Chivumbulutso 1 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chivumbulutso 1:1-20

Mawu Oyamba

1Vumbulutso lochokera kwa Yesu Khristu, limene Mulungu anamupatsa kuti aonetse atumiki ake zimene zinayenera kuchitika posachedwa. Iye anatuma mngelo wake kuti adziwitse mtumiki wake Yohane, 2amene akuchitira umboni chilichonse chimene anachiona. Awa ndi Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu Khristu. 3Ngodala munthu amene awerenga mawu oneneratu zamʼtsogolo ndi iwo amene amamva ndi kusunga zolembedwa mʼbukuli pakuti nthawi yayandikira.

Malonje kwa Mipingo Isanu ndi Iwiri

4Ndine Yohane,

Kupita ku mipingo isanu ndi iwiri ya mʼchigawo cha Asiya.

Chisomo ndi mtendere kwa inu, kuchokera kwa Iye amene ali, amene analipo ndi amene akubwera ndi kwa mizimu isanu ndi iwiri yokhala patsogolo pa mpando wake waufumu, 5ndiponso kuchokera kwa Yesu Khristu mboni yokhulupirika, woyamba kuukitsidwa, ndi wolamulira mafumu a dziko lapansi.

Kwa Iye amene amatikonda ndipo watimasula ku machimo athu ndi magazi ake, 6ndipo watisandutsa mafumu ndi ansembe kuti tizitumikira Mulungu ndi Atate ake. Kwa Iye kukhale ulemerero ndi mphamvu ku nthawi zosatha, Ameni.

7“Onani akubwera ndi mitambo,”

ndipo “Aliyense adzamuona,

ndi amene anamubaya omwe.”

Ndipo anthu a mitundu yonse ya pa dziko lapansi “adzalira chingʼangʼadza chifukwa cha Iye.”

Zidzakhaladi momwemo, Ameni.

8“Ine ndine Alefa ndi Omega,” akutero Ambuye Mulungu Wamphamvuzonseyo “amene muli, amene munalipo, ndi amene mudzakhalapo.”

Wina Wokhala ngati Mwana wa Munthu

9Ine Yohane mʼbale wanu ndi mnzanu mʼmasautso ndi mu ufumu ndi mukupirira kwambiri, zomwe ndi zathu mwa Yesu, ndinali pa chilumba cha Patimo chifukwa cha Mawu a Mulungu ndi umboni wa Yesu. 10Pa tsiku la Ambuye ndinanyamulidwa ndi Mzimu ndipo ndinamva kumbuyo kwanga mawu ofuwula ngati lipenga, 11amene anati, “Lemba mʼbuku zimene ukuziona ndipo uzitumize ku mipingo isanu ndi iwiri ya ku Efeso, Simurna, Pergamo, Tiyatira, Sarde, Filadefiya ndi ku Laodikaya.”

12Nditatembenuka kuti ndione amene amandiyankhulayo, ndinaona zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zagolide. 13Pakati pa zoyikapo nyalezo ndinaona wina wooneka ngati Mwana wa Munthu atavala mkanjo wofika kumapazi ake ndipo anamangirira lamba wagolide pa chifuwa pake. 14Tsitsi lake linali loyera ngati thonje, kuyera ngati matalala, ndipo maso ake amawala ngati malawi amoto. 15Mapazi ake anali ngati chitsulo choti chili mʼngʼanjo yamoto, ndipo mawu ake anali ngati mkokomo wamadzi othamanga. 16Mʼdzanja lake lamanja ananyamula nyenyezi zisanu ndi ziwiri, ndipo mʼkamwa mwake munali lupanga lakuthwa konsekonse. Nkhope yake imawala ngati dzuwa lowala kwambiri.

17Nditamuona ndinagwa pa mapazi ake ngati wakufa. Kenaka Iye anasanjika dzanja lake lamanja pa ine nati, “Usachite mantha. Ndine Woyamba ndi Wotsiriza. 18Ine ndine Wamoyo; ndinali wakufa ndipo taona ndine wamoyo mpaka muyaya! Ndipo ndili ndi makiyi a imfa ndi Hade.

19“Chomwecho, lemba zimene waona, zimene zilipo panopa ndi zimene zidzachitike mʼtsogolo. 20Tanthauzo la nyenyezi zisanu ndi ziwiri zimene waziona mʼdzanja langa lamanja ndi la zoyikapo nyale zagolide zisanu ndi ziwiri ndi ili: Nyenyezi zisanu ndi ziwiri ndi angelo a mipingo isanu ndi iwiri ija, ndipo zoyikapo nyale zisanu ndi ziwiri zija ndi mipingo isanu ndi iwiri ija.”

Słowo Życia

Apokalipsa 1:1-20

Wstęp

1Oto objawienie, które Bóg przekazał Jezusowi Chrystusowi, aby powiedział On swoim sługom o tym, co ma się wkrótce wydarzyć. Jezus wysłał więc anioła, aby ten przekazał to objawienie Jego słudze, Janowi. 2On zaś przekazał innym słowo Boże oraz to, czego dowiedział się od Jezusa Chrystusa.

3Szczęśliwy jest ten, kto czyta, i ci, którzy słuchają słów tego proroctwa. Niech zwrócą uwagę na jego treść, bo niedługo wszystko to się wypełni.

Pozdrowienia

4Ja, Jan, piszę do siedmiu kościołów, znajdujących się w prowincji Azja. Niech Bóg, który był, jest i nadchodzi, obdarza was swoją łaską i pokojem! Tą samą łaską i pokojem niech obdarzy was siedem Duchów, obecnych przy Jego tronie, 5oraz Jezus Chrystus, który jest godnym zaufania świadkiem! On jest pierwszym, który zmartwychwstał. On panuje również nad wszystkimi władcami świata. Chrystus kocha nas tak bardzo, że przelał za nas swoją krew i w ten sposób uwolnił nas od grzechów. 6On sprawił również, że staliśmy się członkami królewskiej rodziny i kapłanami samego Boga Ojca. Jemu należy się wieczna chwała oraz władza. Amen!

7On, już niebawem, nadejdzie wśród obłoków

i zobaczą Go wszyscy ludzie,

nawet ci, którzy Go przebili.

Wówczas wszystkie narody świata

będą płakać z Jego powodu.

Wszystko to się naprawdę wydarzy! Amen!

8Bóg, który jest Wszechmocnym Panem, mówi: „Ja jestem Alfa i Omega”. On był, jest i nadchodzi!

Wizja Chystusa

9Ja, Jan, wasz przyjaciel i towarzysz w cierpieniu, a także współobywatel Bożego królestwa, nieugięcie trzymający się Pana, zostałem zesłany na wyspę Patmos za głoszenie ludziom słowa Bożego i opowiadanie im o Jezusie. 10Pewnego razu, w dzień Pański, ogarnął mnie Duch Święty i usłyszałem za sobą potężny głos, brzmiący jak dźwięk trąby:

11—Zapisz w księdze wszystko, co widzisz, a następnie wyślij ją do siedmiu kościołów: do Efezu, Smyrny, Pergamonu, Tiatyry, Sardes, Filadelfii i Laodycei.

12Gdy się odwróciłem, aby zobaczyć, czyj to głos, ujrzałem siedem złotych świeczników, 13a między nimi kogoś, kto wyglądał jak Syn Człowieczy. Był ubrany w długą szatę i przepasany na piersiach złotym pasem. 14Jego głowa i włosy były białe jak śnieżnobiała wełna, a spojrzenie—przenikające jak płomień ognia. 15Jego stopy lśniły jak rozgrzany w piecu mosiądz, a głos brzmiał jak huk fal. 16W prawej ręce trzymał siedem gwiazd, a z Jego ust wychodził ostry, obosieczny miecz. Jego twarz lśniła jak słońce w pełnym blasku.

17Gdy Go ujrzałem, padłem jak martwy u Jego stóp. Ale On dotknął mnie swoją prawą ręką i rzekł:

—Nie bój się! Jestem Pierwszy i Ostatni. 18Umarłem, ale ożyłem i będę żyć wiecznie. Mam klucze do świata zmarłych. 19Zapisz to, co już zobaczyłeś, co jest teraz oraz co się wydarzy potem. 20Siedem gwiazd w mojej prawej dłoni to aniołowie siedmiu kościołów, a siedem złotych świeczników to siedem kościołów.