’t be changed.” 9So King Darius put the order in writing.

10Daniel found out that the king had signed the order. In spite of that, he did just as he had always done before. He went home to his upstairs room. Its windows opened toward Jerusalem. He went to his room three times a day to pray. He got down on his knees and gave thanks to his God. 11Some of the other royal officials went to where Daniel was staying. They saw him praying and asking God for help. 12So they went to the king. They spoke to him about his royal order. They said, “Your Majesty, didn’t you sign an official order? It said that for the next 30 days your people could pray only to you. They could not pray to anyone else, whether god or human being. If they did, they would be thrown into the lions’ den.”

The king answered, “The order must still be obeyed. It’s what the law of the Medes and Persians requires. So it can’t be changed.”

13Then they spoke to the king again. They said, “Daniel is one of the prisoners from Judah. He doesn’t pay any attention to you, Your Majesty. He doesn’t obey the order you put in writing. He still prays to his God three times a day.” 14When the king heard this, he was very upset. He didn’t want Daniel to be harmed in any way. Until sunset, he did everything he could to save him.

15Then the men went as a group to King Darius. They said to him, “Your Majesty, remember that no order or command you give can be changed. That’s what the law of the Medes and Persians requires.”

16So the king gave the order. Daniel was brought out and thrown into the lions’ den. The king said to him, “You always serve your God faithfully. So may he save you!”

17A stone was brought and placed over the opening of the den. The king sealed it with his own special ring. He also sealed it with the rings of his nobles. Then nothing could be done to help Daniel. 18The king returned to his palace. He didn’t eat anything that night. He didn’t ask for anything to be brought to him for his enjoyment. And he couldn’t sleep.

19As soon as the sun began to rise, the king got up. He hurried to the lions’ den. 20When he got near it, he called out to Daniel. His voice was filled with great concern. He said, “Daniel! You serve the living God. You always serve him faithfully. So has he been able to save you from the lions?”

21Daniel answered, “Your Majesty, may you live forever! 22My God sent his angel. And his angel shut the mouths of the lions. They haven’t hurt me at all. That’s because I haven’t done anything wrong in God’s sight. I’ve never done anything wrong to you either, Your Majesty.”

23The king was filled with joy. He ordered his servants to lift Daniel out of the den. So they did. They didn’t see any wounds on him. That’s because he had trusted in his God.

24Then the king gave another order. The men who had said bad things about Daniel were brought in. They were thrown into the lions’ den. So were their wives and children. Before they hit the bottom of the den, the lions attacked them. And the lions crushed all their bones.

25Then King Darius wrote to people of all nations, no matter what language they spoke. He said,

“May you have great success!

26“I order people in every part of my kingdom to respect and honor Daniel’s God.

“He is the living God.

He will live forever.

His kingdom will not be destroyed.

His rule will never end.

27He sets people free and saves them.

He does miraculous signs and wonders.

He does them in the heavens and on the earth.

He has saved Daniel

from the power of the lions.”

28So Daniel had success while Darius was king. Things went well with Daniel during the rule of Cyrus, the Persian.