Danieli 6 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 6:1-28

Danieli Mʼdzenje la Mikango

1Kunamukomera Dariyo kusankha akalonga 120 kuti alamulire mu ufumu wonse, 2ndikusankha nduna zazikulu zitatu kuti ziwayangʼanire ndipo imodzi mwa ndunazo anali Danieli. Akalongawo amayangʼaniridwa ndi nduna zazikuluzo kuti zinthu za mfumu zisawonongeke. 3Tsono Danieli anadzionetsa kuti akhoza kugwira ntchito bwino kopambana nduna zinzake chifukwa anali wanzeru kwambiri. Ndiye mfumu inaganiza zomuyika kuti akhale woyangʼanira ufumu wonse. 4Chifukwa cha ichi, anzake ndi akalonga anayesa kupeza zifukwa zomutsutsira Danieli pa kayendetsedwe ka ntchito za dzikolo, koma sanapeze cholakwa chilichonse. Iwo sanapeze chinyengo mwa iye, chifukwa anali wokhulupirika ndipo sankachita chinyengo kapena kutayirira ntchito. 5Pomaliza, anthu awa ananena kuti, “Sitidzapeza cholakwa chilichonse chomutsutsira Danieli kupatula chokhacho chimene chikhudza chipembedzo cha Mulungu wake.”

6Choncho akalonga ndi nduna pamodzi anapita kwa mfumu ndipo anati: “Inu mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo wautali! 7Nduna zoyendetsa ufumu wanu, aphungu, akalonga ndi abwanamkubwa tonse tagwirizana kuti inu mfumu mukhazikitse lamulo ndi kulisindikiza kuti aliyense amene apemphera kwa mulungu wina kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, pa masiku makumi atatu otsatirawa, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango. 8Tsopano inu mfumu khazikitsani lamulo limeneli ndipo musindikizepo dzina lanu kuti lisasinthike monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sasinthidwa.” 9Choncho mfumu Dariyo anasindikizapo dzina lake pa lamuloli.

10Danieli atamva kuti lamulo lasindikizidwa, anapita ku nyumba kwake nalowa mʼchipinda chapamwamba chimene mazenera ake anali otsekula kuloza ku Yerusalemu. Katatu pa tsiku iye ankagwada pansi pa mawondo ndipo amapemphera, kuyamika Mulungu wake, monga momwe ankachitira kale. 11Ndipo anthu awa anapita pamodzi ndi kukapeza Danieli akupemphera ndi kupempha Mulungu wake kuti amuthandize. 12Kotero iwo anapita kwa mfumu ndipo anayankhula naye za lamulo lake kuti, “Kodi simunasindikize lamulo lakuti pa masiku makumi atatu otsatirawa aliyense amene apemphera kwa mulungu wina aliyense kapena kwa munthu kupatula kwa inu mfumu, adzaponyedwa mʼdzenje la mikango?”

Mfumu inayankha kuti, “Lamulo lilipobe monga mwa malamulo a Amedi ndi Aperezi, amene sangathe kusinthika.”

13Kenaka iwo anati kwa mfumu, “Danieli, amene ndi mmodzi mwa akapolo ochokera ku Yuda, sakulabadira inu mfumu, kapena lamulo limene munasindikizapo dzina lanu lija. Iye akupempherabe katatu pa tsiku.” 14Mfumu itamva izi, inavutika kwambiri mu mtima mwake. Iyo inayesa kupeza njira yopulumutsira Danieli. Iyo inachita chotheka chilichonse kufikira kulowa kwa dzuwa kuti imupulumutse.

15Ndipo anthuwo anapita pamodzi kwa mfumu ndipo anati kwa iye, “Kumbukirani, inu mfumu kuti monga mwa lamulo la Amedi ndi Aperezi, palibe chimene mfumu inalamulira kapena kukhazikitsa chimasinthidwa.”

16Choncho mfumu inalamula, ndipo anabwera naye Danieli ndi kukamuponya mʼdzenje la mikango. Mfumu inati kwa Danieli, “Mulungu wako amene umutumikira nthawi zonse, akupulumutse!”

17Anatenga mwala natseka pa khoma pa dzenje la mikango, ndipo mfumu inadindapo chizindikiro chake ndi cha nduna zake kuti wina asasinthepo kanthu pa za Danieli. 18Kenaka mfumu inabwerera ku nyumba yake ndipo inakhala usiku wonse osadya kanthu, osalola chosangalatsa chilichonse. Ndipo sinagone tulo.

19Mʼbandakucha, mfumu inanyamuka ndi kufulumira kupita ku dzenje la mikango lija. 20Itayandikira pa dzenjelo, inayitana Danieli moonetsa nkhawa, “Danieli, mtumiki wa Mulungu wa moyo! Kodi Mulungu wako, amene umutumikira nthawi zonse, wakulanditsa ku mikango?”

21Danieli anayankha kuti, “Inu mfumu mukhale ndi moyo wautali! 22Mulungu wanga anatumiza mngelo wake, ndipo anatseka pakamwa pa mikango. Iyo sinandivulaze chifukwa Mulungu anaona kuti ndine wosalakwa ndi kutinso sindinakulakwireni inu mfumu.”

23Mfumu inali ndi chimwemwe chopambana ndipo inalamulira kuti amutulutse Danieli mʼdzenjemo. Ndipo atamutulutsa Danieli mʼdzenjemo, sanapezeke ndi chilonda chilichonse pa thupi lake, chifukwa iye anadalira Mulungu wake.

24Mwa lamulo la mfumu, anthu onse amene ananeneza Danieli aja anagwidwa ndi kukaponyedwa mʼdzenje la mikango, pamodzi ndi akazi awo ndi ana awo. Ndipo asanafike pansi pa dzenjelo, mikango inawawakha ndi mphamvu ndi kuteketa mafupa awo onse.

25Kenaka mfumu Dariyo inalembera anthu a mitundu yonse, ndi anthu a ziyankhulo zosiyanasiyana a mʼdziko lonse kuti,

“Mtendere uchuluke pakati panu!

26“Ndikukhazikitsa lamulo kuti paliponse mʼdziko langa anthu ayenera kuopa ndi kuchitira ulemu Mulungu wa Danieli.

“Popeza Iye ndi Mulungu wamoyo

ndi wamuyaya;

ufumu wake sudzawonongeka,

ulamuliro wake sudzatha.

27Iye amalanditsa ndipo amapulumutsa,

amachita zizindikiro ndi zozizwitsa

kumwamba ndi pa dziko lapansi.

Iye walanditsa Danieli

ku mphamvu ya mikango.”

28Choncho Danieli anapeza ufulu pa nthawi ya ulamuliro wa Dariyo ndi ulamuliro wa Koresi wa ku Perisiya.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Даниял 6:1-28

Даниял в яме со львами

1Дарию было угодно поставить сто двадцать сатрапов, чтобы они управляли всем царством, 2а над ними – трёх сановников, одним из которых был Даниял. Сатрапы должны были отчитываться перед ними, чтобы царю не было никакого ущерба. 3Скоро Даниял так отличился среди сатрапов и сановников своими исключительными качествами, что царь уже думал поставить его над всем царством. 4Тогда сановники и сатрапы стали искать предлог, чтобы обвинить Данияла в неверном ведении царских дел. Но это им не удалось, потому что он был верен, и за ним не находилось ни оплошности, ни вины. 5Наконец, эти люди сказали:

– Нам не найти предлога для обвинения Данияла, разве только в Законе его Бога.

6Тогда сановники и сатрапы пришли все вместе к царю и сказали:

– О царь Дарий, живи вечно! 7Все царские сановники, военачальники, сатрапы, советники и наместники согласны в том, что царю следует дать повеление и наложить запрет, чтобы всякого, кто станет в течение следующих тридцати дней молиться иному богу или человеку, кроме тебя, о царь, бросили бы в яму со львами. 8Итак, о царь, издай запрет и подпиши указ, чтобы его нельзя было изменить – по законам мидян и персов, которые не подлежат отмене.

9И царь Дарий подписал этот указ и запрет.

10Когда Даниял узнал о том, что этот указ подписан, он пошёл домой в верхнюю комнату, окна которой открывались в сторону Иерусалима. Три раза в день он опускался на колени и молился, славя своего Бога, как он делал это и прежде. 11А заговорщики пришли все вместе и нашли Данияла молящимся и просящим милости у Аллаха. 12Тогда они пошли к царю и говорили с ним о его царском запрете:

– Разве ты не подписал запрета, по которому того, кто в течение следующих тридцати дней будет молиться иному богу или человеку, кроме тебя, о царь, бросили бы в яму со львами?

Царь ответил:

– Это воистину так, по законам мидян и персов, которые не подлежат отмене.

13Тогда они сказали царю:

– Даниял, один из иудейских пленников, не слушается ни тебя, о царь, ни запрета, который ты подписал. Он по-прежнему молится три раза в день.

14Услышав это, царь был очень расстроен; он решил спасти Данияла и до захода солнца всячески пытался это сделать.

15Но заговорщики все вместе пришли к царю и сказали ему:

– Вспомни, о царь, что по закону мидян и персов никакой запрет или повеление, изданные царём, изменить нельзя.

16Тогда царь отдал приказ, и Данияла привели и бросили в яму со львами. Царь сказал Даниялу:

– Пусть твой Бог, Которому ты верно служишь, спасёт тебя!

17Затем принесли камень и положили его на отверстие ямы, и царь запечатал его своей печатью и печатями вельмож, чтобы никто не освободил Данияла. 18Потом царь вернулся во дворец и постился весь вечер; он отказался от развлечений, и сон бежал от него.

19При первом свете зари царь встал и поспешил к яме со львами. 20Приблизившись к яме, он позвал Данияла жалобным голосом:

– Даниял, раб живого Бога, смог ли Аллах, Которому ты верно служишь, спасти тебя от львов?

21Даниял ответил:

– О царь, живи вечно! 22Мой Бог послал ангела Своего и замкнул пасти львов. Они не причинили мне вреда, потому что я оказался безвинным перед Ним. Да и пред тобой, о царь, я никогда не делал никакого зла.

23Царь был чрезвычайно рад за него и приказал вытащить Данияла из ямы. Когда Данияла вытащили из ямы, на нём не оказалось никаких ран, потому что он верил в своего Бога.

24По приказу царя обвинителей Данияла привели и бросили в яму со львами, вместе с их детьми и жёнами. И прежде чем они упали на дно ямы, львы схватили их и разодрали на части.

25Тогда царь Дарий написал ко всем народам, племенам и людям всякого языка, живущим по всей земле:

«Да умножится ваше благополучие!

26Я издаю указ, чтобы в каждой части моего царства люди трепетали перед Богом Данияла и боялись Его.

Ведь Он – Бог живой,

вечно сущий;

царство Его не погибнет,

владычество не прекратится.

27Он избавляет и спасает,

творит знамения и чудеса

на небесах и на земле.

Он избавил Данияла

от челюстей львиных».

28И Даниял преуспевал во времена правления Дария и Кира Персидского6:28 Или: «Дария, то есть Кира Персидского»..