Aroma 9 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aroma 9:1-33

Chisankho Chopambana cha Mulungu

1Ine ndikunena zoona mwa Khristu. Sindikunama ndipo chikumbumtima changa kudzera mwa Mzimu Woyera chikundichitira umboni. 2Ndili ndi chisoni chachikulu ndipo ndikumva kupwetekeka kosalekeza mu mtima mwanga. 3Pakuti ndikanafuna ine mwini nditatembereredwa ndi kuchotsedwa mwa Khristu chifukwa cha abale anga, amene ndi a mtundu wanga, 4anthu Aisraeli. Iwo anasankhidwa kukhala ana. Mulungu anawapatsa ulemerero, anachita nawo mapangano, kuwapatsa Malamulo, Nyumba yopembedzeramo ndi malonjezano ake. 5Awo ndi makolo athu. Kuchokera kwa iwo mʼthupi ndi kumene kunachokera makolo a Khristu Yesu amene ndi Mulungu wolamulira zinthu zonse, alemekezeke mpaka muyaya! Ameni.

6Sikuti mawu a Mulungu analephera. Pakuti si onse obadwa mwa Israeli amene ndi Israeli. 7Kapena kuti ana ake chifukwa anachokera mwa Abrahamu. Koma zidzukulu zako zidzachokera mwa Isake. 8Kutanthauza kuti, si ana obadwa mʼthupi amene ndi ana a Mulungu koma ndi ana a lonjezano amene amatengedwa kukhala zidzukulu za Abrahamu. 9Pakuti Mulungu analonjeza ponena kuti, “Pa nthawi yake ngati yomwe ino chaka chamawa ndidzabweranso, ndipo Sara adzakhala ndi mwana wamwamuna.”

10Ndipo si pokhapo ayi. Ana awiri a Rebeka aja abambo awo anali mmodzi, kholo lathu Isake. 11Komabe, ana amapasawa asanabadwe kapena asanachite chilichonse chabwino kapena choyipa, nʼcholinga choti chifuniro cha Mulungu chosankhiratu munthu aliyense chipitirire, 12osati chifukwa cha ntchito za munthu koma chifuniro cha Iye mwini, anawuza Rebeka kuti, “Wamkulu adzatumikira wamʼngʼono.” 13Monga momwe kwalembedwa kuti, “Ine ndinakonda Yakobo, koma ndinamuda Esau.”

14Nanga tsono tidzanena chiyani? Kodi Mulungu ndi osalungama? Ayi, ndi pangʼono pomwe! 15Pakuti Mulungu anawuza Mose kuti,

“Ine ndidzachitira chifundo amene ndikufuna kumuchitira chifundo,

ndipo ndidzakomera mtima amene ndikufuna kumukomera mtima.”

16Nʼchifukwa chake, izi sizitengera zokhumba za munthu kapena kuyesetsa koma chifundo cha Mulungu. 17Malemba akuti Mulungu anamuwuza Farao kuti, “Ine ndakuyika kukhala mfumu ndi cholinga choti ndionetse mphamvu zanga, kuti mwa iwe dzina langa litchuke pa dziko lonse lapansi.” 18Choncho Mulungu amachitira chifundo munthu amene akufuna kumuchitira chifundo ndipo amawumitsa mtima munthu amene Iye akufuna kumuwumitsa mtima.

19Tsono mmodzi wa inu nʼkundifunsa kuti, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mulungu amatipeza olakwa? Nanga ndani amene amakana chifuniro chake?” 20Koma ndiwe yani, munthu wamba, woti nʼkutsutsana ndi Mulungu? “Kodi chimene chinawumbidwa nʼkufunsa amene anachiwumba kuti, ‘Kodi unandiwumbiranji motere?’ ” 21Kodi wowumba alibe ufulu wowumba kuchokera ku dothi lomwelo mbiya yamtengowapatali ndi ina yamtengo wotsika?

22Koma Mulungu, anafuna kuonetsa mkwiyo wake ndi kuti mphamvu yake idziwike. Iye anapirira modekha mtima kwambiri zochita za anthu omwe anawakwiyirawo amene anayeneradi chiwonongeko. 23Iye anachita izi kufuna kuonetsa kulemera kwa ulemerero wake ndi kuti udziwike kwa amene analandira chifundo chake. Iye anawakonzeratu kuti alandire ulemerero wake 24ngakhale ifenso amene anatiyitana osati kuchokera kwa Ayuda okha komanso kwa a mitundu ina. 25Monga momwe Mulungu akunenera mʼbuku la Hoseya kuti,

“Amene sanali anthu anga ndidzawatcha ‘anthu anga;’

ndipo Ine ndidzatcha ‘wokondedwa wanga’ amene sali wokondedwa wanga,”

26ndipo,

“Pamalo omwewo pamene ananena kuti,

‘Sindinu anthu anga,’

pomweponso adzawatchula kuti, ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ ”

27Yesaya anafuwula za Aisraeli kuti,

“Ngakhale chiwerengero cha Aisraeli chingakhale ngati mchenga wa ku nyanja,

otsala okha ndiye adzapulumuke.

28Pakuti Ambuye adzagamula milandu

ya anthu pa dziko lapansi mofulumira ndi kumaliziratu.”

29Monga momwe Yesaya ananena malo ena kuti,

“Ngati Yehova Wamphamvuzonse

akanapanda kutisiyira zidzukulu,

ife tikanawonongeka

ngati anthu a ku Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.”

Kusakhulupirira kwa Aisraeli

30Kodi nanga tidzati chiyani? Tidzati a mitundu ina amene sanafune chilungamo analandira chilungamo chachikhulupiriro 31koma Aisraeli, amene anafuna chilungamo cha lamulo sanachilandire. 32Chifukwa chiyani? Chifukwa iwo sanachifune ndi chikhulupiriro koma ngati mwa ntchito. Iwo anapunthwa pa “Mwala wopunthwitsa.” 33Monga momwe kwalembedwa kuti,

“Taonani, Ine ndikuyika mwala mu Ziyoni wopunthwitsa anthu,

thanthwe limene limagwetsa anthu.

Koma amene akhulupirira Iye sadzachititsidwa manyazi.”

Nova Versão Internacional

Romanos 9:1-33

A Soberania de Deus

1Digo a verdade em Cristo, não minto; minha consciência o confirma no Espírito Santo: 2tenho grande tristeza e constante angústia em meu coração. 3Pois eu até desejaria ser amaldiçoado e separado de Cristo por amor de meus irmãos, os de minha raça, 4o povo de Israel. Deles é a adoção de filhos; deles são a glória divina, as alianças, a concessão da Lei, a adoração no templo e as promessas. 5Deles são os patriarcas, e a partir deles se traça a linhagem humana de Cristo, que é Deus acima de todos, bendito para sempre!9.5 Ou Cristo, que é sobre tudo. Seja Deus louvado para sempre! Amém.

6Não pensemos que a palavra de Deus falhou. Pois nem todos os descendentes de Israel são Israel. 7Nem por serem descendentes de Abraão passaram todos a ser filhos de Abraão. Ao contrário: “Por meio de Isaque a sua descendência será considerada”9.7 Gn 21.12. 8Noutras palavras, não são os filhos naturais9.8 Grego: da carne. que são filhos de Deus, mas os filhos da promessa é que são considerados descendência de Abraão. 9Pois foi assim que a promessa foi feita: “No tempo devido virei novamente, e Sara terá um filho”9.9 Gn 18.10,14.

10E esse não foi o único caso; também os filhos de Rebeca tiveram um mesmo pai, nosso pai Isaque. 11Todavia, antes que os gêmeos nascessem ou fizessem qualquer coisa boa ou má—a fim de que o propósito de Deus conforme a eleição permanecesse, 12não por obras, mas por aquele que chama—, foi dito a ela: “O mais velho servirá ao mais novo”9.12 Gn 25.23. 13Como está escrito: “Amei Jacó, mas rejeitei Esaú”9.13 Ml 1.2,3.

14E então, que diremos? Acaso Deus é injusto? De maneira nenhuma! 15Pois ele diz a Moisés:

“Terei misericórdia de quem eu quiser ter misericórdia

e terei compaixão de quem eu quiser ter compaixão”9.15 Êx 33.19.

16Portanto, isso não depende do desejo ou do esforço humano, mas da misericórdia de Deus. 17Pois a Escritura diz ao faraó: “Eu o levantei exatamente com este propósito: mostrar em você o meu poder e para que o meu nome seja proclamado em toda a terra”9.17 Êx 9.16. 18Portanto, Deus tem misericórdia de quem ele quer e endurece a quem ele quer.

19Mas algum de vocês me dirá: “Então, por que Deus ainda nos culpa? Pois quem resiste à sua vontade?” 20Mas quem é você, ó homem, para questionar a Deus? “Acaso aquilo que é formado pode dizer ao que o formou: ‘Por que me fizeste assim?’9.20 Is 29.16; 45.921O oleiro não tem direito de fazer do mesmo barro um vaso para fins nobres e outro para uso desonroso?

22E se Deus, querendo mostrar a sua ira e tornar conhecido o seu poder, suportou com grande paciência os vasos de sua ira, preparados9.22 Ou prontos para a destruição? 23Que dizer, se ele fez isso para tornar conhecidas as riquezas de sua glória aos vasos de sua misericórdia, que preparou de antemão para glória, 24ou seja, a nós, a quem também chamou, não apenas dentre os judeus, mas também dentre os gentios? 25Como ele diz em Oseias:

“Chamarei ‘meu povo’ a quem não é meu povo;

e chamarei ‘minha amada’ a quem não é minha amada”9.25 Os 2.23,

26e:

“Acontecerá que, no mesmo lugar em que se lhes declarou:

‘Vocês não são meu povo’,

eles serão chamados ‘filhos do Deus vivo’ ”9.26 Os 1.10.

27Isaías exclama com relação a Israel:

“Embora o número dos israelitas seja como a areia do mar,

apenas o remanescente será salvo.

28Pois o Senhor executará na terra a sua sentença,

rápida e definitivamente”9.27,28 Is 10.22,23.

29Como anteriormente disse Isaías:

“Se o Senhor dos Exércitos

não nos tivesse deixado descendentes,

já estaríamos como Sodoma,

e semelhantes a Gomorra”9.29 Is 1.9.

A Incredulidade de Israel

30Que diremos, então? Os gentios, que não buscavam justiça, a obtiveram, uma justiça que vem da fé; 31mas Israel, que buscava uma lei que trouxesse justiça, não a alcançou. 32Por que não? Porque não a buscava pela fé, mas como se fosse por obras. Eles tropeçaram na “pedra de tropeço”. 33Como está escrito:

“Eis que ponho em Sião uma pedra de tropeço

e uma rocha que faz cair;

e aquele que nela confia jamais será envergonhado”9.33 Is 8.14; 28.16.