Chivumbulutso 17 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 17:1-18

Mkazi Wachiwerewere

1Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja amene anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri anadza nati kwa ine, “Bwera ndikuonetse chilango cha mkazi wadama wotchuka uja amene akukhala pambali pa madzi ambiri. 2Mafumu a dziko lapansi amachita naye chigololo ndipo okhala pa dziko lapansi analedzera ndi vinyo wa zigololo zake.”

3Kenaka mngeloyo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku chipululu. Kumeneko ndinaona mkazi atakhala pa chirombo chofiira chokutidwa ndi mayina a chipongwe ndipo chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi. 4Mkaziyo anavala zovala za pepo ndi zofiira nadzikongoletsa ndi golide, miyala yapamwamba ndi ngale. Ananyamula chikho chagolide mʼdzanja lake, chodzaza ndi zinthu zonyansa ndi fungo loyipa la zigololo zake. 5Pa mphumi pake panalembedwa dzina lodabwitsa:

BABULONI WAMKULU

MAYI WA AKAZI ADAMA

NDI WAZOYIPITSA ZA DZIKO LAPANSI.

6Ndinaona kuti mkaziyo anali ataledzera ndi magazi a oyera mtima, magazi a amene anachitira umboni Yesu.

Nditamuona mkaziyo ndinadabwa kwambiri. 7Kenaka mngelo uja anati kwa ine, “Bwanji ukudabwa? Ndikufotokozera chinsinsi cha mkaziyu ndi chinsinsi cha chirombo chimene wakwerapochi chokhala ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi. 8Chirombo chimene wachionachi chinalipo kale koma tsopano kulibe ndipo chidzatuluka ku chidzenje chakuya ndi kupita kukawonongedwa. Anthu okhala pa dziko lapansi amene mayina awo sanalembedwe mʼbuku lamoyo kuyambira pa kulengedwa kwa dziko lapansi adzadabwa pamene adzaona chirombocho, chifukwa chinalipo kale, tsopano kulibe, komabe chidzabwera.

9“Zimenezi zikufunika kuganizira mwanzeru. Mitu isanu ndi iwiriyo ndi mapiri asanu ndi awiri pomwe mkazi uja amakhalirapo. Yomweyonso ndi mafumu asanu ndi awiri. 10Mafumu asanu anagwa, imodzi ilipo ndipo ina sinabwere; koma pamene idzafika, idzayenera kukhala kwa kanthawi kochepa. 11Chirombo chomwe chinalipo kale ndipo tsopano kulibe ndiyo mfumu yachisanu ndi chitatu. Iyo ndi ya mʼgulu la asanu ndi awiriwo ndipo ikupita kukawonongedwa.

12“Nyanga khumi unaziona zija ndi mafumu khumi amene sanapatsidwe ulamuliro, koma adzapatsidwa ulamuliro pamodzi ndi chirombo kwa ora limodzi. 13Mafumuwo ali ndi cholinga chimodzi ndipo adzapereka mphamvu ndi ulamuliro wawo kwa chirombocho. 14Iwo adzachita nkhondo ndi Mwana Wankhosa, koma Mwana Wankhosayo adzawagonjetsa chifukwa Iye ndi Mbuye wa ambuye ndi Mfumu ya mafumu, ndipo amene adzakhala ndi Iye ndi oyitanidwa ake, osankhidwa ndi otsatira ake okhulupirika.”

15Kenaka mngeloyo anati kwa ine, “Madzi amene unawaona pamene mkazi wadamayo anakhalapo ndiwo anthu ochuluka, mitundu ndi ziyankhulo. 16Nyanga khumi ndi chirombo unazionazo zidzadya mkazi wadamayo. Zidzamufwifwitsa ndi kumusiya wamaliseche; zidzadya nyama yake ndi kumutentha ndi moto. 17Pakuti Mulungu wayika ichi mʼmitima mwawo kuti akwaniritse cholinga chake povomerezana kupereka mphamvu zawo zolamulira kwa chirombo, kufikira Mawu a Mulungu atakwaniritsidwa. 18Mkazi unamuonayo ndi mzinda waukulu umene ulamulira mafumu a dziko lapansi.”

New Russian Translation

Откровение 17:1-18

Суд над Вавилоном

1Один из семи ангелов, у которых было семь чаш, подошел ко мне и сказал:

– Подойди, я покажу тебе, как будет наказана великая блудница, сидящая на многих водах17:1 См. Иер. 51:13.. 2С ней развратничали цари земли, и жители земли упивались вином ее разврата.

3И он перенес меня в духе в пустыню, и я увидел женщину, сидящую на алом звере, который был исписан кощунственными именами; у него было семь голов и десять рогов. 4Женщина была одета во все пурпурное и алое, была украшена золотом, драгоценными камнями и жемчугом. В руке у нее была золотая чаша, наполненная мерзостью и нечистотами ее разврата. 5На лбу у нее написано имя, имеющее тайное значение:

Великий Вавилон

мать блудниц

и мерзостей земли.

6И я увидел, что женщина была пьяна от крови святых, от крови свидетелей Иисуса. Я был поражен, когда ее увидел.

7Ангел сказал мне:

– Чему ты удивляешься? Я тебе скажу, в чем заключается тайна женщины и зверя с семью головами и десятью рогами, на котором она сидит. 8Зверь, которого ты видел, был и нет его. Он выйдет из бездны и отправится в погибель. Жители земли, имена которых от начала мира не были записаны в книге жизни, удивятся, глядя на зверя, потому что он был и нет его, и еще придет.

9Это требует понимания и мудрости. Семь голов – это семь гор17:9 Горы часто символизировали царства этого мира., на которых сидит женщина, 10и семь царей, пять из которых уже пали, один есть, а другой еще не пришел, а когда придет – то ненадолго. 11Зверь, который был и которого нет, – это восьмой царь, и он из числа семи, и идет к погибели.

12Десять рогов, которые ты видел, – это десять царей, еще не получивших своего царства, но вместе со зверем они на один час получат царскую власть17:12 См. Дан. 7:23-24.. 13У них одна общая цель, и они отдадут свою силу и власть зверю. 14Они будут сражаться с Ягненком, но Ягненок одержит над ними победу, потому что Он Господь господствующих17:14 См. Втор. 10:17; Пс. 135:3. и Царь царей и с Ним Его избранные, призванные и верные.

15Потом ангел сказал мне:

– Воды, которые ты видел там, где сидит блудница, – это народы, скопления людей, племена и языки. 16Зверь и десять рогов, которые ты видел, возненавидят блудницу. Они разорят ее, оставят нагой, будут поедать ее тело и жечь ее в огне. 17Потому что Бог внушил этим десяти рогам желание исполнить Его волю и единодушно отдать зверю их царскую власть до тех пор, пока не исполнятся Божьи слова. 18Женщина, которую ты видел, – это великий город, царствующий над всеми царями земли.