Chivumbulutso 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 9:1-21

1Mngelo wachisanu anayimba lipenga lake, ndipo ndinaona nyenyezi ikugwa pa dziko lapansi kuchokera ku thambo. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi ya ku chidzenje chakuya. 2Nyenyeziyo itatsekula pa chidzenje chakuyacho panatuluka utsi ngati wochokera mʼngʼanjo yayikulu. Dzuwa ndi thambo zinada chifukwa cha utsi ochokera mʼdzenjemo. 3Ndipo mʼkati mwa utsimo munatuluka dzombe kukalowa mʼdziko lapansi ndipo linapatsidwa mphamvu zoluma ngati za zinkhanira pa dziko lapansi. 4Dzombelo linalamulidwa kuti lisawononge udzu wa pa dziko lapansi, kapena chomera chilichonse, kapena mtengo uliwonse, koma anthu okhawo amene analibe chizindikiro cha Mulungu pa mphumi zawo. 5Silinapatsidwe mphamvu yowapha koma yowazunza kwa miyezi isanu. Ndipo ululu umene anthuwo anawumva unali ngati wa chinkhanira chikaluma munthu. 6Masiku amenewo anthu adzafunafuna imfa koma sadzayipeza. Adzalakalaka kufa koma imfa izidzawathawa.

7Dzombe linkaoneka ngati akavalo okonzekera nkhondo. Pamitu pawo panali ngati zipewa zaufumu zagolide ndipo nkhope zawo ngati za anthu. 8Tsitsi lawo linali ngati la amayi, mano awo ngati a mikango. 9Dzombelo linavala za pachifuwa zachitsulo. Phokoso la mapiko awo linali ngati phokoso la magaleta ankhondo ambiri okokedwa ndi akavalo othamangira ku nkhondo. 10Linali ndi michira ngati zinkhanira ndi mbola. Mʼmichira yake munali mphamvu yozunza nayo anthu kwa miyezi isanu. 11Mfumu yawo inali mngelo wolamulira Chidzenje chakuya chija. Mʼchihebri dzina lake ndi Abadoni ndipo mʼChigriki ndi Apoliyoni (tanthauzo lake ndiye kuti, Wowononga).

12Tsoka loyamba lapita; matsoka ena awiri akubwerabe.

13Mngelo wachisanu ndi chimodzi anayimba lipenga lake, ndipo ndinamva liwu lochokera ku ngodya zinayi za guwa lansembe lagolide lija lokhala pamaso pa Mulungu. 14Liwulo linati kwa mngelo wachisanu ndi chimodzi amene anali ndi lipenga uja, “Masula angelo anayi amene anamangidwa pa mtsinje waukulu wa Yufurate.” 15Ndipo anamasulidwadi angelo anayi aja amene anasungidwa kukonzekera ora ili, tsiku ili, mwezi uwu ndi chaka ichi kuti aphe limodzi la magawo atatu a anthu. 16Ndinamva chiwerengero cha ankhondo a pa akavalo aja, kuti chinali 200 miliyoni.

17Akavalo ndi okwerapo amene ndinaona mʼmasomphenya anga ankaoneka motere: Zovala za pachifukwa pawo zinali zofiira ngati moto, zobiriwira ngati utsi, ndi zachikasu ngati miyala ya sulufule. Mitu ya akavalowo inali ngati ya mikango ndipo mʼkamwa mwawo munkatuluka moto, utsi ndi sulufule. 18Gawo limodzi la magawo atatu a anthu linaphedwa ndi miliri yamoto, utsi ndi sulufule zimene zinkachoka mʼkamwa mwawo. 19Mphamvu za akavalowo inali mʼkamwa mwawo ndi mʼmichira mwawo; pakuti michira yawo inali ngati njoka; ndi mitu imene inkalumira.

20Anthu ena onse amene sanaphedwe ndi miliri imeneyi sanalapebe kuti asiye ntchito zawo zoyipa. Iwo sanasiye kupembedza ziwanda ndi mafano agolide, asiliva, amkuwa, amwala ndi amtengo, mafano amene sangathe kuona, kumva kapena kuyankhula. 21Sanalapenso kuleka zakupha, zamatsenga awo, zachigololo zawo kapena umbava wawo.

New Russian Translation

Откровение 9:1-21

1Затрубил пятый ангел, и я увидел звезду, упавшую с неба на землю. Звезде был дан ключ от колодца бездны. 2Когда звезда открыла колодец бездны, оттуда поднялся дым, как из огромной печи. От дыма из колодца потемнели даже солнце и небо. 3Из дыма вышла на землю саранча9:3 Ср. Исх. 10:12-14., которой дана была власть, какую имеют на земле скорпионы. 4Ей было запрещено причинять вред земной траве, любым зеленым растениям и любому дереву, но она могла вредить тем людям, у которых на лбу не было печати Бога. 5Саранче не было разрешено убивать их, а только мучить пять месяцев. И люди мучились от боли, которая была как от укусов скорпиона. 6В те дни люди будут искать смерти и не смогут ее найти, они захотят умереть, но сама смерть убежит от них.

7Саранча была похожа на боевых коней, готовых к сражению. На ее головах было нечто вроде корон, как будто из золота, а ее лица были похожи на человеческие. 8Ее волосы напоминали женские, а зубы были похожи на клыки льва. 9На саранче была твердая, как железо, броня, и шум ее крыльев напоминал шум коней и боевых колесниц, мчащихся на сражение9:7-9 См. Иоиль 1:6; 2:4-9.. 10У нее были хвосты, как у скорпионов, и жала, и в этих хвостах заключалась ее власть вредить людям пять месяцев. 11Царем над ней был ангел бездны, его звали по-еврейски Аваддон, а по-гречески Аполлион («губитель»).

12Прошло первое горе, но еще предстояли два других.

13Затрубил шестой ангел, и я услышал голос, раздававшийся от четырех рогов золотого жертвенника, находящегося перед Богом9:13 См. Исх. 30:1-3.. 14Этот голос сказал шестому ангелу, держащему трубу:

– Освободи четырех ангелов, которые связаны у великой реки Евфрата. 15И четыре ангела, которые были приготовлены для этого часа, дня, месяца и года, были освобождены, чтобы погубить третью часть человечества. 16Конное войско насчитывало двести миллионов всадников: я слышал их число.

17Я видел в моем видении этих коней и всадников: на них огненно-красная, темно-синяя и желтая, как сера, броня. Головы коней похожи на головы львов, и из их пасти выходят огонь, дым и сера. 18Этими тремя губительными силами – огнем, дымом и серой, выходившими из их пастей, была погублена третья часть людей. 19Сила коней заключается в их пастях и в их хвостах. Хвосты эти похожи на змей: у них есть головы, которыми они и причиняли вред.

20Те, кто не был погублен этими бедствиями, так и не раскаялись в своих делах. Они по-прежнему поклонялись демонам и идолам из золота, серебра, бронзы, камня и дерева – идолам, которые не могут ни видеть, ни слышать, ни ходить9:20 См. Пс. 113:12-15; 134:15-17; Дан. 5:23.. 21Они не раскаялись ни в убийствах своих, ни в колдовстве, ни в разврате, ни в воровстве.