Danieli 4 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 4:1-37

Maloto Achiwiri a Nebukadinezara

1Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi:

Mtendere uchuluke pakati panu!

2Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.

3Zizindikiro zake ndi zazikulu,

zozizwitsa zake ndi zamphamvu!

Ufumu wake ndi wamuyaya;

ulamuliro wake ndi wa mibadomibado.

4Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa. 5Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa. 6Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo. 7Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira. 8Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.

9Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire. 10Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi. 11Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi. 12Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.

13“Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba. 14Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake. 15Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda.

“ ‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka. 16Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.

17“ ‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’

18“Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”

Danieli Atanthauzira Maloto

19Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.”

Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani! 20Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi, 21mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake. 22Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.

23“Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’

24“Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu: 25Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna. 26Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira. 27Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”

Maloto Akwaniritsidwa

28Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara. 29Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni, 30iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”

31Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa. 32Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”

33Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.

34Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.

Ulamuliro wake ndi ulamuliro wa nthawi zonse;

ufumu wake udzakhala ku mibadomibado.

35Anthu onse a dziko lapansi

ali chabe pamaso pake.

Pakati pa angelo akumwamba

ndi anthu a dziko lapansi

palibe amene akhoza kumuletsa

Mulungu kuchita zimene afuna.

Kapena kunena kwa Iye kuti, “Kodi mwachita chiyani?”

36Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale. 37Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.

Persian Contemporary Bible

دانيال 4:1-37

خواب دوم نبوكدنصر

1نبوكدنصر پادشاه، اين پيام را برای تمام قومهای دنيا كه از نژادها و زبانهای گوناگون بودند، فرستاد:

با درود فراوان! 2می‌خواهم كارهای عجيبی را كه خدای متعال در حق من كرده است برای شما بيان كنم. 3كارهای او چقدر بزرگ و شگفت‌انگيز است. پادشاهی او جاودانی است و سلطنتش بی‌زوال!

4من نبوكدنصر در ناز و نعمت در قصر خود زندگی می‌كردم. 5يک شب خوابی ديدم كه مرا سخت به وحشت انداخت. 6دستور دادم تمام حكيمان بابل را احضار كنند تا خوابم را تعبير نمايند. 7وقتی همهٔ منجمان، جادوگران، فالگيران و طالع‌بينان آمدند، من خوابم را برای ايشان تعريف كردم، اما آنها نتوانستند آن را تعبير كنند. 8سرانجام دانيال مردی كه نام خدای من بلطشصر بر او گذاشته شده و روح خدايان مقدس در اوست، به حضور من آمد و من خوابی را كه ديده بودم برای او بازگو كرده، گفتم:

9«ای بلطشصر، رئيس حكيمان، می‌دانم كه روح خدايان مقدس در توست و دانستن هيچ رازی برای تو مشكل نيست. به من بگو معنی اين خوابی كه ديده‌ام چيست:

10‏-11«درخت بسيار بلندی ديدم كه در وسط زمين روييده بود. اين درخت آنقدر بزرگ شد كه سرش به آسمان رسيد به طوری كه همهٔ مردم دنيا می‌توانستند آن را ببينند. 12برگهايش تر و تازه و شاخه‌هايش پر بار بود و ميوهٔ كافی برای همهٔ مردم داشت. جانوران صحرايی زير سايه‌اش آرميده و پرندگان در میان شاخه‌هايش پناه گرفته بودند و تمام مردم دنيا از ميوه‌اش می‌خوردند.

13«سپس، در خواب ديدم كه فرشتهٔ مقدسی از آسمان به زمين آمد 14و با صدای بلند گفت: درخت را ببريد و شاخه‌هايش را قطع كنيد، ميوه و برگهايش را به زمين بريزيد تا حيوانات از زير آن و پرندگان از روی شاخه‌هايش بروند. 15ولی كندهٔ درخت و ريشه‌های آن را در زمين باقی بگذاريد و آن را با زنجير آهنی و مفرغی ببنديد و در ميان سبزه‌های صحرا رها كنيد. بگذاريد شبنم آسمان او را تر كند و با حيوانات صحرا علف بخورد! 16بگذاريد برای هفت سال عقل انسانی او به عقل حيوانی تبديل شود! 17اين تصميم بوسيلهٔ فرشتگان مقدس اعلام شده است تا مردم جهان بدانند كه دنيا در تسلط خدای متعال است و او حكومت بر ممالک دنيا را به هر كه اراده كند می‌بخشد، حتی به پستترين آدميان!

18«ای بلطشصر، اين بود خوابی كه ديدم. حال به من بگو تعبيرش چيست. تمام حكيمان مملكت من از تعبير اين خواب عاجز مانده‌اند، ولی تو می‌توانی آن را تعبير كنی زيرا روح خدايان مقدس در توست.»

19آنگاه دانيال كه به بلطشصر معروف بود در فكر فرو رفت و مدتی مات و مبهوت ماند. سرانجام پادشاه به گفت: «بلطشصر، نترس؛ تعبيرش را بگو.»

او جواب داد: «ای پادشاه، كاش آنچه در اين خواب ديده‌ای برای دشمنانت اتفاق بيفتد، نه برای تو! 20آن درختی كه ديدی بزرگ شد و سرش به آسمان رسيد به طوری كه تمام دنيا توانستند آن را ببينند، 21و برگهای تر و تازه و شاخه‌های پر بار و ميوهٔ كافی برای همهٔ مردم داشت، و حيوانات صحرا زير سايه‌اش آرميده و پرندگان در ميان شاخه‌هايش پناه گرفته بودند، 22ای پادشاه، آن درخت تويی، زيرا تو بسيار قوی و بزرگ شده‌ای و عظمت تو تا به آسمان و حكومت تو تا دورترين نقاط جهان رسيده است.

23«سپس فرشتهٔ مقدس را ديدی كه از آسمان به زمين آمد و گفت: ”درخت را ببريد و از بين ببريد، ولی كنده و ريشه‌های آن را در زمين باقی بگذاريد و آن را با زنجير آهنی و مفرغی ببنديد و در ميان سبزه‌های صحرا رها كنيد. بگذاريد با شبنم آسمان تر شود و هفت سال با حيوانات صحرا علف بخورد.“

24«ای پادشاه آنچه در اين خواب ديده‌ای چيزی است كه خدای متعال برای تو مقرر داشته است. تعبير خواب چنين است: 25تو از ميان انسانها رانده خواهی شد و با حيوانات صحرا به سر خواهی برد و مانند گاو علف خواهی خورد و از شبنم آسمان تر خواهی شد. هفت سال بدين منوال خواهد گذشت تا بدانی دنيا در تسلط خدای متعال است و او حكومت بر ممالک دنيا را به هر كه اراده كند می‌بخشد. 26اما چون گفته شد كنده و ريشه‌ها در زمين باقی بماند، پس وقتی پی ببری كه خدا بر زمين حكومت می‌كند، آنگاه دوباره بر تخت سلطنت خواهی نشست. 27پس، ای پادشاه، به نصيحت من گوش كن. از گناه كردن دست بردار و هر چه راست و درست است انجام بده و به رنجديدگان احسان كن تا شايد در امان بمانی.»

28تمام اين بلاها بر سر من كه نبوكدنصر هستم آمد. 29دوازده ماه بعد از اين خواب، يک روز بر پشت بام قصر خود در بابل قدم می‌زدم. 30و در وصف بابل می‌گفتم: «چه شهر بزرگ و زيبايی! من با قدرت خود اين شهر را برای مقر سلطنتم بنا كردم تا شكوه و عظمت خود را به دنيا نشان دهم.»

31سخنان من هنوز تمام نشده بود كه صدايی از آسمان گفت: «ای نبوكدنصر پادشاه، اين پيام برای توست: قدرت سلطنت از تو گرفته می‌شود. 32از ميان انسانها رانده می‌شوی و با حيوانات صحرا به سر می‌بری و مانند گاو علف می‌خوری. هفت سال بدين منوال می‌گذرد تا بدانی دنيا در تسلط خدای متعال است و او حكومت بر ممالک دنيا را به هر كه اراده كند می‌بخشد.»

33در همان ساعت اين پيشگويی انجام شد. من از ميان انسانها رانده شدم. مانند گاو علف می‌خوردم و بدنم با شبنم آسمان تر می‌شد. موهايم مثل پرهای عقاب دراز شد و ناخنهايم چون چنگال پرندگان گرديد.

34در پايان هفت سال، من كه نبوكدنصر هستم وقتی سرم را بلند كردم و به آسمان چشم دوختم عقلم به من بازگشت. آنگاه خدای متعال را پرستش كردم و آن وجود ابدی را كه سلطنت می‌كند و سلطنتش جاودانی است، ستايش نمودم. 35تمام مردم دنيا در برابر او هيچ شمرده می‌شوند. او در ميان قدرتهای آسمانی و در بين آدميان خاكی آنچه می‌خواهد می‌كند. هيچكس نمی‌تواند مانع او شود و يا او را مورد بازخواست قرار دهد. 36وقتی عقلم به سرم بازگشت، شكوه و عظمت سلطنت خود را باز يافتم. مشاوران و اميرانم نزد من بازگشتند و من بر تخت سلطنت نشستم و عظمتم بيشتر از پيش شد.

37اكنون من، نبوكدنصر، فرمانروای آسمانها را كه تمام اعمالش درست و بر حق است حمد و سپاس می‌گويم و نام او را به بزرگی ياد می‌كنم. او قادر است آنانی را كه متكبرند، پست و خوار سازد.