Chivumbulutso 19 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 19:1-21

Babuloni Wagwa, Haleluya!

1Zitatha izi, ndinamva chimene chinamveka ngati phokoso la gulu lalikulu mmwamba likufuwula kuti,

“Haleluya!

Chipulumutso ndi ulemerero ndi mphamvu ndi za Mulungu wathu,

2pakuti chiweruzo chake ndi choona ndi cha chilungamo.

Iye waweruza mkazi wadama wotchuka uja

amene anayipitsa dziko lonse lapansi ndi zigololo zake.

Iye wabwezera pa mkaziyo magazi a atumiki ake.”

3Ndipo anafuwulanso kuti,

“Haleluya!

Utsi wochokera kwa mkazi wadamayo udzakwera kumwamba mpaka muyaya.”

4Akuluakulu 24 aja ndi zamoyo zinayi zija anadzigwetsa pansi kupembedza Mulungu amene anakhala pa mpando waufumu. Ndipo anafuwula kuti,

“Ameni, Haleluya!”

5Kenaka mawu anachoka ku mpando waufumu kuti,

“Lemekezani Mulungu wathu

inu nonse atumiki ake,

inu amene mumamuopa,

nonse angʼono ndi akulu!”

6Kenaka ndinamva chimene chinamveka ngati gulu lalikulu, ngati mkokomo wamadzi othamanga ndipo ngati kugunda kwakukulu kwa bingu, ndipo anati,

“Haleluya!

Pakuti Ambuye Mulungu wathu Wamphamvuzonse akulamulira.

7Tiyeni tisangalale ndi kukondwera

ndi kumutamanda!

Pakuti nthawi ya ukwati wa Mwana Wankhosa yafika,

ndipo Mkwatibwi wakonzekeratu.

8Wapatsidwa nsalu yoyera kwambiri, yowala ndi yosada

kuti avale.”

(Nsalu yoyera kwambiri ikuyimira ntchito zolungama za oyera mtima).

9Kenaka mngelo anandiwuza kuti, “Lemba kuti, Odala amene ayitanidwa ku phwando la ukwati wa Mwana Wankhosa.” Ndipo anatinso, “Awa ndiwo mawu woona a Mulungu.”

10Pamenepo ndinadzigwetsa pa mapazi ake kumupembedza. Koma anandiwuza kuti, “Usatero ayi, ine ndine mtumiki mnzako ngati iwe yemwe, ndiponso ngati abale ako amene asunga umboni wa Yesu. Pembedza Mulungu. Pakuti umboni wa Yesu ndiye mzimu wa uneneri.”

Wokwera pa Kavalo Woyera

11Ndinaona kumwamba kutatsekuka ndipo patsogolo panga panali kavalo woyera, amene anakwerapo dzina lake linali Wokhulupirika ndiponso Woona. Poweruza ndi kuchita nkhondo, amachita molungama. 12Maso ake anali ngati malawi amoto, ndipo pamutu pake panali zipewa zaufumu zambiri. Anali ndi dzina lolembedwa, lodziwika ndi Iye yekha, osati wina aliyense. 13Iye anavala mkanjo woviyika mʼmagazi, ndipo dzina lake ndi Mawu a Mulungu. 14Magulu ankhondo akumwamba ankamutsatira atakwera pa akavalo oyera, ndipo iwowo atavala nsalu zoyera kwambiri ndi zosada. 15Mʼkamwa mwake munatuluka lupanga lakuthwa limene anati akaphe nalo mitundu ya anthu. Iye adzalamulira ndi ndodo yachitsulo. Iye anaponda choponderamo mphesa cha ukali wa Mulungu Wamphamvuzonse. 16Pa chovala ndi pa ntchafu pake panalembedwa dzina ili:

MFUMU YA MAFUMU NDI MBUYE WA AMBUYE.

17Ndipo ndinaona mngelo atayimirira pa dzuwa amene anafuwula ndi mawu okweza kwa mbalame zonse zowuluka mlengalenga kuti, “Bwerani, sonkhanani pamodzi ku phwando lalikulu la Mulungu. 18Kuti mudye mnofu wa mafumu, wa akulu a ankhondo, ndi wa anthu amphamvu, wa akavalo ndi okwerapo awo, ndi wa anthu onse, mfulu ndi akapolo, angʼono ndi aakulu.”

19Kenaka ndinaona chirombo chija ndi mafumu a dziko lapansi ndi magulu ankhondo atasonkhana pamodzi kuti achite nkhondo ndi wokwera pa kavalo ndi ankhondo ake. 20Koma chirombocho chinagwidwa pamodzi ndi mneneri wonyenga uja amene anachita zizindikiro zodabwitsa pamaso pake. Ndi zizindikirozi anasocheretsa amene analembedwa chizindikiro cha chirombocho napembedza fano lake. Onse awiri anaponyedwa amoyo mʼnyanja yamoto yasulufule wotentha. 21Ena onse anaphedwa ndi lupanga lija linatuluka mʼkamwa mwa wokwera pa kavalo uja, ndipo mbalame zonse zinadya mokwanira mnofu wa anthu akufawo.

Slovo na cestu

Zjevení 19:1-21

Boží soudy jsou spravedlivé

1Potom jsem slyšel jednohlasý sbor mohutného zástupu v nebi:

„Haleluja, chvalte Boha!

Jeho vítězství, sláva i moc, 2jeho soudy

jsou jedině správné a spravedlivé.

On vykonal rozsudek nad tou nevěstkou,

která vínem svých neřestí přivedla do záhuby celou zemi, on pomstil své služebníky,

jejich krev ulpěla na jejích rukou.“

3A pak ještě:

„Haleluja chvalte Boha.

To město chtělo vládnout na věky

a věčně ho bude připomínat jenom oblak dýmu.“

4Čtyřiadvacet starců a ty čtyři bytosti padli na kolena, hluboce se klaněli Bohu sedícímu na trůnu a volali:

„Je to tak, chvála Bohu!“

5Od trůnu zazněl hlas:

„Chvalte Boha všichni,

kteří mu sloužíte a ctíte ho, malí i velcí!“

Beránkova svatební hostina: Kristus a jeho církev – navždy spojeni

6Pak se ozvalo mocné volání připomínající hukot vodopádu nebo hřmění bouře:

„Haleluja, chvalme Boha.

Náš všemocný Bůh a Pán se ujal své vlády.

7Radujme se, jásejme, vzdejme mu čest!

Nadešel den Beránkovy svatby.

Jeho nevěsta církev je už připravena.

8Dostala běloskvoucí svatební šaty z nejjemnější látky,

utkané ze svatého života vykoupených.“

9Anděl mi dal pokyn: „Piš! Dobře bude těm, kdo jsou pozváni na Beránkovu svatbu. To jsou slova samotného Boha.“ 10Přemohla mne vděčnost, padl jsem před andělem na kolena, ale on mne zvedl a řekl mi: „To nesmíš! Jsem přece pouhý služebník jako ty a tvoji bratři, kterým je svěřeno Ježíšovo poselství. Jenom Bohu se klaněj!“

Jezdec na bílém koni: spravedlivý rozsudek vykonán

11Pak jsem uviděl otevřené nebe a hle, bílý kůň; a jezdec, který na něm seděl, se jmenoval Věrný a Pravý. To je ten, který vynáší spravedlivé rozsudky a vede spravedlivý boj. 12Jeho oči jsou jako naskrz propalující plamen, jeho hlavu zdobí mnohonásobná královská koruna. Na čele má napsané jméno, které nikdo nezná než on sám. Je ztělesněné Boží Slovo. 13-14Oděv má zbrocený krví. Následuje ho družina jezdců na bílých koních, v pláštích z bělostného plátna. 15Z jeho úst vychází ostrý meč, kterým přemáhá národy. Nastolí novou vládu své spravedlnosti a jako vinař tlačí hrozny v lisu, tak ve spravedlivém hněvu vykoná soud nad bezbožnými. 16Na boku svého pláště má napsáno:

král králů, pán pánů.

17-18Dále jsem viděl anděla, stojícího v plném slunci. Svolával mrchožravé ptáky, kteří létali nad ním: „Poleťte sem, budete hodovat na Božích nepřátelích, králích, vojevůdcích, bojovnících, koních i jezdcích, svobodných i otrocích, slabých i mocných!“

19Tu jsem viděl, jak se pozemští vládcové a jejich armády střetli s jezdcem a jeho vojskem. 20Šelma a lživý prorok, (který jí přisluhoval a svými zázraky mnohé svedl, aby přijali znak té šelmy a klaněli se její soše) skončili v moři plamenů. 21Jejich armády byly pobity mečem jezdce na bílém koni a ptáci se vrhli na těla mrtvých.