Danieli 10 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Danieli 10:1-21

Masomphenya a Danieli a Munthu

1Chaka chachitatu cha Koresi mfumu ya Aperezi, Danieli amene ankatchedwa Belitesezara analandira mawu a vumbulutso. Uthenga wake unali woona ndipo anawumvetsa movutikira. Uthengawu anawumva kudzera mʼmasomphenya.

2Pa nthawi imeneyi, ine Danieli ndinalira kwa masabata atatu. 3Sindinadye chakudya chokoma; nyama ndi vinyo sizinakhudze milomo yanga ndi pangʼono pomwe; ndipo sindinadzole mafuta aliwonse mpaka patatha masabata atatu.

4Pa tsiku la 24 la mwezi woyamba, nditayima mʼmbali mwa mtsinje waukulu wa Tigirisi, 5ndinakweza maso ndipo ndinaona kuti pafupi ndi ine panali munthu wochokera ku Ufazi atavala zovala zosalala ndi lamba wa golide woyengeka bwino mʼchiwuno mwake. 6Thupi lake linali ngati mwala wonyezimira, nkhope yake ngati chiphaliwali, maso ake ngati muni wowala, manja ndi miyendo yake ngati mkuwa wowala, ndipo mawu ake ngati liwu la chikhamu cha anthu.

7Ine Danieli ndinali ndekha pamene ndinaona masomphenyawa; anthu amene anali ndi ine sanawaone, koma anadzazidwa ndi mantha kotero kuti anathawa ndi kukabisala. 8Choncho ndinatsala ndekha, ndikuonetsetsa masomphenya a ulemererowa. Ndiye nkhope yanga inasinthika, ndinalefuka, ndipo ndinalibenso mphamvu. 9Kenaka ndinamva iye akuyankhula, ndipo pamene ndinkamvetsera, ndinagwa chafufumimba ndi kugona tulo tofa nato.

10Dzanja linandikhudza ndi kundinyamula ndipo ndinachita ngati kuwerama pa mawondo manja atagwira pansi. 11Iye anati, “Danieli, iwe wokondedwa kwambiri, imirira ndipo uganizire mosamala mawu ndiyankhule kwa iwe, popeza tsopano ndatumidwa kwa iwe.” Atanena izi kwa ine ndinayimirira monjenjemera.

12Ndipo iye anapitiriza nati, “Usachite mantha Danieli. Kuyambira tsiku loyamba pamene unatsimikiza mtima kuti umvetse zinthuzi ndi kudzichepetsa pamaso pa Mulungu wako, pempho lako linamveka ndipo ndabwera kudzayankha mapemphero akowo. 13Koma mtsogoleri wa ufumu wa Peresiya ananditchingira pa masiku 21, kenaka Mikayeli, mmodzi mwa angelo akuluakulu anadza kudzandithandiza chifukwa ndinakhala komweko ndi mafumu a ku Peresiya. 14Tsopano ndafika kuti ndidzakufotokozere zimene zidzachitika kwa anthu a mtundu wako kutsogolo. Ndipo pali masomphenya enanso okhudza nthawi imene ikudza.”

15Pa nthawi yomwe ankanena izi kwa ine, ndinazolika nkhope yanga pansi kusowa chonena. 16Kenaka wina wa maonekedwe ngati munthu anakhudza milomo yanga, ndipo ndinatsekula pakamwa panga ndi kuyamba kuyankhula. Ndinati kwa amene anayima patsogolo panga, “Ine ndasweka mtima chifukwa cha masomphenyawa mbuye wanga, ndipo ndalefuka. 17Kodi ine mtumiki wamba wa mbuye wanga ndingathe bwanji kuyankhula ndi inu mbuye wanga? Mphamvu zanga zatha, ndipo ndikulephera kupuma.”

18Kenaka wooneka ngati munthu uja anandikhudzanso ndipo anandipatsa mphamvu. 19Iye anati, “Usachite mantha, munthu wokondedwa kwambiriwe. Mtendere ukhale ndi Iwe ndipo ukhale wolimba.”

Atayankhula nane, ndinalimbikitsidwa ndipo ndinati, “Yankhulani Mbuye wanga, popeza mwandipatsa mphamvu.”

20Ndipo iye anati, “Kodi ukudziwa chifukwa chimene ndabwerera kwa iwe? Ndiyamba ndabwerera kukamenyana ndi mtsogoleri wa ufumu wa Peresiya, ndipo ndikakanthana naye, kenaka mtsogoleri wa ufumu wa Grisi adzabwera. 21Koma ndikuwuza zimene zalembedwa mʼbuku la zoona koma palibe wondithandiza kulimbana nawo kupatula Mikayeli, kalonga wako.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

但以理書 10:1-21

底格里斯河邊的異象

1波斯塞魯士執政第三年,但以理,又名伯提沙撒,得到啟示。這啟示是真實的,是關於一場大爭戰的事。但以理通過異象明白了啟示的意思。

2那時,我但以理悲傷了三個星期, 3期間沒有吃過美味,沒有嚐過酒肉,沒有抹過膏油。 4一月二十四日,我站在底格里斯河邊, 5舉目觀看,見有一個人身穿細麻衣,腰束純金的帶子, 6身體如碧玉,面貌如閃電,眼睛如火炬,四肢如明亮的銅,聲音如眾人的呼喊。 7只有我但以理看見了這異象,跟我在一起的人都沒有看見,但他們極其恐懼,紛紛逃匿, 8只剩下我一人觀看這奇異的景象。我渾身無力,臉色蒼白,精疲力盡。 9接著,我聽見他說話的聲音,一聽見他的聲音,我便俯伏在地上昏睡過去。 10忽然有一隻手輕拍我,扶我用膝和手掌支撐起身體。 11他對我說:「倍受眷愛的但以理啊,要留心聽我說,站起來吧,因為我是奉命到你這裡來的。」他說完這話,我便戰戰兢兢地站起來。 12他說:「但以理啊,不要怕,從你在上帝面前謙卑地懇求明白這異象的第一天,你的禱告已蒙垂聽。我是來答覆你的。 13波斯國的守護神攔阻我二十一日。由於我滯留在波斯諸王那裡,天使長米迦勒便來幫助我。 14我來是要使你明白將來你同胞的遭遇,因為這異象是關於將來的事。」 15他對我說話時,我低著頭,說不出話。 16後來,有一位樣子像人的用手摸我的嘴唇,我便開口對站在我面前的說:「我主啊,因為這異象,我痛苦不堪,毫無氣力。 17僕人我怎能跟我主說話?我現在渾身無力,沒有氣息。」

18於是,那位樣子像人的再次摸我,使我有力量。 19他對我說:「倍受眷愛的人啊,不要怕,願你平安!要剛強勇敢。」我聽到他的話,便有了力量,於是對他說:「我主啊,請說,因為你使我有了力量。」 20他說:「你知道我為什麼要到你這裡來嗎?現在我要回去與波斯的守護神爭戰。我離開後,希臘的守護神就會來。 21除了你們的守護天使米迦勒以外,誰也不能幫助我抵擋他們。我來是要把記錄在真理書上的事告訴你。