Chivumbulutso 21 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 21:1-27

Kumwamba ndi Dziko Lapansi Zatsopano

1Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse. 2Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake. 3Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo. 4‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’ ”

5Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”

6Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo. 7Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga. 8Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.”

Mzinda wa Yerusalemu Watsopano

9Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.” 10Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu. 11Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo. 12Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli. 13Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu. 14Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.

15Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake. 16Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200. 17Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito. 18Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi. 19Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido, 20achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto. 21Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.

22Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake. 23Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja. 24Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo. 25Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko. 26Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko. 27Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

Słowo Życia

Apokalipsa 21:1-27

Nowe niebo i nowa ziemia

1Potem zobaczyłem nowe niebo i nową ziemię, bowiem obecna ziemia i niebo zniknęły. Nie było również morza. 2I ujrzałem święte miasto—nową Jerozolimę, zstępującą z nieba, od Boga. Wyglądała wspaniale—jak panna młoda, która pięknie ubrała się dla swojego męża.

3Wtedy usłyszałem donośny głos dobiegający od tronu: „Odtąd Bóg będzie mieszkał wśród ludzi. Będą Jego ludem, a On będzie ich Bogiem 4i otrze z ich oczu wszelkie łzy. Nie będzie już więcej śmierci, smutku, płaczu ani bólu. Wszystko to przeminęło wraz ze starym światem”.

5Wówczas Ten, który zasiada na tronie, powiedział: „Oto czynię wszystko nowe!”. Potem zwrócił się do mnie:

—Zapisz to, słowa te są bowiem wiarygodne i prawdziwe.

6I mówił dalej: „Wykonało się! Ja jestem Alfa i Omega, Początek i Koniec. Spragnionym za darmo dam pić ze źródła wody życia. 7Zwycięzcy otrzymają wszystko: Ja będę ich Bogiem, a oni—moimi dziećmi. 8Natomiast tchórze, niewierzący, zwyrodnialcy, mordercy oraz ci, którzy prowadzą rozwiązłe życie, uprawiają czary, oddają cześć podobiznom bożków lub kłamią, trafią do ognistego jeziora płonącej siarki, które jest drugą śmiercią”.

9Wtedy podszedł do mnie jeden z siedmiu aniołów, trzymających puchary napełnione siedmioma ostatecznymi klęskami, i powiedział:

—Chodź, pokażę ci pannę młodą, którą zostanie małżonką Baranka.

Miasto Bożej chwały

10Dzięki mocy Ducha, anioł przeniósł mnie na szczyt wysokiej góry, skąd pokazał mi Jerozolimę—święte miasto, zstępujące z nieba, od Boga. 11Jaśniało ono Bożą chwałą jak kosztowny klejnot—wyglądało jak przejrzysty, kryształowy jaspis. 12Miało potężny, wysoki mur oraz dwanaście bram strzeżonych przez dwunastu aniołów. Na każdej z nich wypisane było imię jednego z dwunastu rodów Izraela. 13Z każdej strony—północnej, południowej, wschodniej i zachodniej—znajdowały się trzy bramy. 14Mur miasta zbudowany był na fundamencie składającym się z dwunastu warstw, na których wypisane były imiona dwunastu apostołów Baranka.

15Anioł, który do mnie mówił, miał z sobą złotą miarę, którą miał zmierzyć miasto, jego bramy oraz mur. 16Miasto zbudowane było na planie kwadratu—jego długość równała się szerokości. Anioł zmierzył długość, szerokość i wysokość miasta—każdy z tych wymiarów wynosił dwa tysiące czterysta kilometrów. 17Potem zmierzył mur—jego grubość wynosiła sześćdziesiąt pięć metrów.

18Całe miasto było zbudowane ze szczerego złota, czystego jak kryształ, a jego mur—z jaspisu. 19Poszczególne warstwy fundamentu, na którym stał mur, były ozdobione szlachetnymi kamieniami: pierwsza warstwa—jaspisem, druga—szafirem, trzecia—chalcedonem, czwarta—szmaragdem, 20piąta—sardoniksem, szósta—karneolem, siódma—chryzolitem, ósma—berylem, dziewiąta—topazem, dziesiąta—chryzoprazem, jedenasta—hiacyntem, dwunasta—ametystem. 21Każda z dwunastu bram wykonana była natomiast z jednej perły, a plac miasta wyłożony był szczerym złotem, czystym jak kryształ.

22Nie zauważyłem tam natomiast żadnej świątyni, ponieważ był nią sam Pan, wszechmocny Bóg, oraz Baranek. 23Miasto to nie potrzebowało słońca ani księżyca, bo rozjaśniała je chwała Boga, a jego światłem był Baranek. 24Jasność ta będzie świecić narodom świata, a ich władcy wniosą do tego miasta wszystko, co cenne. 25Jego bramy będą otwarte przez cały dzień, bo nie będzie tam nocy. 26Do miasta tego zostaną wniesione wszystkie wspaniałości narodów. 27Nie wejdzie do niego natomiast nic nieczystego ani żaden człowiek, którzy czyni zło i kłamie. Znajdą się tam tylko ci, którzy zostali zapisani w księdze życia Baranka.