Danieli 12 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 12:1-13

Nthawi Yotsiriza

1“Pa nthawi imeneyo Mikayeli, mngelo wamkulu amene amateteza anthu a mtundu wako, adzabwera. Imeneyi idzakhala nthawi ya mavuto aakulu omwe sanaonekepo kuyambira pachiyambi cha mitundu ya anthu mpaka nthawi ikudzayo. Komatu pa nthawiyi anthu a mtundu wako, aliyense amene dzina lake lidzapezeke lolembedwa mʼbuku adzapulumutsidwa. 2Ambiri mwa amene akugona mʼnthaka adzadzuka: ena adzapita ku moyo wosatha, ena ku malo amanyazi ndi chilango chosatha. 3Amene ali anzeru mʼnjira ya chilungamo adzawala ngati kuwala kwa mlengalenga, ndipo amene alondolera ambiri ku njira yolungama, adzawala ngati nyenyezi ku nthawi zosatha. 4Koma iweyo, Danieli, sungitsa mawuwa, umate bukuli kufikira nthawi ya chimaliziro. Anthu ambiri adzapita uku ndi uko ndipo nzeru zidzanka zikukulirakulira.”

5Kenaka ine Danieli poyangʼana ndinaona anthu ena awiri atayima, wina tsidya lino la mtsinje, wina tsidya linalo. 6Mmodzi mwa awiriwo anafunsa munthu wovala chovala chosalala amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja kuti, “Kodi padzapita nthawi yayitali bwanji kuti zodabwitsazi zidzakwaniritsidwe?”

7Munthu wovala chovala chosalala, amene anali mʼmbali mwa madzi a mu mtsinje uja, anakweza dzanja lake lamanja ndi lamanzere kumwamba, ndipo ndinamumva akulumbira mʼdzina la Wamoyo ku nthawi zonse uja kuti, “Zidzachitika patapita zaka zitatu ndi theka. Zinthu zonsezi zidzachitika akadzatha masautso amene agwera anthu olungama.”

8Ndinamva, koma sindinamvetsetse. Choncho ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, nanga matsiriziro a zonsezi adzakhala chiyani?”

9Ndipo anandiyankha kuti, “Pita iwe Danieli, pakuti mawuwa ndi osungidwa ndi omatidwa kufikira nthawi ya chimaliziro. 10Anthu ambiri adzayeretsedwa nakhala olungama wopanda chodetsa, koma oyipa adzakhala chiyipire. Palibe mmodzi wa anthu oyipa amene adzamvetsetsa koma okhawo amene ali anzeru adzamvetsetsa.

11“Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290. 12Wodala munthu amene adikirabe nadzafika pa mapeto a masiku 1,335.

13“Koma iweyo Danieli, pitiriza ndipo ulimbikire mpaka matsiriziro. Kenaka udzamwalira. Koma mʼmasiku otsiriza udzauka kuti ulandire gawo lako.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Дониёл 12:1-13

О конце времён

1– В то время поднимется Микаил, великий ангел, защитник твоего народа. Тогда будет такое бедственное время, какого не было с тех пор, как появились народы. Но в то время твой народ – все, чьи имена будут найдены записанными в книгу, – будет избавлен. 2Многие из спящих в прахе земли проснутся: одни для вечной жизни, другие на позор и вечное отвращение. 3Мудрые12:3 Или: «Учащие мудрости». воссияют подобно ясному небу, и те, кто ведёт многих к праведности, – подобно звёздам, во веки и веки! 4Но ты, Дониёл, скрой эти слова и запечатай свиток, пока не придут последние времена. Многие будут метаться из стороны в сторону, а знание будет умножаться.

5Я, Дониёл, увидел, как появились двое других – один на одном берегу реки, а другой на другом берегу. 6Один из них сказал одетому в льняные одежды, который стоял над водами реки:

– Сколько времени пройдёт до конца этих непостижимых событий?

7Одетый в льняные одежды, который стоял над водами реки, поднял правую и левую руки к небу, и я услышал, как он клянётся Живущим вечно, говоря:

– Год, два года и полгода12:7 Букв.: «Время, времена и полвремени» – т. е. 3,5 года.. Когда не станет того, кто сломил силы святого народа12:7 Или: «Когда силы святого народа будут сломлены»., всё это совершится.

8Я услышал, но не понял. Тогда я спросил:

– Мой господин, каким будет исход всего этого?

9Он ответил:

– Иди, Дониёл. Эти слова скрыты и запечатаны до последних времён. 10Многие очистятся, убелятся и будут испытаны, но нечестивые будут продолжать поступать нечестиво. Никто из нечестивых не поймёт, но те, кто мудр, поймут.

11Со времени, когда будет отменена ежедневная жертва и будет поставлено осквернение, что ведёт к опустошению, пройдёт тысяча двести девяносто дней. 12Благословен тот, кто ждёт и достигнет завершения тысячи трёхсот тридцати пяти дней.

13А ты иди своим путём до конца. Ты упокоишься и в конце дней встанешь, чтобы получить свою долю.