Chivumbulutso 12 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 12:1-18

Mayi ndi Chinjoka

1Chizindikiro chachikulu chinaoneka kuthambo; mayi atavala dzuwa, mapazi ake ataponda mwezi, pamutu pake pali chipewa chaufumu chokhala ndi nyenyezi khumi ndi ziwiri. 2Mayiyo anali woyembekezera ndipo pa nthawi yake yochira analira mokuwa chifukwa cha ululu wakubala. 3Kenaka ku thambo kunaonekanso chizindikiro china; chinjoka chachikulu kwambiri, chofiira chomwe chinali ndi mitu isanu ndi iwiri ndi nyanga khumi; pamutu uliwonse chitavala chipewa chaufumu. 4Mchira wake unakokolola gawo limodzi la magawo atatu a nyenyezi kuzichotsa ku thambo ndi kuziponya pa dziko lapansi. Chinjoka chija chinadzayima patsogolo pa mayi uja amene anali pafupi kuberekayu kuti mwanayo akangobadwa chimudye. 5Mayiyo anabereka mwana wamwamuna amene adzalamulira anthu a mitundu ina yonse ndi ndodo yachitsulo. Ndipo mwanayo analandidwa ku dzanja la mayiyo ndi kupita naye kwa Mulungu ku mpando wake waufumu. 6Mayiyo anathawira ku chipululu ku malo kumene Mulungu anamukonzera, kumene akasamalidweko masiku 1,260.

7Zitatero, kumwamba kunayambika nkhondo. Mikayeli ndi angelo ake kumenyana ndi chinjoka chija. Chinjokacho ndi angelo ake anabwezeranso. 8Koma analibe mphamvu ndipo anagonjetsedwa nathamangitsidwa kumwambako. 9Chinjoka chachikulu chija chinagwetsedwa pansi. Ichocho ndiye njoka yakalekale ija yotchedwa Mdierekezi kapena Satana, amene amasocheretsa anthu a pa dziko lonse lapansi. Chinaponyedwa pa dziko la pansi pamodzi ndi angelo ake.

10Kenaka ndinamva mawu ofuwula kumwamba akunena kuti,

“Tsopano chipulumutso, mphamvu,

ufumu wa Mulungu wathu

ndi ulamuliro wa Khristu wake zabwera.

Pakuti woneneza abale athu uja,

amene amangokhalira kuwaneneza pamaso pa Mulungu usana ndi usiku,

wagwetsedwa pansi.

11Abale athuwo anamugonjetsa

ndi magazi a Mwana Wankhosa

ndiponso mawu a umboni wawo.

Iwo anadzipereka kwathunthu,

moti sanakonde miyoyo yawo.

12Choncho, kondwerani, inu dziko lakumwamba

ndi onse okhala kumeneko!

Koma tsoka dziko lapansi ndi nyanja

chifukwa Mdierekezi wagwetsedwa kwa inu!

Iye wadzazidwa ndi ukali

chifukwa akudziwa kuti nthawi yake ndi yochepa.”

13Pamene chinjokacho chinaona kuti chagwetsedwa pa dziko lapansi, chinayamba kuthamangitsa mayi uja amene anali atabala mwana wamwamunayu. 14Mayiyo anapatsidwa mapiko awiri a chiwombankhanga chachikulu kuti athawire ku malo ake aja a ku chipululu. Kumeneko adzasamalidwako zaka zitatu ndi theka kuti chinjoka chija chisamupeze. 15Kenaka chinjoka chija chinalavulira mayiyo madzi ambiri ngati mtsinje, kuti madziwo amukokolole. 16Koma dziko lapansi linamuthandiza mayiyo. Nthaka inatsekuka ndi kumeza mtsinje uja unachokera mʼkamwa mwa chinjokacho. 17Pamenepo chinjokacho chinamupsera mtima mayiyo ndipo chinachoka kupita kukachita nkhondo ndi ana ena onse a mayiyo, ndiye kuti anthu amene anasunga malamulo a Mulungu ndi kuchitira umboni za Yesu.

18Kenaka ndinaona chinjokacho chitayima mʼmbali mwa nyanja.

Nova Versão Internacional

Apocalipse 12:1-18

A Mulher e o Dragão

1Apareceu no céu um sinal extraordinário: uma mulher vestida do sol, com a lua debaixo dos seus pés e uma coroa de doze estrelas sobre a cabeça. 2Ela estava grávida e gritava de dor, pois estava para dar à luz. 3Então apareceu no céu outro sinal: um enorme dragão vermelho com sete cabeças e dez chifres, tendo sobre as cabeças sete coroas12.3 Grego: diademas.. 4Sua cauda arrastou consigo um terço das estrelas do céu, lançando-as na terra. O dragão pôs-se diante da mulher que estava para dar à luz, para devorar o seu filho no momento em que nascesse. 5Ela deu à luz um filho, um homem, que governará todas as nações com cetro de ferro. Seu filho foi arrebatado para junto de Deus e de seu trono. 6A mulher fugiu para o deserto, para um lugar que lhe havia sido preparado por Deus, para que ali a sustentassem durante mil duzentos e sessenta dias.

7Houve então uma guerra nos céus. Miguel e seus anjos lutaram contra o dragão, e o dragão e os seus anjos revidaram. 8Mas estes não foram suficientemente fortes, e assim perderam o seu lugar nos céus. 9O grande dragão foi lançado fora. Ele é a antiga serpente chamada Diabo ou Satanás, que engana o mundo todo. Ele e os seus anjos foram lançados à terra.

10Então ouvi uma forte voz dos céus, que dizia:

“Agora veio a salvação,

o poder e o Reino do nosso Deus,

e a autoridade do seu Cristo,

pois foi lançado fora o acusador dos nossos irmãos,

que os acusa diante do nosso Deus, dia e noite.

11Eles o venceram

pelo sangue do Cordeiro

e pela palavra do testemunho que deram;

diante da morte,

não amaram a própria vida.

12Portanto, celebrem-no, ó céus,

e os que neles habitam!

Mas ai da terra e do mar,

pois o Diabo desceu até vocês!

Ele está cheio de fúria,

pois sabe que lhe resta pouco tempo”.

13Quando o dragão foi lançado à terra, começou a perseguir a mulher que dera à luz o menino. 14Foram dadas à mulher as duas asas da grande águia, para que ela pudesse voar para o lugar que lhe havia sido preparado no deserto, onde seria sustentada durante um tempo, tempos e meio tempo, fora do alcance da serpente. 15Então a serpente fez jorrar da sua boca água como um rio, para alcançar a mulher e arrastá-la com a correnteza. 16A terra, porém, ajudou a mulher, abrindo a boca e engolindo o rio que o dragão fizera jorrar da sua boca. 17O dragão irou-se contra a mulher e saiu para guerrear contra o restante da sua descendência, os que obedecem aos mandamentos de Deus e se mantêm fiéis ao testemunho de Jesus.

18Então o dragão se pôs em pé12.18 Alguns manuscritos dizem E eu estava em pé. na areia do mar.