Chivumbulutso 14 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 14:1-20

Mwana Wankhosa ndi Anthu 144,000

1Kenaka ndinaona patsogolo panga panali Mwana Wankhosa, atayimirira pa Phiri la Ziyoni, ndipo Iye anali pamodzi ndi anthu 144,000 amene pa mphumi pawo panalembedwa dzina la Mwana Wankhosayo ndi la Atate ake. 2Ndipo ndinamva liwu lochokera kumwamba ngati mkokomo wa madzi ambiri, ndiponso ngati kugunda kwamphamvu kwa bingu. Liwu limene ndinamvalo linali ngati a anthu akuyimba azeze awo. 3Anthuwo ankayimba nyimbo yatsopano patsogolo pa mpando waufumu ndi zamoyo zinayi zija ndi akuluakulu aja. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatha kuphunzira nyimboyo kupatula anthu 144,000 aja amene anawomboledwa pa dziko lapansi. 4Awa ndiwo amene sanadzidetse koma anadzisunga ndipo sanadziyipitse ndi akazi. Anthu amenewa ndiwo ankatsatira Mwana Wankhosa kulikonse kumene ankapita. Ndiwo amene anagulidwa pakati pa anthu a dziko lapansi kuti akhale oyambirira kuperekedwa kwa Mulungu ndi kwa Mwana Wankhosa. 5Iwo sananenepo bodza ndipo alibe cholakwa.

Angelo Atatu

6Kenaka ndinaona mngelo wina akuwuluka mu mlengalenga ndipo anali ndi Uthenga Wabwino wamuyaya woti akalalikire kwa anthu okhala pa dziko lapansi, kwa a mtundu uliwonse, a fuko lililonse, a chiyankhulo chilichonse ndi kwa anthu onse. 7Mngeloyo anayankhula mokweza mawu kuti, “Wopani Mulungu ndi kumutamanda, chifukwa nthawi yoweruza anthu yafika. Mumupembedze Iye amene analenga thambo, dziko lapansi, nyanja ndi akasupe amadzi.”

8Mngelo wachiwiri anatsatana naye ndipo anati, “Wagwa! Wagwa Babuloni womveka uja, amene anachititsa anthu a mitundu yonse kumwa vinyo wa zilakolako zake zachigololo.”

9Mngelo wachitatu anatsatana nawo ndi mawu ofuwula anati, “Ngati wina apembedza chirombo chija ndi fano lake ndi kulembedwa chizindikiro pa mphumi kapena pa dzanja, 10nayenso adzamwa vinyo waukali wa Mulungu, umene wathiridwa popanda kuchepetsa mphamvu zake mʼchikho cha ukali wa Mulungu. Munthuyo adzazunzidwa ndi moto wamiyala yasulufure pamaso pa angelo oyera ndi pa Mwana Wankhosa. 11Ndipo utsi wa moto wowazunzawo udzakwera kumwamba mpaka muyaya. Sikudzakhala kupumula usana ndi usiku kwa amene anapembedza chirombo chija ndi fano lake kapena kwa aliyense amene analembedwa chizindikiro cha dzina lake lija.” 12Pamenepa ndi pofunika kupirira kwa anthu oyera mtima amene amasunga malamulo a Mulungu ndi kukhalabe okhulupirika kwa Yesu.

13Kenaka ndinamva mawu kuchokera kumwamba akuti, “Lemba kuti, Odala anthu amene akufa ali mwa Ambuye kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo.”

“Inde,” akutero Mzimu, “akapumule ntchito zawo zotopetsa pakuti ntchito zawo zidzawatsata.”

Zokolola za Dziko la Pansi

14Ndinayangʼana patsogolo panga ndinaona mtambo woyera patakhalapo wina ngati Mwana wa Munthu, kumutu atavala chipewa chaufumu chagolide ndipo mʼdzanja mwake munali chikwakwa chakunthwa. 15Tsono mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu nafuwula mwamphamvu kwa uja wokhala pa mtamboyu. Mngeloyo anati, “Tenga chikwakwa chako ndipo kolola, pakuti nthawi yokolola ya dziko la pansi yakwana” 16Choncho wokhala pa mtambo uja anayamba kukolola dzinthu pa dziko lapansi ndi chikwakwa chakecho.

17Mngelo wina anatuluka mʼNyumba ya Mulungu kumwamba ndipo nayenso anali ndi chikwakwa chakunthwa. 18Kenaka mngelo winanso amene amalamulira moto, anatuluka kuchokera ku guwa lansembe nayitana mwamphamvu mngelo uja amene anali ndi chikwakwa chakunthwa chija, nati, “Tenga chikwakwa chako chakunthwacho yamba kudula mphesa za mʼmunda wamphesa wa pa dziko lapansi, pakuti mphesa zapsa kale.” 19Pamenepo mngeloyo anayambadi kugwiritsa ntchito chikwakwa chake nadula mphesa za dziko lapansi, naziponya mʼchopondera mphesa chachikulu cha ukali woopsa wa Mulungu. 20Mphesazo zinapondedwa mʼchopondera mphesa kunja kwa mzinda. Mʼchopondera mphesamo munatuluka magazi amene anayenderera ngati mtsinje, kuzama kwake mita ndi theka ndipo kutalika kwake makilomita 300.

New Russian Translation

Откровение 14:1-20

Новая песнь на горе Сион

1Я посмотрел и увидел Ягненка. Он стоял на горе Сион14:1 Гора Сион – возвышенность в восточной части Иерусалима, на которой был построен храм Бога (см. Пс. 47:2-3). Позднее слово «Сион» стало синонимом Иерусалима (см. 4 Цар. 19:31). Также в Писании гора Сион упоминается в связи с небесным Иерусалимом (см. Евр. 12:22)., и с Ним было сто сорок четыре тысячи человек, у которых на лбу было написано имя Ягненка и имя Его Отца. 2Я слышал шум с небес, он напоминал одновременно шум могучих вод, раскаты сильного грома и звук, который производят арфисты, играющие на своих арфах. 3Они поют новую песнь перед троном, перед четырьмя живыми существами и перед старцами. Эту песнь не мог никто выучить, кроме ста сорока четырех тысяч искупленных с земли. 4Это были те, кто не осквернил себя с женщинами, оставшись девственниками14:4 Вероятно, этот образ символизирует духовную чистоту этих людей – они не осквернились развратной жизнью и поклонением зверю.. Они всюду шли за Ягненком, куда бы Он ни шел. Они были искуплены из всего человечества и освящены как первые плоды14:4 Первые плоды – первый урожай, первенцы животных и людей в древности считались священными и посвящались Богу (см., напр., Исх. 13:1-2; Лев. 23:9-14; Чис. 3:12; 15:20-21; Втор. 15:19-20; 26:1-11). для Бога и Ягненка. 5В их словах не нашлось никакой лжи, они непорочны14:5 См. Соф. 3:13..

Три ангела

6Потом я увидел еще одного ангела, летящего посреди неба. У него была Радостная Весть, которая вечна, чтобы провозгласить ее живущим на земле – всем племенам, родам, языкам и народам.

7– Бойтесь Бога, – громко говорил ангел, – и воздайте Ему славу, потому что наступил час суда Его. Поклонитесь Создавшему небо и землю, море и источники вод14:7 См. Исх. 20:11; Пс. 145:6..

8За ним следовал второй ангел. Он говорил:

– Пал, пал великий Вавилон!14:8 См. Ис. 21:9. Он напоил все народы доводящим до безумия вином своего разврата14:8 См. Ис. 13:19-22; Иер. 50:39; 51:6-8..

9Вслед за ними последовал третий ангел. Он громко говорил:

– Кто поклоняется зверю и его изображению и кто принимает клеймо на свой лоб или на руку, 10тот будет пить вино Божьей ярости, вино неразбавленное, приготовленное в чаше Его гнева, и будет мучиться в горящей сере на глазах у святых ангелов и Ягненка. 11Для поклоняющихся зверю и его изображению и для принявших клеймо с его именем не будет покоя ни днем, ни ночью, и дым их мучений будет подниматься вечно14:11 См. Ис. 34:10.. 12Здесь от святых, соблюдающих повеления Божьи и верящих в Иисуса, требуется терпение.

13И я услышал с небес голос:

– Запиши: отныне блаженны те, кто умирает с верой в Господа.

– Да, – говорит Дух, – теперь они отдохнут от своих трудов, и их дела следуют за ними.

Жатва на земле

14Я посмотрел и увидел белое облако. На облаке сидел Некто, «как бы Сын Человеческий»14:14 Или: «некто, похожий на человека». Здесь, очевидно, говорится об Иисусе; выражение «как бы Сын Человеческий» перекликается с видением пророка Даниила, который увидел превознесенного Царя, Чье Царство вечно (см. Дан. 7:13). Когда Иисус называл Себя Сыном Человеческим, см., напр., Мат. 8:20, Он недвусмысленно давал понять, что Он и есть Тот Самый Царь из видения пророка Даниила, т. е. Мессия.. На Его голове был золотой венец, и в руке Он держал острый серп. 15Затем из храма вышел еще один ангел и громко сказал Сидящему на облаке:

– Пошли Свой серп и пожни, потому что время жатвы уже настало и урожай на земле уже созрел.

16Тогда Сидящий на облаке бросил Свой серп на землю, и на земле был собран урожай.

17Потом из небесного храма вышел еще один ангел, у него тоже в руке был острый серп. 18И еще один ангел вышел от жертвенника, где он заведовал огнем. Он громко крикнул ангелу, у которого был острый серп:

– Пошли твой острый серп и собери грозди винограда с виноградника земли, потому что ягоды его уже созрели.

19Ангел бросил свой серп на землю, собрал виноград и кинул его в великую давильню14:19 Давильня – в те времена виноград давили в специальных углублениях, высеченных в скале, откуда сок вытекал через специальное отверстие. Божьей ярости. 20Виноград был потоптан в давильне, которая за городом, и из нее рекой потекла кровь. Эта река крови была длиной в тысячу шестьсот стадий14:20 То есть около 300 км. и по глубине достигала коням до уздечек14:17-20 См. Ис. 63:1-6; Иоиль 3:13..