Chivumbulutso 22 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 22:1-21

Mtsinje Wamoyo

1Ndipo mngeloyo anandionetsa mtsinje wamadzi amoyo, oyera ngati mwala wa krustalo ukutuluka ku mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa, 2Ukuyenda pakati pa msewu waukulu wa mu mzindawo. Mbali iliyonse ya mtsinjewo kunali mtengo wamoyo, utabala zipatso khumi ndi ziwiri. Kubereka zipatso mwezi uliwonse. Ndipo masamba a mtengowo ndi mankhwala wochiritsa anthu a mitundu ina. 3Sipadzakhalanso temberero lililonse. Mpando waufumu wa Mulungu ndi wa Mwana Wankhosa udzakhala mu mzindawo, ndipo atumiki ake adzamutumikira. 4Iwo adzaona nkhope yake ndipo dzina lake lidzalembedwa pa mphumi zawo. 5Sipadzakhalanso usiku. Sadzafuna kuwala kwa nyale kapena kwa dzuwa pakuti Ambuye Mulungu adzakhala kuwala kwawo. Ndipo adzalamulira kwamuyaya.

6Mngeloyo anandiwuza kuti, “Mawu awa ndi okhulupirika ndi owona. Ambuye Mulungu wa mizimu ya aneneri anatumiza mngelo wake kudzaonetsa atumiki ake zinthu zimene ziyenera kuchitika posachedwapa.”

Yesu Akubweranso

7“Taonani, ndikubwera posachedwa! Wodala ndi amene asunga mawu oneneratu za kutsogolo a mʼbuku ili.”

8Ine Yohane, ndine amene ndinamva ndi kuona zinthu izi. Ndipo pamene ndinamva ndi kuona izi ndinagwa pansi kuti ndipembedze mngelo amene amandionetsa zimenezi. 9Koma mngeloyo anandiwuza kuti, “Usatero ayi! Ine ndine wotumikira monga iwe pamodzi ndi abale ako aneneri ndi onse amene amasunga mawu a mʼbuku pembedzani Mulungu.”

10Kenaka anandiwuza kuti, “Usabise mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili chifukwa nthawi yayandikira. 11Wochita zoyipa apitirire kuchita zoyipazo; wochita zonyansa apitirire kuchita zonyansazo; wochita zabwino apitirire kuchita zabwinozo; ndipo woyera mtima apitirire kukhala woyera mtima.”

Mawu Otsiriza: Kuyitanidwa ndi Chenjezo

12“Taonani, ndikubwera posachedwa! Ndikubwera ndi mphotho zanga kuti ndidzapereke kwa aliyense malinga ndi zimene anachita. 13Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza, Chiyambi ndi Chimaliziro ndine.

14“Odala amene achapa mikanjo yawo, kuti akhale ndi ufulu wopita ku mtengo wamoyo ndi kuti akalowe mʼzipata za mu mzindawo. 15Kunja kuli agalu, amatsenga, achiwerewere, akupha anthu, opembedza mafano ndi aliyense amene amakonda bodza ndi kulichita.

16“Ine Yesu, ndatuma mngelo wanga kuti achitire umboni uwu ku mipingo. Ine ndine Muzu ndi Chipatso cha Davide ndipo ndine Nthanda Yonyezimira.”

17Mzimu Woyera ndi mkwatibwi akuti, “Bwerani!” Ndipo amene akumva anena kuti Bwerani! Iye amene ali ndi ludzu abwere, ndipo aliyense amene afuna alandire mphatso yaulere ya madzi amoyo.

18Ndikuchenjeza aliyense amene akumva mawu onena zamʼtsogolo a mʼbukuli kuti, “Ngati wina awonjezerapo kalikonse, Mulungu adzamuwonjezera miliri imene yalembedwa mʼbuku ili. 19Ndipo wina akachotsapo mawu onena zamʼtsogolo a mʼbuku ili, Mulungu adzachotsa gawo lake pa mtengo wamoyo ndi la mu mzinda woyera zimene zanenedwa mʼbuku ili.”

20Iye amene akuchitira umboni pa zinthu izi akuti, “Inde, Ine ndikubwera posachedwa.”

Ameni. Bwerani Ambuye Yesu.

21Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi anthu onse. Ameni.

O Livro

Apocalipse 22:1-21

O rio da vida

1Finalmente o anjo mostrou-me o rio da água da vida, limpa e cristalina, que saía do trono de Deus e do Cordeiro, 2e que fluía pelo meio da rua principal da cidade. De cada lado do rio crescia a árvore da vida que produz doze colheitas de frutos, uma em cada mês do ano; as suas folhas são utilizadas para curar as nações.

3Ali não haverá mais maldição porque o trono de Deus e do Cordeiro ali estarão. Os seus servos o adorarão, 4e verão diretamente o seu rosto. Terão gravado nas testas o nome de Deus. 5Ali nunca mais haverá noite e não serão precisos candeeiros. E tão-pouco o Sol é necessário, porque o Senhor Deus é a sua luz. E eles reinarão com o seu Deus para sempre.

6O anjo disse-me: “Estas palavras são inteiramente dignas de confiança e verdadeiras. Deus, o Senhor, que inspirou os profetas que falaram em seu nome, foi quem enviou agora o seu anjo para mostrar, a todos aqueles que põem as suas vidas ao seu serviço, as coisas que hão de acontecer brevemente.”

Jesus vem!

7“Atenção, porque o meu regresso está próximo! Feliz é aquele que guarda no coração as palavras proféticas deste livro.”

8Eu, João, sou aquele que vi e ouvi todas estas coisas. E quando as vi e ouvi, lancei-me ao chão para adorar o anjo que me tinha mostrado tudo aquilo. 9Mas ele impediu-me: “Não, não faças tal coisa! Porque eu sou teu companheiro de serviço, assim como dos teus irmãos, os profetas, e de todos os que aceitam o que está revelado neste livro. Só a Deus deves adorar.

10Não mantenhas em segredo as palavras proféticas deste livro”, disse-me ele. “Porque já está próximo o tempo em que elas se vão cumprir. 11O que pratica a injustiça continue a praticá-la. O que é mau continue a ser mau. O que é justo continue a ser justo. O que é santo continue a santificar-se.”

12“Eu virei em breve, trazendo a recompensa que cada um merece de acordo com as suas obras. 13Eu sou o Alfa e o Ómega, o primeiro e o último, a origem e o fim.”

14Felizes são todos os que lavam as suas roupas, para que tenham direito a entrar na cidade pelas portas e comer do fruto da árvore da vida. 15Mas ficarão de fora os cães (os impuros e inimigos de Deus), assim como os que se dedicam à feitiçaria e ao ocultismo, e os que praticam imoralidade sexual, e os assassinos, e os que praticam idolatria, e todos os que mentem e amam a mentira.

16“Eu, Jesus, enviei o meu anjo para vos revelar todas estas coisas destinadas às igrejas. Eu sou a própria raiz e descendência de David! Eu sou a radiosa estrela da manhã!”

17O Espírito Santo e a esposa dizem: “Vem!” E quem ouvir este apelo diga também: “Vem!” Quem tem sede, que se aproxime. Que todo aquele que quiser beba de graça da água da vida. 18Eu declaro solenemente a todo aquele que ouvir as palavras proféticas deste livro que, se alguém lhes acrescentar alguma coisa, Deus o castigará com as pragas que nele estão escritas. 19E se alguém tirar, seja o que for, às palavras proféticas deste livro, Deus lhe retirará a sua participação na árvore da vida e na cidade santa, que estão descritas neste livro.

20Aquele que revelou estas coisas afirma: “Sim, em breve voltarei!”

Que assim seja! Pois vem, Senhor Jesus!

21Que Jesus Cristo, o Senhor, vos conceda a todos a sua graça. Amém!