Danieli 5 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 5:1-31

Malemba pa Khoma

1Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo. 2Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo. 3Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo. 4Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.

5Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba. 6Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.

7Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”

8Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu. 9Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.

10Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike! 11Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula. 12Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”

13Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda? 14Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera. 15Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera. 16Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”

17Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.

18“Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu. 19Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa. 20Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake. 21Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.

22“Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi. 23Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse. 24Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.

25“Mawu amene analembedwa ndi awa:

MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.

26“Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:

Mene: Mulungu wawerenga masiku a ufumu wanu ndipo wauthetsa.

27Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.

28Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”

29Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.

30Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa, 31ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Дониёл 5:1-31

Пророческая надпись на стене

1Несколько лет спустя царь Валтасар5:1 Валтасар – старший сын и соправитель Набонида, бывшего последним правителем Нововавилонской империи. Матерью Валтасара была Нитокрис, дочь Навуходоносора. устроил великий пир для тысячи своих приближённых и пил с ними вино. 2Выпив вина, Валтасар приказал принести золотые и серебряные кубки, которые его дед5:2 Букв.: «отец». Слово «отец» также может означать «предшественник»; то же в ст. 11, 13 и 18. Навуходоносор взял из Иерусалимского храма. Царь со своими приближёнными, жёнами и наложницами собирался пить из них. 3Золотые и серебряные кубки, взятые из храма Всевышнего в Иерусалиме, были принесены, и царь со своими приближёнными, жёнами и наложницами пил из них. 4Они пили вино и славили богов, сделанных из золота и серебра, из бронзы, железа, дерева и камня.

5В тот же час появились пальцы человеческой руки, которые стали писать на штукатурке стены царского дворца, рядом со светильником. Царь глядел на эту руку, когда она писала. 6Его лицо побледнело, и он так испугался, что его колени затряслись, и у него подкосились ноги.

7Царь громко закричал, чтобы привели волшебников, астрологов и колдунов, и сказал этим вавилонским мудрецам:

– Того, кто прочтёт эту надпись и объяснит мне её смысл, оденут в пурпур, возложат ему на шею золотую цепь, и он станет третьим человеком5:7 Третьим человеком – Набонид был первым человеком в царстве, а Валтасар, его соправитель, – вторым. в царстве.

8Все царские мудрецы вошли, но не смогли ни прочитать надписи, ни объяснить царю её смысл. 9Тогда царь Валтасар перепугался ещё больше, и его лицо побледнело ещё сильнее. Его приближённые были в крайнем замешательстве.

10Услышав голоса царя и его приближённых, в пиршественный зал вошла царица5:10 Или: «царица-мать». Это могла быть жена Навуходоносора, бабушка Валтасара, но, скорее всего, жена Набонида, мать Валтасара..

– О царь, живи вечно! – сказала она. – Не тревожься и не бледней! 11В твоём царстве есть человек, в котором пребывает дух святых богов5:11 Или: «святой, божественный дух».. Во времена твоего деда он прославился своей просвещённостью, разумом и мудростью, подобной мудрости богов. Царь Навуходоносор, твой дед, поставил его главой чародеев, волшебников, астрологов и колдунов – сам царь, твой дед. 12В этом человеке, Дониёле, которого царь назвал Валтасисаром, нашлись проницательность, знание, разум и умение толковать сны, раскрывать загадки и разрешать сложные задачи. Вели позвать Дониёла, и он объяснит тебе смысл надписи.

13Тогда Дониёла привели к царю, и царь сказал ему:

– Ты ли Дониёл, один из тех пленников, которых мой дед, царь, привёл из Иудеи? 14Я слышал, что в тебе пребывает дух богов5:14 Или: «божественный дух». и что в тебе нашлись просвещённость, разум и великая мудрость. 15Ко мне приводили мудрецов и волшебников, чтобы они прочитали эту надпись и объяснили мне её смысл, но они не смогли сделать этого. 16А о тебе я слышал, что ты можешь давать истолкования и разрешать трудные задачи. Если ты сможешь прочитать эту надпись и объяснить мне её смысл, то тебя оденут в пурпур, возложат тебе на шею золотую цепь, и ты станешь третьим человеком в царстве.

17И Дониёл ответил царю:

– Оставь дары себе и отдай награды кому-нибудь другому. Я и так прочитаю царю надпись и объясню ему её смысл.

18Царь, Бог Высочайший дал твоему деду Навуходоносору владычество и величие, славу и честь. 19От величия, которое Он ему дал, все народы, племена и люди всякого языка трепетали перед ним и боялись его. Тех, кого царь хотел предать смерти, он предавал смерти; тех, кого он хотел пощадить, щадил; тех, кого он хотел возвысить, возвышал, а тех, кого хотел смирить, смирял. 20Но когда его сердце возгордилось и огрубело от гордости, он был смещён с престола и лишён славы. 21Его прогнали от людей, и его разум уподобился разуму зверя; он жил с дикими ослами и ел траву, подобно волу; его тело омывалось небесной росой, пока он не признал, что Бог Высочайший властвует над царствами смертных и ставит над ними кого желает.

22Но ты, его внук5:22 Букв.: «сын». Слово «сын» также может означать «преемник». Валтасар, не смирил себя, хотя знал всё это! 23Ты возвысил себя против Владыки небес. Ты велел принести себе кубки из Его храма и со своими приближёнными, жёнами и наложницами пил из них. Ты славил богов из серебра и золота, из бронзы, железа, дерева и камня, которые не могут ни видеть, ни слышать, ни понимать. Но Всевышнего, в руках Которого твоя жизнь и все твои пути, ты не почтил. 24Поэтому и послана была от Него рука, которая сделала эту надпись.

25Вот что здесь написано:

Мене, Мене, Текел, У-парсин

26Вот смысл этих слов:

Мене5:26 Это слово означает «исчислен». – Всевышний исчислил дни твоего царствования и положил ему конец.

27Текел5:27 Это слово означает «взвешен». – ты взвешен на весах и найден слишком лёгким.

28Перес5:28 Это единственное число от слова «парсин» и может означать «разделён» или «Персия». – твоё царство разделено и отдано мидянам и персам.

29Тогда, по повелению Валтасара, Дониёла одели в пурпур, возложили ему на шею золотую цепь и провозгласили третьим человеком в царстве.

30В ту же ночь Валтасар, царь вавилонян, был убит, 31и Дарий Мидянин5:31 Дарий Мидянин – личность этого правителя точно не установлена. Есть предположение, что Дарий было тронным именем самого Куруша II Великого (см. сноску на 6:28). По другой версии Дарий был одним из наместников Куруша. принял царство в возрасте шестидесяти двух лет5:31 Этой ночью, в октябре 539 г. до н. э., персы захватили Вавилон..