Chivumbulutso 5 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 5:1-14

Buku la Mwana Wankhosa

1Kenaka ndinaona buku mʼdzanja la wokhala pa mpando waufumu uja. Bukulo linali lolembedwa mbali zonse ndipo linali lomatidwa ndi zomatira zisanu ndi ziwiri. 2Ndipo ndinaona mngelo wamphamvu akulengeza ndi mawu okweza kuti, “Ndani ali woyenera kumatula zomatira ndi kufutukula bukuli?” 3Koma panalibe ndi mmodzi yemwe kumwamba kapena pa dziko lapansi kapena kunsi kwa dziko lapansi woti afutukule bukulo kapena kuona zamʼkati mwake. 4Ndinalira kwambiri chifukwa panalibe amene anapezeka woyenera kufutukula bukuli kapena kuona zamʼkati mwake. 5Tsono mmodzi mwa akuluakulu aja anati kwa ine, “Usalire! Taona, Mkango wa fuko la Yuda, Muzu wa Davide, wapambana. Iye angathe kufutukula bukuli ndi kumatula zomatira zisanu ndi ziwirizo.”

6Kenaka ndinaona Mwana Wankhosa akuoneka ngati wophedwa atayimirira pakatikati pa mpando waufumu uja ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Mwana Wankhosayo anali ndi nyanga zisanu ndi ziwiri ndi maso asanu ndi awiri omwe ndi Mizimu isanu ndi iwiri ya Mulungu yomwe anayitumiza ku dziko lonse lapansi. 7Iye anabwera natenga buku lija limene linali mʼdzanja lamanja la wokhala pa mpando waufumuyo. 8Ndipo atalitenga, zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu 24 aja anadzigwetsa pansi pamaso pa Mwana Wankhosa. Aliyense wa akuluakuluwo anali ndi zeze ndiponso mbale zagolide zodzaza ndi lubani. Lubaniyo ndi mapemphero a oyera mtima. 9Ndipo ankayimba nyimbo yatsopano yakuti,

“Inu ndinu woyenera kulandira bukuli

ndi kumatula zomatira zake,

chifukwa munaphedwa,

ndipo magazi anu munagulira Mulungu

anthu a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse, ndi mtundu uliwonse.

10Inu munawasandutsa kukhala mtundu waufumu ndi ansembe otumikira Mulungu,

ndipo adzalamulira dziko lapansi.”

11Kenaka nditayangʼananso ndinamva mawu a angelo ambiri, miyandamiyanda kuchulukitsa ndi miyandamiyanda. Anazungulira mpando waufumu pamodzi ndi zamoyo zija ndi akuluakulu aja. 12Ndipo angelowo anayimba ndi mawu ofuwula akuti,

“Mwana Wankhosa amene anaphedwayu

ndi woyenera kulandira ulamuliro, chuma, nzeru, mphamvu, ulemu,

ulemerero ndi mayamiko.”

13Kenaka ndinamva mawu a cholengedwa chilichonse kumwamba, pa dziko lapansi, kunsi kwa dziko lapansi, pa nyanja ndi zonse zili mʼmenemo zikuyimba kuti,

“Kwa wokhala pa mpando waufumu ndi kwa Mwana Wankhosa,

kukhale mayamiko, ulemu, ulemerero ndi mphamvu

mpaka muyaya!”

14Zamoyo zinayi zija zinati: “Ameni,” ndipo akuluakulu aja anadzigwetsa pansi napembedza.

Hoffnung für Alle

Offenbarung 5:1-14

Das Buch mit den sieben Siegeln

1Ich sah, dass der auf dem Thron in seiner rechten Hand eine Schriftrolle hielt. Sie war innen und außen beschrieben und mit sieben Siegeln verschlossen. 2Und ich sah einen mächtigen Engel, der mit lauter Stimme rief: »Wer ist würdig, die Siegel aufzubrechen und das Buch zu öffnen?« 3Doch es war niemand da, der es öffnen und hineinsehen konnte; niemand im Himmel, niemand auf der Erde und auch niemand im Totenreich. 4Da weinte ich sehr, weil niemand zu finden war, der würdig gewesen wäre, das Buch zu öffnen und hineinzusehen. 5Doch einer von den Ältesten5,5 Vgl. die Anmerkung zu Kapitel 4,4. sagte zu mir: »Weine nicht! Einer hat gesiegt; er kann das Buch öffnen und seine sieben Siegel brechen. Es ist der Löwe aus dem Stamm Juda, der Nachkomme von König David.«

6Und dann sah ich es: In der Mitte vor dem Thron, umgeben von den vier mächtigen Gestalten und den Ältesten, stand ein Lamm, das aussah, als ob es geschlachtet wäre. Es hatte sieben Hörner und sieben Augen. Das sind die sieben Geister Gottes, die in die ganze Welt ausgesandt worden sind. 7Das Lamm ging zu dem, der auf dem Thron saß, und empfing die Schriftrolle aus dessen rechter Hand. 8Im selben Augenblick fielen die vier Gestalten und die vierundzwanzig Ältesten vor dem Lamm nieder. Jeder Älteste hatte eine Harfe und goldene Schalen voller Weihrauch. Das sind die Gebete aller, die zu Gott gehören.

9Und alle sangen ein neues Lied:

»Du allein bist würdig, das Buch zu nehmen,

nur du darfst seine Siegel brechen.

Denn du bist als Opfer geschlachtet worden,

und mit deinem Blut hast du Menschen für Gott freigekauft,

Menschen aller Stämme und Sprachen,

aus allen Völkern und Nationen.

10Durch dich sind sie jetzt Könige und Priester,

die unserem Gott dienen.

Und sie werden über die ganze Erde5,10 Oder: auf der Erde. herrschen.«

11Danach sah ich viele Tausende und Abertausende von Engeln, eine unzählbare Menge, und ich hörte, wie sie gemeinsam etwas riefen. Sie standen um den Thron, um die vier Gestalten und um die Ältesten. 12Gewaltig ertönte ihre Stimme:

»Allein dem Lamm, das geopfert wurde,

gehören alle Macht und aller Reichtum.

Ihm allein gebühren Weisheit und Kraft,

Ehre, Herrlichkeit und Anbetung!«

13Dann hörte ich, wie auch alle anderen Geschöpfe einstimmten. Alle im Himmel und auf der Erde, im Totenreich und auch die Geschöpfe des Meeres, sie alle riefen:

»Anbetung und Ehre, alle Herrlichkeit

und Macht gebühren dem,

der auf dem Thron sitzt,

und dem Lamm für immer und ewig!«

14Die vier Gestalten bekräftigten dies mit ihrem »Amen«. Und die vierundzwanzig Ältesten fielen nieder und beteten Gott an.